< Ezekieli 16 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
La parole de l'Éternel me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
Fils de l'homme, fais connaître à Jérusalem ses abominations.
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
Dis: Ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel, à Jérusalem: Par ton origine et ta naissance tu es du pays de Canaan; ton père est un Amoréen, ta mère une Héthienne.
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
A ta naissance, au jour où tu naquis, ton nombril ne fut point coupé, tu ne fus point lavée dans l'eau pour être nettoyée, tu ne fus pas purifiée avec du sel, ni enveloppée de langes.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
Aucun œil n'eut pitié de toi, pour te faire aucune de ces choses par compassion pour toi; mais tu fus jetée sur la surface d'un champ, par mépris pour ta vie, au jour de ta naissance.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
Or je passai près de toi, je te vis gisant dans ton sang, près d'être foulée aux pieds, et je te dis: Vis dans ton sang! je te dis: Vis dans ton sang!
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
Je t'ai multipliée par myriades, comme l'herbe des champs, tu pris de l'accroissement, tu grandis et tu devins d'une beauté parfaite. Tes seins se formèrent, tu devins nubile, mais tu étais nue, et entièrement nue.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
Et je passai près de toi et te regardai; voici, ton âge était l'âge où l'on aime, et j'étendis sur toi le pan de mon vêtement, je couvris ta nudité; je te fis serment, je fis alliance avec toi, dit le Seigneur, l'Éternel, et tu m'appartins.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
Je te lavai dans l'eau, et en t'y plongeant, j'ôtai le sang de dessus toi, et je t'oignis d'huile.
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
Je te revêtis de broderies, je te mis une chaussure de couleur d'hyacinthe; je te ceignis de fin lin et te couvris de soie.
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
Je te parai d'ornements; je mis des bracelets à tes mains, et un collier à ton cou,
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
Un anneau à ton nez, des boucles à tes oreilles, une couronne magnifique sur ta tête.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
Ainsi tu fus parée d'or et d'argent; ton vêtement était de fin lin, de soie, de broderies; la fleur de farine, le miel et l'huile faisaient ta nourriture; tu devins extrêmement belle, et tu parvins à une royale dignité.
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
Ta renommée se répandit parmi les nations à cause de ta beauté, car elle était parfaite, grâce à la magnificence dont je t'avais ornée, dit le Seigneur, l'Éternel.
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
Mais tu t'es confiée en ta beauté, tu t'es prostituée à la faveur de ta renommée, et tu as prodigué tes prostitutions à tout passant, en te livrant à lui.
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
Tu as pris de tes vêtements; tu t'es fait des hauts lieux garnis d'étoffes de toute couleur, et tu t'y es prostituée, - chose qui n'était point arrivée, et qui n'arrivera plus.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
Tu as aussi pris les magnifiques parures, faites de mon or et de mon argent, que je t'avais données; tu en as fait des figures d'hommes, auxquels tu t'es prostituée.
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
Tu as pris tes vêtements brodés pour les en couvrir, et tu leur as offert mon huile et mes parfums.
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Et mon pain que je t'avais donné, la fleur de farine, l'huile et le miel dont je te nourrissais, tu as mis ces choses devant elles comme une offrande d'agréable odeur. Voilà ce qui en est, dit le Seigneur, l'Éternel.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
Tu as pris tes fils et tes filles, que tu m'avais enfantés, et tu les leur as sacrifiés pour être dévorés. Était-ce trop peu que tes prostitutions?
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
Tu as immolé mes fils, tu les as livrés, en les faisant passer par le feu en leur honneur.
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
Et au milieu de toutes tes abominations et de tes adultères, tu ne t'es point souvenue du temps de ta jeunesse, alors que tu étais nue et découverte, gisante dans ton sang, près d'être foulée aux pieds.
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
Et après toutes tes méchantes actions, - malheur, malheur à toi! dit le Seigneur, l'Éternel, -
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
Tu t'es bâti des maisons de débauche, tu t'es fait des hauts lieux sur toutes les places.
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
A l'entrée de chaque rue tu as bâti ton haut lieu, et tu as déshonoré ta beauté; car tu t'es livrée à tout passant et tu as multiplié tes adultères.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
Tu t'es prostituée aux enfants de l'Égypte, tes voisins aux corps vigoureux, et pour m'irriter tu as multiplié tes adultères.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
Et voici, j'ai étendu ma main contre toi, j'ai diminué la part qui t'était assignée, et t'ai livrée à la discrétion de tes ennemis, les filles des Philistins, qui ont rougi de ta conduite criminelle.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
Tu t'es prostituée aux enfants de l'Assyrie, parce que tu n'étais pas assouvie; et après avoir commis adultère avec eux, tu ne fus point encore assouvie;
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
Car tu as multiplié tes impudicités avec la terre de Canaan et jusqu'en Caldée; même alors tu n'en eus point assez.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
Combien ton cœur est lâche, dit le Seigneur, l'Éternel, que tu aies fait toutes ces choses à la façon d'une insigne prostituée!
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
Quand tu bâtissais tes maisons de débauche à chaque bout de rue, quand tu faisais tes hauts lieux dans toutes les places, tu n'as pas même été comme la femme débauchée qui réclame un salaire;
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
Tu as été la femme adultère qui reçoit les étrangers à la place de son mari.
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
On paie un salaire à toutes les femmes débauchées, mais toi, tu as donné des présents à tous tes amants; tu leur as fait des largesses, afin que de toute part ils viennent vers toi, pour tes prostitutions.
