< Ezekieli 17 >
1 Yehova anayankhula nane kuti,
The word of Yahweh came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
“Son of man, present a riddle and speak a parable to the house of Israel.
3 Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
Say, 'The Lord Yahweh says this: A large eagle with large wings and long pinions, full of feathers, and that was multicolored went to Lebanon and took hold of the top of a cedar tree.
4 Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
It broke off the tips of the branches and took them to the land of Canaan; he planted it in a city of merchants.
5 “‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
He also took some seed of the land and planted it in fertile soil. He placed it beside a large body of water like a willow.
6 Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
Then it sprouted and became a spreading vine low to the ground. Its branches turned toward him, and its roots grew under it. So it became a vine and produced branches and sent out shoots.
7 “‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
But there was another great eagle with large wings and many feathers. Behold! This vine turned its roots toward the eagle, and it spread out its branches toward the eagle from the place it had been planted so it would be watered.
8 Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
It had been planted in good soil beside a large body of water so it would produce branches and sprout fruit, to become a magnificent vine.'
9 “Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
Say to the people, 'The Lord Yahweh says this: Will it prosper? Will it not be uprooted and stripped of its fruit so that it withers, and all its fresh growth will wither? No strong arm or many people will be needed to pull it out by its roots.
10 Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
So behold! After it has been planted, will it grow? Will it not wither when the eastern wind touches it? It will completely wither away in the garden plot where it sprouted.'”
11 Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
Then the word of Yahweh came to me, saying,
12 “Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
“Speak to the rebellious house, 'Do you not know what these things mean? Behold! The king of Babylon came to Jerusalem and took her king and her princes and brought them to him in Babylon.
13 Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
Then he took a royal descendant, made a covenant with him, and brought him under an oath. He took away the powerful people of the land,
14 kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
so the kingdom might become lowly and not lift itself up. By keeping his covenant the land will survive.
15 Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
But the king of Jerusalem rebelled against him by sending his ambassadors to Egypt to acquire horses and an army. Will he succeed? Will the one doing these things escape? If he breaks the covenant, will he escape?
16 “‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
As I live!—this is the Lord Yahweh's declaration—he will surely die in the land of the king who made him king, the king whose oath he despised, and whose covenant he broke. He will die in the middle of Babylon.
17 Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
Pharaoh with his mighty army and a great company of men will not help him in battle, when ramps are constructed and siege walls are built up to cut off many lives.
18 Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
For the king despised his oath by breaking the covenant. Behold, he reached out with his hand to make a promise and yet he did all these things. He will not escape.
19 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
Therefore the Lord Yahweh says this: As I live, was it not my oath that he despised and my covenant that he broke? So I will bring his punishment on his head!
20 Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
I will spread my net out over him, and he will be caught in my hunting net. Then I will bring him to Babylon and execute judgment on him there for his treason that he committed when he betrayed me!
21 Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
All of his refugees in his armies will fall by the sword, and the ones who remain will be scattered in every direction. Then you will know that I am Yahweh; I have declared this would happen.”
22 “‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
The Lord Yahweh says this, 'So I myself will take away the highest part of the cedar tree, and I will plant it away from its tender branches. I will break it off, and I myself will plant it on a high mountain.
23 Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
I will plant it on the mountains of Israel so it will bear branches and produce fruit, and it will become a majestic cedar so that every winged bird will live under it. They will nest in the shade of its branches.
24 Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”
Then all the trees of the field will know that I am Yahweh. I bring down the high trees and I raise up the low trees. I wither the watered tree and I cause the dried tree to bloom. I am Yahweh, I have declared that this will happen; and I have done it.'”