< Ezekieli 16 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of the Lord was maad to me,
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
and he seide, Sone of man, make thou knowun to Jerusalem her abhomynaciouns; and thou schalt seie,
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
The Lord God seith these thingis. A! thou Jerusalem, thi rote and thi generacioun is of the lond of Canaan; thi fadir is Amorrei, and thi moder is Cetei.
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
And whanne thou were borun, thi nawle was not kit awei in the dai of thi birthe, and thou were not waischun in watir in to helthe, nethir saltid with salt, nether wlappid in clothis.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
An iye sparide not on thee, that it hauynge merci on thee, dide to thee oon of these thingis; but thou were cast forth on the face of erthe, in the castynge out of thi soule, in the dai in which thou were borun.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
Forsothe Y passide bi thee, and Y siy thee defoulid in thi blood; and Y seide to thee, whanne thou were in thi blood, Lyue thou; sotheli Y seide to thee in thi blood, Lyue thou.
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
Y yaf thee multiplied as the seed of a feeld, and thou were multiplied, and maad greet; and thou entridist, and camest fulli to wymmens ournyng; thi tetis wexiden greet, and thin heer wexide; and thou were nakid, and ful of schenschipe.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
And Y passide bi thee, and Y siy thee, and lo! thi tyme, the tyme of louyeris; and Y spredde abrood my clothing on thee, and Y hilide thi schenschipe. And Y swoor to thee, and Y made a couenaunt with thee, seith the Lord God, and thou were maad a wijf to me.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
And Y waischide thee in water, and Y clenside awei thi blood fro thee, and Y anoyntide thee with oile.
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
And Y clothide thee with clothis of dyuerse colours, and Y schodde thee in iacynct, and Y girde thee with biys;
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
and Y clothide thee with sutil thingis, and Y ournede thee with ournement.
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
And Y yaf bies in thin hondis, and a wrethe aboute thi necke; and Y yaf a ryng on thi mouth, and cerclis to thin eeris, and a coroun of fairnesse in thin heed.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
And thou were ourned with gold and siluer, and thou were clothid with biys and ray cloth with rounde ymagis, and many colours. Thou etist cleene flour of wheete, and hony, and oile, and thou were maad fair ful greetli; and thou encreessidist in to a rewme,
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
and thi name yede out in to hethene men for thi fairnesse; for thou were perfit in my fairnesse which Y hadde sett on thee, seith the Lord God.
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
And thou haddist trist in thi fairnesse, and didist fornicacioun in thi name; and thou settidist forth thi fornicacioun to ech that passide forth, that thou schuldist be maad his.
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
And thou tokist of my clothis, and madist to thee hiy thingis set aboute on ech side; and thou didist fornycacioun on tho, as it was not don, nether schal be don.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
And thou tokist the vessels of thi fairnesse, of my gold and of my siluer, which Y yaf to thee; and thou madist to thee ymagis of men, and didist fornycacioun in tho.
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
And thou tokist thi clothis of many colours, and thou were clothid in tho; and thou settidist myn oile and myn encence in the siyt of tho.
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And thou settidist my breed, which Y yaf to thee, flour of wheete, and oile, and hony, bi whiche Y nurschide thee, in the siyt of tho, in to odour of swetnesse; and it was don, seith the Lord God.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
And thou tokist thi sones and thi douytris, whiche thou gendridist to me, and offridist to tho, for to be deuourid. Whether thi fornicacioun is litil?
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
Thou offridist my sones, and yauest hem, and halewidist to tho.
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
And aftir alle thin abhomynaciouns and fornicaciouns, thou bithouytist not on the daies of thi yong wexynge age, whanne thou were nakid, and ful of schenschipe, and were defoulid in thi blood.
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
And after al thi malice, wo, wo bifelle to thee, seith the Lord God.
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
And thou bildidist to thee a bordel hous, and madist to thee a place of hordom in alle stretis.
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
At ech heed of the weie thou bildidist a signe of thin hordom, and madist thi fairnesse abhomynable; and thou departidist thi feet to ech man passynge forth, and multepliedist thi fornicaciouns.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
And thou didist fornicacioun with the sones of Egipt, thi neiyboris of grete fleischis, and thou multepliedist thi fornicacioun, to terre me to wraththe.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
Lo! Y schal stretch forth myn hond on thee, and Y schal take awei thi iustifiyng; and Y schal yyue thee in to the soulis of hem that haten thee, of the douytris of Palestyns, that ben aschamed in thi weie ful of greet trespas.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
And thou didist fornicacioun with the sones of Assiriens, for thou were not fillid yit; and after that thou didist fornicacioun, nether so thou were fillid.
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
And thou multipliedist thi fornycacioun in the lond of Canaan with Caldeis, and nether so thou were fillid.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
In what thing schal Y clense thin herte, seith the Lord God, whanne thou doist alle these werkis of a womman an hoore, and gredi axere?
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
For thou madist thi bordel hous in `the heed of ech weie, and thou madist thin hiy place in ech street; and thou were not maad as an hoore ful of anoiyng,
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
encreessynge prijs, but as a womman auowtresse, that bryngith in aliens on hir hosebonde.
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
Hiris ben youun to alle hooris, but thou hast youe hire to alle thi louyeris; and thou yauest to hem, that thei schulden entre to thee on ech side, to do fornycacioun with thee.
