< Ezekieli 16 >
1 Yehova anayankhula nane kuti,
La parole de Yahvé me fut adressée, en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
Fils d'homme, fais connaître à Jérusalem ses abominations;
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
et dis: « Le Seigneur Yahvé dit à Jérusalem: « Ton origine et ta naissance sont du pays des Cananéens. Ton père était un Amoréen, et ta mère était une Héthienne.
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
Quant à ta naissance, le jour où tu es née, ton nombril n'a pas été coupé. On ne t'a pas lavée dans l'eau pour te purifier. On ne t'a pas salé du tout, ni enveloppé dans des couvertures.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
Aucun œil n'a eu pitié de toi, pour te faire l'une de ces choses, pour avoir pitié de toi; mais on t'a jeté en plein champ, parce que tu étais en horreur le jour où tu es né.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
« Quand j'ai passé près de toi et que je t'ai vu te vautrer dans ton sang, je t'ai dit: « Si tu es dans ton sang, vis.
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
Je t'ai fait multiplier comme les plantes des champs, tu as grandi et tu es devenue grande, et tu as atteint une grande beauté. Tes seins se sont formés, et tes cheveux ont poussé; pourtant tu étais nue et dénudée.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
"''Quand je passais devant toi et que je te regardais, voici que ton temps était le temps de l'amour; j'ai étendu sur toi mon vêtement et j'ai couvert ta nudité. Oui, je me suis engagé envers toi et j'ai conclu une alliance avec toi, dit le Seigneur Yahvé, et tu es devenu mien.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
"''Puis je t'ai lavé avec de l'eau. Oui, j'ai lavé à fond ton sang, et je t'ai oint d'huile.
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
Je t'ai aussi revêtu d'un ouvrage brodé et je t'ai mis des sandales de cuir. Je t'ai habillé de lin fin et je t'ai couvert de soie.
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
Je t'ai paré d'ornements, j'ai mis des bracelets à tes mains, et j'ai mis une chaîne à ton cou.
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
J'ai mis un anneau à ton nez, des boucles d'oreille à tes oreilles, et une belle couronne sur ta tête.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
Tu étais ainsi paré d'or et d'argent. Tes vêtements étaient de lin fin, de soie et de broderie. Tu mangeais de la farine fine, du miel et de l'huile. Tu étais d'une grande beauté, et tu as prospéré jusqu'à devenir une famille royale.
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
Ta renommée s'est répandue parmi les nations à cause de ta beauté, car elle était parfaite, grâce à la majesté dont je t'avais revêtue, dit le Seigneur Yahvé.
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
"''Mais tu t'es confiée à ta beauté, tu t'es prostituée à cause de ta renommée, et tu as déversé ta prostitution sur tous les passants. C'était à lui.
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
Tu as pris une partie de tes vêtements, tu t'es fait des hauts lieux ornés de couleurs variées, et tu t'es prostituée dessus. Cela ne doit pas arriver, et cela n'arrivera pas.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
Vous avez aussi pris vos beaux bijoux, de mon or et de mon argent, que je vous avais donnés, et vous vous êtes fait des images d'hommes, et vous vous êtes prostitués avec elles.
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
Tu as pris tes vêtements brodés, tu les as couverts, et tu as mis devant eux mon huile et mon encens.
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Et le pain que je t'ai donné, la fleur de farine, l'huile et le miel, dont je t'ai nourri, tu l'as mis devant eux comme un parfum agréable, et il en a été ainsi, dit le Seigneur Yahvé.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
"« Tu as pris tes fils et tes filles, que tu m'avais enfantés, et tu les as sacrifiés pour qu'ils soient dévorés. Votre prostitution a-t-elle été peu de chose,
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
pour que vous fassiez mourir mes enfants et que vous les livriez, en les faisant passer par le feu pour eux?
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
Dans toutes tes abominations et tes prostitutions, tu ne t'es pas souvenu des jours de ta jeunesse, quand tu étais nu et dénudé, et que tu te vautrais dans ton sang.
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
"« Il est arrivé, après toutes vos méchancetés, malheur à vous, dit le Seigneur Yahvé,
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
que vous vous êtes bâti une voûte, et que vous vous êtes fait une place élevée dans toutes les rues.
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
Tu t'es bâti une place élevée à la tête de chaque chemin, et tu as fait de ta beauté une abomination; tu as ouvert tes pieds à tous les passants, et tu as multiplié tes prostitutions.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
Tu t'es aussi livrée à l'impudicité avec les Égyptiens, tes voisins, grands par la chair, et tu as multiplié tes prostitutions, pour m'irriter.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
Voici donc que j'ai étendu ma main sur toi, que j'ai diminué ta part, et que je t'ai livrée à la volonté de celles qui te haïssent, les filles des Philistins, qui ont honte de ton impudicité.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
Tu t'es aussi prostituée avec les Assyriens, parce que tu étais insatiable; oui, tu t'es prostituée avec eux, et pourtant tu n'étais pas satisfaite.
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
Tu as en outre multiplié tes prostitutions jusqu'au pays des marchands, jusqu'en Chaldée; et pourtant tu n'as pas été satisfaite de cela.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
"« Que ton cœur est faible, dit le Seigneur Yahvé, puisque tu fais toutes ces choses, qui sont l'œuvre d'une prostituée impudente,
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
en ce que tu bâtis ta voûte à la tête de chaque chemin, et que tu fais ta place élevée dans chaque rue, et que tu n'as pas été comme une prostituée, en ce que tu méprises le salaire.
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
"« Femme adultère, qui prend des étrangers au lieu de son mari!
