< Ezekieli 19 >

1 “Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
Thou. therefore take up a dirge, for the prince of Israel;
2 Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
and thou shalt say— How was thy mother a lioness, Between lions, she lay down, - In the midst of young lions, She nourished her whelps;
3 Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
And she reared up one of her whelps— A young lion, he became, And he learned to rend prey. Men, he devoured.
4 Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
Then nations heard of him. In their pit, was he caught, — So they brought him with hooks. Into the land of Egypt.
5 “‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
And she saw she had waited Lost was her hope, Then took she another of her whelps. A young lion, she made him.
6 Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
Yea he went to and fro amidst lions A young lion, he became, - And he learned to rend prey. Men, he devoured;
7 Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
And he injured his widows, And their cities, laid waste, - And deserted was the land and its fulness, At the noise of his roaring.
8 Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
Then set upon him the nations round about. From the provinces, - And spread over him their net In their pit, was he caught;
9 Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
And they put him in a cage with hooks, And brought him to Babylon’s king, — They brought him into strong-holds, That his noise might be heard no more Among the mountains of Israel.
10 “‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
Thy mother [was] like a vine of thy vineyard, By waters, was planted, — Fruitful and full of branches, she became By reason of waters abundant;
11 Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
And they served her as staves of power For the sceptres of rulers, And high became the stature thereof With its interwoven foliage, - And it was seen by its height, By its multitude of branches.
12 Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
Then was she uprooted in indignation To the ground, was she cast, And an east wind, dried up her fruit, —Broken off and withered were her staves of power, A fire, devoured them.
13 Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
Now, therefore, is she planted in a desert, -In a land parched and dry;
14 Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”
And there hath gone forth a fire out of her staves of rods. Her fruit, hath it devoured, And there is in her no staff of power. As a sceptre to bear rule. A dirge, it is, and hath been made a dirge.

< Ezekieli 19 >