< Ezekieli 2 >

1 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
Et il me dit: Fils de l'homme, tiens-toi sur tes pieds, et je te parlerai.
2 Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
Et un esprit vint en moi; il me prit et il me releva, et m'affermit sur mes pieds, et je l'entendis qui me parlait.
3 Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
Et il me dit: Fils de l'homme, je t'envoie en la maison d'Israël qui m'irrite; car ils m'ont irrité, eux et leurs pères, jusqu'à ce jour.
4 Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
Et tu leur diras: Voici ce que dit le Seigneur.
5 Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
Peut-être écouteront-ils et auront-ils peur, car c'est une maison qui m'irrite; peut-être ils connaîtront que tu es un prophète au milieu d'eux.
6 Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
Pour toi, fils de l'homme, ne les crains pas, ne sois point intimidé devant leur face; car ils se mettront en fureur, et ils t'assiégeront de toutes parts, et tu demeureras au milieu des scorpions; mais ne crains pas leurs discours, ne sois pas intimidé devant leur face; car c'est une maison qui m'irrite.
7 Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
Et tu leur répéteras mes paroles; peut-être écouteront-ils et auront-ils peur; car c'est une maison qui m'irrite.
8 Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
Et toi, fils de l'homme, obéis à celui qui te parle; ne sois pas irritant comme cette maison qui m'irrite. Ouvre la bouche, et mange ce que je te donne.
9 Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
Et je vis, et voilà qu'une main était étendue vers moi, et elle tenait le rouleau d'un livre.
10 Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.
Et elle le déroula devant moi, et il y avait des lettres des deux côtés des pages, et il y était écrit: Une lamentation, un chant de deuil, et des hélas!

< Ezekieli 2 >