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
Les gens font des cadeaux à toutes les prostituées; mais toi, tu fais des cadeaux à tous tes amants, et tu les corromps, afin qu'ils viennent de tous côtés pour te prostituer.
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
Tu es différente des autres femmes dans ta prostitution, en ce que personne ne te suit pour se prostituer; et comme tu donnes un salaire, et qu'on ne te donne pas de salaire, tu es donc différente. »''
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
C'est pourquoi, prostituée, écoute la parole de Yahvé:
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
Le Seigneur Yahvé dit: Parce que ta souillure s'est répandue et que ta nudité a été découverte par tes prostitutions avec tes amants, à cause de toutes les idoles de tes abominations et du sang de tes enfants que tu leur as donné,
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
voici, je rassemblerai tous tes amants avec lesquels tu as pris plaisir, tous ceux que tu as aimés et tous ceux que tu as haïs. Je les rassemblerai même contre toi de toutes parts, et je leur découvrirai ta nudité, afin qu'ils voient toute ta nudité.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
Je te jugerai comme on juge les femmes qui rompent le mariage et versent le sang, et je ferai retomber sur toi le sang de la colère et de la jalousie.
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
Je te livrerai aussi entre leurs mains; ils jetteront tes voûtes et briseront tes hauts lieux. Ils te dépouilleront de tes vêtements et prendront tes beaux bijoux. Ils te laisseront nu et dénudé.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
Ils amèneront contre toi une troupe, ils te lapideront, ils te transperceront de leurs épées.
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
Ils brûleront vos maisons par le feu, et ils exerceront sur vous des jugements en présence de nombreuses femmes. Je te ferai cesser de te prostituer, et tu ne donneras plus de salaire.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
Je ferai en sorte que ma colère contre toi s'apaise, et que ma jalousie s'éloigne de toi. Je me tairai, et je ne me mettrai plus en colère.
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
"« Parce que tu ne t'es pas souvenu des jours de ta jeunesse, mais que tu t'es déchaîné contre moi en toutes ces choses, voici que je fais retomber ta voie sur ta tête, dit le Seigneur Yahvé: « et tu ne commettras plus cette infamie avec toutes tes abominations.
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
« Voici, tous ceux qui se servent de proverbes se serviront de ce proverbe contre toi, en disant: « Telle est la mère, telle est la fille ».
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
Tu es la fille de ta mère, qui a en horreur son mari et ses enfants, et tu es la sœur de tes sœurs, qui ont en horreur leurs maris et leurs enfants. Ta mère était une Hittite, et ton père un Amoréen.
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
Ta sœur aînée est Samarie, qui habite à ta gauche, elle et ses filles; et ta sœur cadette, qui habite à ta droite, est Sodome avec ses filles.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
Tu n'as pas marché dans leurs voies, tu n'as pas commis leurs abominations; mais bientôt tu t'es corrompue plus qu'eux dans toutes tes voies.
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
Je suis vivant, dit le Seigneur Yahvé, Sodome, ta sœur, n'a pas fait, elle et ses filles, ce que tu as fait, toi et tes filles.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
"''Voici ce qu'était l'iniquité de ta sœur Sodome: l'orgueil, l'abondance du pain et l'aisance prospère étaient chez elle et chez ses filles. Elle n'a pas non plus fortifié la main des pauvres et des nécessiteux.
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
Ils se sont montrés arrogants et ont commis des abominations devant moi. C'est pourquoi je les ai fait disparaître quand je l'ai vu.
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
Samarie n'a pas commis la moitié de tes péchés; mais toi, tu as multiplié tes abominations plus qu'elles, et tu as justifié tes sœurs par toutes les abominations que tu as commises.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
Tu portes toi-même ta propre honte, en ce que tu as jugé tes sœurs; par les péchés que tu as commis plus abominablement qu'elles, elles sont plus justes que toi. Oui, toi aussi, sois confondue, et porte ta honte, en ce que tu as justifié tes sœurs.
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
"« Je renverserai leur captivité, la captivité de Sodome et de ses filles, la captivité de Samarie et de ses filles, et la captivité de vos captifs au milieu d'eux;
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
afin que vous portiez votre propre honte, et que vous ayez honte de tout ce que vous avez fait, puisque vous leur êtes une consolation.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
Tes sœurs, Sodome et ses filles, retourneront dans leur ancien domaine; Samarie et ses filles retourneront dans leur ancien domaine; et toi et tes filles, vous retournerez dans votre ancien domaine.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
Car ta sœur Sodome n'a pas été mentionnée par ta bouche au jour de ton orgueil,
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
avant que ta méchanceté ne soit découverte, comme au temps de l'opprobre des filles de Syrie, et de toutes celles qui l'entourent, les filles des Philistins, qui te méprisent tout autour.
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
Tu as porté tes débauches et tes abominations, dit Yahvé.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
"'Car le Seigneur Yahvé dit: « Je vous traiterai aussi comme vous avez fait, vous qui avez méprisé le serment en rompant l'alliance.
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
Mais je me souviendrai de mon alliance avec toi aux jours de ta jeunesse, et j'établirai avec toi une alliance éternelle.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
Alors tu te souviendras de tes voies et tu auras honte quand tu recevras tes sœurs, tes aînées et tes cadettes; et je te les donnerai pour filles, mais non par ton alliance.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
J'établirai mon alliance avec vous. Alors vous saurez que je suis Yahvé;
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
afin que vous vous souveniez et que vous soyez confus, et que vous n'ouvriez plus la bouche à cause de votre honte, quand je vous aurai pardonné tout ce que vous avez fait, dit le Seigneur Yahvé.'"