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
Et tu as été le contraire des autres femmes dans tes impudicités, en ce qu'on ne te recherchait pas; tu donnais un salaire, tandis que l'on ne t'en donnait aucun; tu as été le contraire des autres.
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
C'est pourquoi, ô prostituée, écoute la parole de l'Éternel!
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
Ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Parce que tes trésors ont été prodigués, et que ta nudité s'est découverte dans tes prostitutions, devant tes amants et toutes tes abominables idoles; à cause du sang de tes enfants, que tu leur as livrés,
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
Voici, je rassemblerai tous tes amants, avec lesquels tu te plaisais, tous ceux que tu as aimés, tous ceux que tu as haïs, je les rassemblerai de toute part contre toi; je leur découvrirai ta nudité, et ils la verront tout entière.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
Et je te jugerai comme on juge les femmes adultères et celles qui répandent le sang; je t'abandonnerai à la sanguinaire vengeance de la fureur et de la jalousie.
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
Je te livrerai entre leurs mains; ils abattront tes maisons de débauche et démoliront tes hauts lieux; ils te dépouilleront de tes vêtements; ils enlèveront tes magnifiques parures et te laisseront nue, entièrement nue.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
Ils feront monter contre toi une foule de gens qui t'assommeront de pierres, et qui te mettront en pièces avec leurs épées.
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
Ils brûleront tes maisons par le feu, et feront justice de toi, en présence d'un grand nombre de femmes; ainsi je mettrai fin à tes prostitutions, et tu ne donneras plus de salaire.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
Et j'assouvirai ma fureur contre toi, et ma jalousie se détournera de toi; alors je serai en repos et n'aurai plus à m'irriter.
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
Parce que tu ne t'es point souvenue du temps de ta jeunesse, que tu m'as provoqué par toutes ces choses, voici, je ferai retomber ta conduite sur ta tête, dit le Seigneur, l'Éternel, et tu ne commettras plus le crime avec toutes tes abominations.
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
Voici, tout homme qui use de proverbes, en fera un sur ton compte, et dira: “Telle mère, telle fille! “
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
Tu es la fille de ta mère, qui eut en aversion son mari et ses enfants; tu es la sœur de tes sœurs, qui ont eu en aversion leurs maris et leurs enfants; votre mère était Héthienne et votre père Amoréen.
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
Ta sœur aînée, avec ses filles, qui habite à ta gauche, c'est Samarie; ta sœur cadette qui demeure à ta droite, c'est Sodome et ses filles.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
Tu n'as pas seulement marché dans leurs voies et pratiqué les mêmes abominations; c'était trop peu; mais tu t'es corrompue plus qu'elles dans toute ta conduite.
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
Je suis vivant! dit le Seigneur, l'Éternel; Sodome, ta sœur elle-même, avec ses filles, n'a point fait ce que tu as fait, toi, avec tes filles.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
Voici quelle a été l'iniquité de Sodome, ta sœur: l'orgueil, l'abondance et une molle oisiveté; voilà ce qu'elle avait, elle et ses filles; mais elle ne soutenait pas la main de l'affligé et du pauvre.
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
Elles sont devenues hautaines et ont commis l'abomination devant moi; aussi les ai-je exterminées, dès que je l'ai vu.
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
Et Samarie n'a pas commis la moitié autant de péchés que toi; tu as multiplié tes abominations plus qu'elle, et par toutes les abominations que tu as commises tu as justifié tes sœurs.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
Porte donc, toi aussi, l'opprobre que tu as infligé à tes sœurs! A cause de tes péchés que tu as rendus plus abominables que les leurs, elles se trouvent être plus justes que toi. Sois donc, toi aussi, couverte de confusion, et porte ton opprobre, puisque tu as justifié tes sœurs.
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
Je ramènerai leurs captifs, les captifs de Sodome et de ses filles, les captifs de Samarie et de ses filles, ainsi que tes propres captifs au milieu des leurs,
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
Afin que tu portes ton opprobre, que tu sois confuse à cause de tout ce que tu as fait, en étant pour elles un sujet de consolation.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
Et tes sœurs, Sodome et ses filles, reviendront à leur premier état; Samarie et ses filles reviendront à leur premier état; et toi et tes filles vous reviendrez à votre premier état.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
Cependant, dans le temps de ton orgueil,
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
Avant que ta méchanceté fût découverte, lorsque tu recevais les outrages des filles de Syrie et de tous ses alentours, des filles des Philistins qui t'insultaient de toute part, ne discourais-tu pas sur Sodome ta sœur?
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
Tu portes sur toi le fardeau de tes crimes et de tes abominations! dit l'Éternel.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
Car ainsi a dit l'Éternel: Je te ferai comme tu as fait, toi qui as méprisé le serment, en rompant l'alliance.
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
Toutefois je me souviendrai de l'alliance que j'ai faite avec toi, dans les jours de ta jeunesse, et j'établirai en ta faveur une alliance éternelle.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
Alors tu te souviendras de ta conduite, et tu en seras confuse, quand tu recevras tes sœurs, tant les aînées que les cadettes, et que je te les donnerai pour filles, mais non en vertu de ton alliance.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Car j'établirai mon alliance avec toi, et tu sauras que je suis l'Éternel,
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
Afin que tu te souviennes, que tu sois confuse, et qu'à cause de ta confusion tu n'ouvres plus la bouche, quand je t'aurai pardonné tout ce que tu as fait, dit le Seigneur, l'Éternel.

< Ezekieli 16 >