< Ezekieli 17 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
and to be word LORD to(wards) me to/for to say
2 “Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
son: child man to riddle riddle and to use a proverb proverb to(wards) house: household Israel
3 Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
and to say thus to say Lord YHWH/God [the] eagle [the] great: large great: large [the] wing slow [the] wing full [the] plumage which to/for him [the] embroidery to come (in): come to(wards) [the] Lebanon and to take: take [obj] treetop [the] cedar
4 Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
[obj] head: top shoot his to pluck and to come (in): bring him to(wards) land: country/planet merchant in/on/with city to trade to set: make him
5 “‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
and to take: take from seed [the] land: country/planet and to give: put him in/on/with land: soil seed to take: take upon water many willow to set: make him
6 Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
and to spring and to be to/for vine to overrun low height to/for to turn branch his to(wards) him and root his underneath: stand him to be and to be to/for vine and to make alone: pole and to send: depart bough
7 “‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
and to be eagle one great: large great: large wing and many plumage and behold [the] vine [the] this to hunger root her upon him and branch his to send: depart to/for him to/for to water: watering [obj] her from bed plantation her
8 Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
to(wards) land: soil pleasant to(wards) water many he/she/it to transplant to/for to make branch and to/for to lift: bear fruit to/for to be to/for vine clothing
9 “Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
to say thus to say Lord YHWH/God to prosper not [obj] root her to tear and [obj] fruit her to strip and to wither all fresh-plucked branch her to wither and not in/on/with arm great: large and in/on/with people many to/for to lift: raise [obj] her from root her
10 Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
and behold to transplant to prosper not like/as to touch in/on/with her spirit: breath [the] east to wither to wither upon bed branch her to wither
11 Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
and to be word LORD to(wards) me to/for to say
12 “Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
to say please to/for house: household [the] rebellion not to know what? these to say behold to come (in): come king Babylon Jerusalem and to take: take [obj] king her and [obj] ruler her and to come (in): bring [obj] them to(wards) him Babylon [to]
13 Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
and to take: take from seed: children [the] kingship and to cut: make(covenant) with him covenant and to come (in): bring [obj] him in/on/with oath and [obj] leader [the] land: country/planet to take: take
14 kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
to/for to be kingdom low to/for lest to lift: raise to/for to keep: obey [obj] covenant his to/for to stand: stand her
15 Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
and to rebel in/on/with him to/for to send: depart messenger his Egypt to/for to give: give to/for him horse and people: soldiers many to prosper to escape [the] to make: do these and to break covenant and to escape
16 “‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
alive I utterance Lord YHWH/God if: surely yes not in/on/with place [the] king [the] to reign [obj] him which to despise [obj] oath his and which to break [obj] covenant his with him in/on/with midst Babylon to die
17 Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
and not in/on/with strength: soldiers great: large and in/on/with assembly many to make: do [obj] him Pharaoh in/on/with battle in/on/with to pour: build siege mound mound and in/on/with to build siegework to/for to cut: eliminate soul: life many
18 Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
and to despise oath to/for to break covenant and behold to give: give hand: power his and all these to make: do not to escape
19 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
to/for so thus to say Lord YHWH/God alive I if: surely yes not oath my which to despise and covenant my which to break and to give: pay him in/on/with head his
20 Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
and to spread upon him net my and to capture in/on/with net my and to come (in): bring him Babylon [to] and to judge with him there unfaithfulness his which be unfaithful in/on/with me
21 Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
and [obj] all (fugitive his *Q(K)*) in/on/with all band his in/on/with sword to fall: kill and [the] to remain to/for all spirit: breath to spread and to know for I LORD to speak: speak
22 “‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
thus to say Lord YHWH/God and to take: take I from treetop [the] cedar [the] to exalt and to give: put from head: top shoot his tender to pluck and to transplant I upon mountain: mount high and be eminent
23 Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
in/on/with mountain: mount height Israel to transplant him and to lift: bear branch and to make fruit and to be to/for cedar great and to dwell underneath: under him all bird all wing in/on/with shadow branch his to dwell
24 Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”
and to know all tree [the] land: country for I LORD to abase tree high to exult tree low to wither tree fresh and to sprout tree dry I LORD to speak: speak and to make: do

< Ezekieli 17 >