< Ezekieli 19 >

1 “Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
“And as for you, take up a lament over the leaders of Israel,
2 Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
and you shall say: Why did your mother, the lioness, recline among the male lions, and raise her little ones in the midst of young lions?
3 Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
And she led away one of her little ones, and he became a lion. And he learned to seize prey and to consume men.
4 Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
And the Gentiles heard about him, and they seized him, but not without receiving wounds. And they led him away in chains to the land of Egypt.
5 “‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
Then, when she had seen that she was weakened, and that her hope had perished, she took one of her little ones, and appointed him as a lion.
6 Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
And he advanced among the lions, and he became a lion. And he learned to seize prey and to devour men.
7 Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
He learned to make widows, and to lead their citizens into the desert. And the land, with its plenitude, was made desolate by the voice of his roaring.
8 Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
And the Gentiles came together against him, on every side, from the provinces, and they spread their net over him; by their wounds, he was captured.
9 Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
And they put him into a cage; they led him in chains to the king of Babylon. And they cast him into a prison, so that his voice would no longer be heard upon the mountains of Israel.
10 “‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
Your mother is like a vine, in your blood, planted by the water; her fruit and her branches have increased because of many waters.
11 Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
And her strong branches were made into scepters for the rulers, and her stature was exalted among the branches. And she saw her own loftiness among the multitude of her branches.
12 Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
But she was uprooted in wrath, and cast upon the ground. And the burning wind dried up her fruit. Her robust branches withered and were dried up. A fire consumed her.
13 Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
And now she has been transplanted into the desert, into a land impassable and dry.
14 Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”
And a fire has gone forth from a rod of her branches, which has consumed her fruit. And there is no strong branch in her to become a scepter for the rulers. This is a lamentation, and it shall be a lamentation.”

< Ezekieli 19 >