< Ezekieli 19 >

1 “Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
Et toi, prononce une complainte sur les princes d'Israël,
2 Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
Et dis: Qu'était-ce que ta mère? Une lionne couchée au milieu des lions, et élevant ses petits au milieu des lionceaux.
3 Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
Elle éleva un de ses petits, qui devint un jeune lion; il apprit à déchirer sa proie, et dévora des hommes.
4 Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
Mais les nations en entendirent parler, et il fut pris dans leur fosse; et, après lui avoir mis des boucles aux narines, elles l'emmenèrent au pays d'Égypte.
5 “‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
Quand la lionne vit qu'elle attendait en vain, que tout son espoir était perdu, elle prit un autre de ses petits, et en fit un jeune lion.
6 Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
Il marcha parmi les lions, et devint un jeune lion; il apprit à déchirer sa proie, et dévora des hommes;
7 Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
Il désolait leurs palais, et détruisait leurs villes; le pays avec tout ce qu'il contient fut frappé de stupeur à l'ouïe de son rugissement.
8 Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
Contre lui se rangèrent les nations de toutes les contrées voisines, et elles jetèrent sur lui leurs filets; il fut pris dans leur fosse.
9 Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
Elles le mirent en cage, avec des boucles aux narines; puis elles l'emmenèrent auprès du roi de Babylone, et le conduisirent dans une forteresse, afin qu'on n'entendît plus sa voix sur les montagnes d'Israël.
10 “‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
Ta mère était, comme toi, semblable à une vigne plantée près des eaux; elle était chargée de fruits et de sarments, grâce à l'abondance des eaux.
11 Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
Elle avait de vigoureux rameaux pour des sceptres de souverains; par son élévation elle atteignait jusqu'aux branches touffues; elle attirait les regards par sa hauteur et par l'abondance de ses rameaux.
12 Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
Mais elle fut arrachée avec fureur et jetée par terre; le vent d'orient a desséché son fruit; ses rameaux vigoureux ont été brisés et desséchés;
13 Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
Le feu les a dévorés, et maintenant elle est plantée dans le désert, dans une terre sèche et aride.
14 Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”
Le feu est sorti d'un rameau de ses branches et a consumé son fruit, et elle n'a plus de rameau vigoureux pour un sceptre de roi. Telle est la complainte, et elle servira de complainte.

< Ezekieli 19 >