< Ezekieli 2 >

1 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
И ми рече: Сине човешки, изправи се на нозете си, и ще ти говоря.
2 Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
И като ми говори, Духът влезе в мене и ме постави на нозете ми; и чух онзи, който ми говореше.
3 Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
И рече ми: Сине човешки, аз те изпращам при израилтяните, при бунтовни люде, които въстанаха против Мене; те и бащите им са престъпвали Моите думи дори до тоя днешен ден.
4 Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
Тия чада, при които те изпращам, са безочливи и коравосърдечни; а ти да им думаш: Така казва Господ Иеова.
5 Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
послушали или непослушали, (защото е бунтовен дом), пак те ще познаят, че е имало пророк всред тях.
6 Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
И ти, сине човешки, да се не плашиш от тях, и от думите им да се не убоиш, ако и да има тръни и бодили около тебе, и да живееш между скорпии; да се не убоиш от думите им, нито да се ужасяваш от погледите им, макар че са бунтовен дом.
7 Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
И да им говориш думите Ми, или послушали или непослушали; защото са твърде бунтовни.
8 Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
Ти обаче, сине човешки, слушай това, което ти говоря; не ставай и ти бунтовник като тоя бунтовен дом; отвори устата си и изяж това, което ти давам.
9 Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
И като погледнах, ето ръка простряна към мене, и ето в нея свитък книга.
10 Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.
И той го разви пред мене. Писаното бе отвътре и отвън, в което бяха написани плачове, ридание и горко.

< Ezekieli 2 >