< Ezekieli 17 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of the Lord was maad to me,
2 “Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
and he seide, Sone of man, sette forth a derk speche, and telle thou a parable to the hous of Israel;
3 Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
and thou schalt seie, The Lord God seith these thingis. A greet egle of grete wyngis, with long stretchyng out of membris, ful of fetheris and of dyuersite, cam to the Liban, and took awei the merowe of the cedre.
4 Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
He pullide awei the hiynesse of boowis therof, and bar it ouer in to the lond of Chanaan, and settide it in the citee of marchauntis.
5 “‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
And he took of the seed of the lond, and settide it in the lond for seed, that it schulde make stidfast roote on many watris; he settide it in the hiyere part.
6 Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
And whanne it hadde growe, it encreesside in to a largere vyner, in lowe stature; for the boowis therof bihelden to that egle, and the rootis therof weren vndur that egle; therof it was maad a vyner, and it made fruyt in to siouns, and sente out boowis.
7 “‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
And another greet egle was maad, with grete wyngis, and many fetheris; and lo! this vyner as sendynge hise rootis to that egle, stretchide forth his siouns to that egle, that he schulde moiste it of the cornfloris of his seed.
8 Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
Which is plauntid in a good lond on many watris, that it make boowis, and bere fruyt, that it be in to a greet vyner.
9 “Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
Seie thou, Ezechiel, The Lord God seith these thingis, Therfor whether he schal haue prosperite? Whether Nabugodonosor schal not pulle awei the rootis of hym, and schal streyne the fruytis of hym? And he schal make drie alle the siouns of buriowning therof, and it schal be drie; and not in greet arm, nether in myche puple, that he schulde drawe it out bi the rootis.
10 Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
Lo! it is plauntid, therfor whether it schal haue prosperite? Whether not whanne brennynge wynd schal touche it, it schal be maad drye, and schal wexe drie in the cornfloris of his seed?
11 Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
And the word of the Lord was maad to me, and he seide, Seie thou to the hous terrynge to wraththe,
12 “Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
Witen ye not what these thingis signefien? Seie thou, Lo! the king of Babiloyne cometh in to Jerusalem; and he schal take the kyng and the princis therof, and he schal leede hem to hym silf in to Babiloyne.
13 Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
And he schal take of the seed of the rewme, and schal smyte with it a boond of pees, and he schal take of it an ooth; but also he schal take awei the stronge men of the lond,
14 kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
that it be a meke rewme, and be not reisid, but that it kepe the couenaunt of hym, and holde it.
15 Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
Which yede awei fro hym, and sente messangeris in to Egipt, that it schulde yyue to hym horsis and miche puple. Whether he that dide these thingis, schal haue prosperite, ether schal gete helthe? and whether he that brekith couenaunt, schal ascape?
16 “‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
Y lyue, seith the Lord God, for in the place of the king that made hym kyng, whos ooth he made voide, and brak the couenaunt, which he hadde with hym, in the myddis of Babiloyne he schal die.
17 Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
And not in greet oost, nether in myche puple Farao schal make batel ayens hym, in the castyng of erthe, and in bildyng of palis, that he sle many persones.
18 Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
For he dispiside the ooth, that he schulde breke the boond of pees, and lo! he yaf his hond; and whanne he hath do alle these thingis, he schal not ascape.
19 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
Therfor the Lord God seith these thingis, Y lyue, for Y schal sette on his heed the ooth which he dispiside, and the boond of pees which he brak.
20 Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
And Y schal spredde abrood my net on hym, and he schal be takun in my net, and Y schal brynge hym in to Babiloyne; and there Y schal deme hym in the trespassyng, bi which he dispiside me.
21 Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
And alle hise flieris a wei with al his cumpenye schulen falle doun bi swerd, forsothe the remenauntis schulen be schaterid in to ech wynd; and ye schulen wite, that Y the Lord spak.
22 “‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
The Lord God seith these thingis, And Y schal take of the merowe of an hiy cedre, and Y schal sette a tendir thing of the cop of hise braunchis; Y schal streyne, and Y schal plaunte on an hiy hil, and apperynge fer.
23 Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
In the hiy hil of Israel Y schal plaunte it; and it schal breke out in to buriownyng, and it schal make fruyt, and it schal be in to a greet cedre, and alle briddis schulen dwelle vndur it; ech volatil schal make nest vndur the schadewe of hise boowis.
24 Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”
And alle trees of the cuntrei schulen wite, that Y am the Lord; Y made low the hiy tre, and Y enhaunside the low tre, and Y made drie the greene tree, and Y made the drie tree to brynge forth boowis; Y the Lord haue spoke, and Y haue do.

< Ezekieli 17 >