< Ezekieli 16 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
"Fils de l’homme, fais connaître à Jérusalem ses abominations.
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
Tu diras: Ainsi parle le Seigneur Dieu à Jérusalem: Le lieu de ton extraction et ton pays natal, c’est la terre de Canaan; ton père était Amorréen et ta mère Héthéenne.
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
Quant à ta naissance, le jour où tu fus enfantée, ton nombril ne fut pas coupé, tu ne fus pas lavée dans l’eau pour être purifiée, tu ne fus pas saupoudrée de sel ni enveloppée de langes.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
Nul oeil ne te prit en pitié pour te donner aucun de ces soins, par compassion pour toi; tu fus jetée au milieu des champs par suite de la répulsion que tu inspirais, le jour où tu naquis.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
Mais je passai auprès de toi, je te vis t’agiter dans ton sang, et je te dis: "Vis dans ton sang!"
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
Je t’ai multipliée comme la végétation des champs, tu as augmenté, grandi, tu as revêtu la plus belle des parures, tes seins se sont affermis, ta chevelure a poussé, mais tu étais nue et dénudée.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
Et je passai près de toi et vis que tu étais arrivée à l’âge des amours; j’étendis mon vêtement sur toi et couvris ta nudité; je m’engageai à toi par serment et fis alliance avec toi, dit le Seigneur Dieu, et tu fus à moi.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
Je te lavai dans l’eau, je nettoyai le sang qui te recouvrait et je t’oignis d’huile.
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
Je te revêtis de broderies, je te mis des chaussures de tahach, je te ceignis de byssus et te couvris de soie.
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
Je t’ornai de parures, je te mis des bracelets aux mains, un collier au cou.
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
Je te mis un anneau au nez, des boucles aux oreilles et une couronne magnifique sur la tête.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
Tu te paras d’or et d’argent; ton costume était de byssus, de soie et de broderie; tu te nourris de fine fleur de farine, de miel et d’huile; et tu fus belle, très belle, et digne de la royauté.
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
Et tu t’es rendue célèbre parmi les nations par ta beauté, qui était parfaite, grâce à l’éclat que j’avais répandu sur toi, dit le Seigneur Dieu!
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
Mais tu t’es fiée à ta beauté et livrée à la prostitution à la faveur de ta renommée; tu as prodigué tes débauches à tout passant quel qu’il fût.
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
Tu as pris de tes vêtements, tu en as fait des hauts lieux bigarrés et tu t’es prostituée sur eux, ce qui ne devait pas arriver et ne devait pas être.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
Et tu as pris tes belles parures faites de mon or et de mon argent que je t’avais donnés et tu t’es confectionné des simulacres de mâles et tu t’es prostituée à eux.
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
Et tu as pris tes vêtements brodés et tu les en as recouverts et tu as mis devant eux mon huile et mon encens.
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Et mon pain que je t’avais donnéje te nourrissais de fine fleur de farine, d’huile et de mieltu le leur as offert en odeur agréable; oui, il en a été ainsi, dit le Seigneur Dieu.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
Et tu as pris tes fils et tes filles que tu m’avais enfantés et tu les leur as sacrifiés en pâture; était-ce trop peu que ta prostitution?
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
Tu as immolé mes fils, tu les as livrés en les faisant passer devant eux.
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
Et au cours de toutes tes abominations, de tes débauches, tu ne t’es pas souvenue des jours de ton enfance, où tu étais nue et dénudée et où tu te roulais dans ton sang.
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
Et ensuite après toute ta dépravationmalheur, malheur à toi! dit le Seigneur Dieu,
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
tu t’es bâti un tertre et tu t’es fait un haut-lieu sur chaque place.
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
A l’entrée de chaque chemin tu as édifié ton haut-lieu, tu as souillé ta beauté, tu t’es abandonnée à tout passant, tu as multiplié tes impudicités.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
Tu t’es prostituée aux enfants de l’Egypte, tes voisins, forts en chair, et tu as multiplié tes débauches pour me courroucer.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
Et voici que j’ai étendu ma main sur toi et j’ai réduit ta subsistance, je t’ai livrée à la merci de tes ennemies, les filles des Philistins, confuses de ta conduite infâme.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
Ensuite tu t’es prostituée aux enfants d’Achour, faute d’être assouvie; tu t’es prostituée avec eux, sans en avoir encore assez.
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
Tu as multiplié aussi tes débauches du côté du pays mercantile des Chaldéens, et avec cela non plus tu ne fus pas rassasiée.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
Que ton coeur était languissant, dit le Seigneur Dieu, quand tu commettais tous ces actes, à la façon d’une courtisane sans frein!
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
Quand tu bâtissais ton tertre à l’entrée de chaque chemin, ta hauteur sur chaque place, tu n’étais pas comme les courtisanes toujours mécontentes du salaire.
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
O femme adultère, qui prends des étrangers à la place de ton mari!
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
A toutes les courtisanes on offre un don, et toi, tu as fait des cadeaux à tous tes amants, tu les as achetés afin qu’ils vinssent à toi des alentours pour tes débauches.
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
II s’est passé pour toi le contraire des autres femmes, car c’est toi qui t’es prostituée, et l’on ne s’est pas prostitué à toi; c’est toi qui payais un salaire et l’on ne t’en a point donné; ç’a été un renversement des choses.
