< Ezekieli 19 >

1 “Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
« Prononcez une complainte sur les princes d'Israël,
2 Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
et dites, Quelle était ta mère? Une lionne. Elle s'est couchée parmi les lions, au milieu des jeunes lions, elle a nourri ses petits.
3 Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
Elle a élevé un de ses petits. Il est devenu un jeune lion. Il a appris à attraper la proie. Il a dévoré des hommes.
4 Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
Les nations ont aussi entendu parler de lui. Il a été pris dans leur fosse; et ils l'ont emmené avec des crochets dans le pays d'Égypte.
5 “‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
"'Or, quand elle vit qu'elle avait attendu, et son espoir était perdu, puis elle a pris un autre de ses petits, et en a fait un jeune lion.
6 Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
Il montait et descendait parmi les lions. Il est devenu un jeune lion. Il a appris à attraper la proie. Il a dévoré des hommes.
7 Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
Il connaissait leurs palais, et ont dévasté leurs villes. La terre était désolée avec sa plénitude, à cause du bruit de ses rugissements.
8 Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
Et les nations l'attaquèrent de tous côtés, depuis les provinces. Ils ont étendu leur filet sur lui. Il a été pris dans leur fosse.
9 Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
Ils l'ont mis dans une cage avec des crochets, et l'ont amené au roi de Babylone. Ils l'ont amené dans des forteresses, afin que sa voix ne soit plus entendue sur les montagnes d'Israël.
10 “‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
"'Ta mère était comme une vigne dans ton sang, plantée près des eaux. Il était fécond et plein de branches à cause des nombreuses eaux.
11 Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
Il avait des branches robustes pour les sceptres de ceux qui gouvernaient. Leur stature était exaltée parmi les épais branchages. Ils ont été vus dans leur taille avec la multitude de leurs branches.
12 Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
Mais il a été arraché avec fureur. Il a été jeté à terre, et le vent d'est a desséché ses fruits. Ses branches fortes ont été brisées et se sont desséchées. Le feu les a consumés.
13 Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
Maintenant, elle est plantée dans le désert, dans une terre sèche et assoiffée.
14 Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”
Le feu est sorti de ses branches. Il a dévoré ses fruits, de sorte qu'il n'y a pas en elle de branche forte pour être un sceptre pour gouverner. C'est une lamentation, et ce sera une lamentation. »

< Ezekieli 19 >