< Ezekieli 2 >

1 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
Et il me fut dit: Fils de l'homme, tiens-toi sur tes pieds, et je te parlerai.
2 Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
Dès qu'il m'eut parlé, l'Esprit entra en moi, et me fit tenir debout, et j'entendis celui qui me parlait.
3 Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
Fils de l'homme, me dit-il, je t'envoie vers les enfants d'Israël, vers ces nations rebelles qui se sont révoltées contre moi; eux et leurs pères ont péché contre moi jusqu'à aujourd'hui même.
4 Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
Ce sont des enfants à la face impudente et au cœur obstiné, vers lesquels je t'envoie; tu leur diras: Ainsi a parlé le Seigneur, l'Éternel!
5 Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
Et soit qu'ils écoutent, soit qu'ils n'en fassent rien, - car c'est une maison rebelle, - ils sauront du moins qu'un prophète est au milieu d'eux.
6 Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
Mais toi, fils de l'homme, ne les crains point et ne crains point leurs paroles; bien que tu sois au milieu des épines et des ronces, et que tu demeures parmi des scorpions, ne crains point leurs paroles, et ne t'effraie pas de leur visage, quoiqu'ils soient une maison rebelle.
7 Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
Tu leur annonceras donc mes paroles, soit qu'ils écoutent, soit qu'ils n'en fassent rien, car ils ne sont que rébellion.
8 Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
Mais toi, fils de l'homme, écoute ce que je vais te dire et ne sois point rebelle, comme cette maison rebelle; ouvre la bouche, et mange ce que je vais te donner.
9 Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
Alors je regardai, et voici une main étendue vers moi, qui tenait un livre en rouleau.
10 Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.
Elle le déploya devant moi, et il était écrit, au-dedans et au-dehors; des lamentations, des plaintes et des gémissements y étaient écrits.

< Ezekieli 2 >