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
C’Est pourquoi, prostituée, écoute la parole du Seigneur.
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
Ainsi parle le Seigneur Dieu: "Puisque tes fonds ont été gaspillés, que ta nudité s’est dévoilée dans tes prostitutions avec tes amants et avec toutes tes idoles infâmes, et en raison du sang de tes enfants que tu leur as voués,
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
pour tout cela je vais rassembler tous tes amants auxquels tu plaisais, tous ceux que tu aimais avec tous ceux que tu haïssais, je les rassemblerai contre toi de toute part et je leur découvrirai ta nudité, et ils verront toute ta nudité.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
Et je t’infligerai le châtiment des femmes adultères et qui versent le sang, et je ferai de toi un être de sang, de fureur et de jalousie.
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
Je te livrerai entre leurs mains et ils abattront ton tertre et démoliront tes hauts-lieux; ils te dépouilleront de tes vêtements, prendront tes effets d’apparat et te laisseront là nue et dépouillée.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
Ils feront monter contre toi une multitude et t’accableront de pierres et te perceront de leurs glaives.
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
Ils consumeront par le feu tes maisons et exécuteront des jugements contre toi sous les yeux de nombreuses femmes; ainsi je mettrai fin à ta prostitution, et dorénavant tu ne donneras plus de salaire non plus.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
J’Assouvirai ma colère sur toi, et ma jalousie se détournera de toi, je me tiendrai tranquille sans plus me courroucer.
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
Parce que tu ne t’es pas rappelé les jours de ta jeunesse et que tu m’as fâché par toutes ces choses, moi aussi, voici que je fais retomber ta conduite sur ta tête, dit le Seigneur Dieu: n’as-tu pas ajouté la bassesse à toutes tes abominations?
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
Certes, tous les faiseurs de proverbes t’appliqueront le proverbe que voici: "Telle mère, telle fille!"
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
Tu es bien la fille de ta mère, qui a pris en aversion son mari et ses enfants, et la soeur—de tes soeurs, qui ont pris en aversion leurs maris et leurs fils; votre mère est une Hétéenne et votre père un Amorréen.
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
Ta soeur aînée, c’est Samarie avec ses filles qui demeure à ta gauche, et ta soeur cadette qui demeure à ta droite, c’est Sodome et ses filles.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
Non seulement tu as marché dans leurs voies et pratiqué leurs abominations, mais peu s’en est fallu que tu n’eusses été plus corrompue qu’elles dans toutes tes voies.
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
Par ma vie, dit le Seigneur Dieu, Sodome ta soeur, elle avec ses filles, n’a pas agi comme tu as agi, toi et tes filles.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
Or, voici quel a été le crime de Sodome, ta soeur: l’orgueil d’être bien repue et d’avoir toutes ses aises s’est trouvé en elle et en ses filles, et elle n’a pas soutenu la main du pauvre et du nécessiteux.
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
Elles ont été hautaines, elles ont commis des abominations devant moi, et je les ai supprimées quand j’ai vu cela.
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
Mais Samarie n’a pas commis la moitié de tes péchés; tu as accumulé plus d’abominations que celles-là et innocenté tes soeurs par toutes les abominations que tu as faites.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
Aussi, porte ta confusion, toi qui as rendu excusable ta soeur; à cause de tes péchés par lesquels tu as dépassé leurs abominations, elles se trouvent plus innocentes que toi, aussi sois honteuse et porte ta confusion, toi qui innocentes tes soeurs.
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
Et j’assurerai leur retour de captivité, le retour de Sodome et de ses filles et le retour de Samarie et de ses filles, et le retour de tes captifs au milieu d’elles,
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
afin que tu portes ta confusion et que tu rougisses de tout ce que tu as fait, en devenant pour elles un sujet de consolation.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
Oui, tes soeurs, Sodome et ses filles, reviendront à leur état primitif, et Samarie et ses filles reviendront à leur état primitif, et toi et tes filles, vous reviendrez à votre état primitif.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
Est-ce que le nom de Sodome, ta soeur, ne devait pas être une leçon dans ta bouche, au jour de ton orgueil,
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
avant que se manifestât ta perversité, comme au temps des outrages des filles d’Aram et de tous ses environs, des filles des Philistins qui te harcelaient de toutes parts?
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
Ton infamie et tes abominations, tu les portes, dit l’Eternel.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
Oui, ainsi parle le Seigneur Dieu, j’agirai envers toi comme tu as agi, toi qui as méprisé le serment et rompu l’alliance.
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
Mais moi, je me rappellerai l’alliance conclue avec toi aux jours de ton enfance, et j’établirai avec toi une alliance éternelle.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
Et tu te rappelleras tes voies et tu seras confuse, quand tu recueilleras tes soeurs, celles qui sont plus âgées que toi et celles qui sont plus jeunes que toi, et que je te les donnerai pour filles, mais non en vertu de ton alliance.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Je rétablirai, moi, mon alliance avec toi, et tu sauras que je suis l’Eternel,
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
afin que tu te souviennes et que tu aies honte, et que tu ne puisses plus ouvrir la bouche, de confusion, quand je t’aurai pardonné tout ce que tu as fait, dit le Seigneur Dieu."

< Ezekieli 16 >