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
And it was don in thee ayens the custom of wymmen in thi fornycaciouns, and fornicacioun schal not be after thee; for in that that thou yauest hiris, and tokist not hiris, the contrarie was don in thee.
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
Therfor, thou hoore, here the word of the Lord.
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
The Lord God seith these thingis, For thi riches is sched out, and thi schenschipe is schewid in thi fornicaciouns on thi louyeris, and on the idols of thin abhomynaciouns, in the blood of thi sones, whiche thou yauest to hem; lo!
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
Y schal gadere to gidere alle thi louyeris, with whiche thou were meddlid, and alle men whiche thou louedist, with alle men whiche thou hatidist; and Y schal gadere hem on thee on ech side, and Y schal make nakid thi schenschipe bifore hem, and thei schulen se al thi filthe.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
And Y schal deme thee bi the domes of auoutressis, and schedinge out blood;
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
and Y schal yyue thee in to the blood of strong veniaunce, and of feruour. And Y schal yyue thee in to the hondis of hem, and thei schulen destrie thi bordel hous, and thei schulen destrie the place of thin hordom; and thei schulen make thee nakid of thi clothis, and thei schulen take awei the vessels of thi fairnesse, and thei schulen forsake thee nakid, and ful of schenschipe.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
And thei schulen bringe on thee a multitude, and thei schulen stoon thee with stoonys, and thei schulen sle thee with her swerdis.
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
And thei schulen brenne thin housis with fier, and thei schulen make domes in thee, bifor the iyen of ful many wymmen; and thou schalt ceese to do fornicacioun, and thou schalt no more yyue hiris.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
And myn indignacioun schal reste in thee, and my feruent loue schal be takun awei fro thee; and Y schal reste, and Y schal no more be wrooth,
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
for thou haddist not mynde on the daies of thi yong wexynge age, and thou terridist me to ire in alle these thingis. Wherfor and Y yaf thi weies in thin heed, seith the Lord God, and Y dide not aftir thi grete trespassis, in alle these thin abhomynaciouns.
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
Lo! ech man that seith a prouerbe comynli, schal take it in thee,
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
and schal seie, As the modir, so and the douytir of hir. Thou art the douyter of thi modir, that castide awey hir hosebonde and hir sones; and thou art the sister of thi sistris, that castiden a wei her hosebondis and her sones. Thi modir is Cetei, and thi fadir is Ammorrei;
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
and thi gretter sister is Samarie, sche and hir douytris, that dwellen at thi left side; but thi sistir lesse than thou, that dwellith at thi riyt side, is Sodom, and hir douytris.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
But thou yedist not in the weies of hem, nethir thou didist aftir the grete trespassis of hem; hast thou do almest a litil lesse cursidere dedis than thei, in alle thi weies?
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
Y lyue, seith the Lord God, for Sodom, thi sister, did not, sche and hir douytris, as thou didist, and thi douytris.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
Lo! this was the wickidnesse of Sodom, thi sister, pride, fulnesse of breed, and habundaunce, and idilnesse of hir, and of hir douytris; and thei puttiden not hond to a nedi man and pore.
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
And thei weren enhaunsid, and diden other abhominaciouns bifore me; and Y took hem awei, as thou hast seyn.
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
And Samarie synnede not the half of thi synnes, but thou hast ouercome hem in thi grete trespassis; and thou hast iustified thi sistris in alle thin abhomynaciouns, whiche thou wrouytist.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
Therfor and thou bere thi schenschipe, that hast ouercome thi sistris with thi synnes, and didist more cursidli than thei; for thei ben iustified of thee. Therfor and be thou schent, and bere thi schenschipe, which hast iustified thi sistris.
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
And Y schal conuerte and restore hem by the conuersioun of Sodom with hir douytris, and bi the conuersioun of Samarie and of hir douytris; and Y schal conuerte thi turnyng ayen in the myddis of hem,
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
that thou bere thi schenschipe, and be aschamed in alle thingis whiche thou didist, coumfortynge hem.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
And thi sister Sodom and hir doytris schulen turne ayen to her eldnesse; and Samarie and hir douytris shulen turne ayen to her eeldnesse; and thou and thi douytris turne ayen to youre eldnesse.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
Forsothe Sodom, thi sister, was not herd in thi mouth, in the dai of thi pride,
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
bifore that thi malice was schewid, as in this tyme, in to schenschipe of the douytris of Sirie, and of alle douytris in thi cumpas, of the douytris of Palestyn that ben aboute thee bi cumpas.
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
Thou hast bore thi greet trespas, and thi schenschipe, seith the Lord God.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
For the Lord God seith these thingis, And Y schal do to thee as thou dispisidist the ooth, that thou schuldist make voide the couenaunt;
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
and Y schal haue mynde on my couenaunt with thee in the daies of thi yongthe, and Y schal reise to thee a couenaunt euerlastynge.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
And thou schalt haue mynde on thi weies, and schalt be aschamed, whanne thou schalt resseyue thi sistris grettere than thou, with thi lesse sistris; and Y schal yyue hem in to douytris to thee, but not of thi couenaunt.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And Y schal reise my couenaunt with thee, and thou schalt wite, that Y am the Lord, that thou haue mynde, and be aschamed;
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
and that it be no more to thee to opene the mouth for thi schame, whanne Y schal be plesid to thee in alle thingis whiche thou didist, seith the Lord God.

< Ezekieli 16 >