< Ezekieli 15 >

1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
Le niheo amako ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
O ana’ondatio, Ino ty andikoara’ i vahey ty hatae bey? Ino ty singa’e te amo hatae añ’alao?
3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
Hangalam-baramba hao handranjian-draha? Handrambesam-pantake hao hampiradoradoam-balàñe?
4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
Hehe te ahifik’ añ’afo ao ho fandrehetse; tomontoe’ ty afo añ’ila’e roe, vaho ho mae ty añivo’e ao. Mañeva fitoloñañe hao?
5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
Inao! ie tsy ho nañeva hampitoloñeñe te ni-ary, àntsake t’ie mae ro tsy maha-pi-draha kanao finorototo.
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
Aa hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Hambañe ami’ty vahe amo hatae añ’ala ao, ie natoloko añ’ afo ho fandrehetse, ty nanolorako amo mpimone’ Ierosalaimeo.
7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Hampiatrefeko am’ iereo ty tareheko; ndra te miakatse ami’ty afo iereo mbe ho forototoe’ i afoy avao; vaho ho fohi’ areo te Izaho Iehovà, ie hatreatreko am’ iereo ty tareheko.
8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”
Hampangoakoaheko i taney ty amy nifotera’ iareo ahy hoe t’Iehovà Talè.

< Ezekieli 15 >