< Ezekieli 15 >

1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And the word of the Lord came to me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
Son of man, what shall be made of the wood of the vine, out of all the trees of the woods that are among the trees of the forests?
3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
Shall wood be taken of if, to do any work, or shall a pin be made of it for any vessel to hang thereon?
4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
Behold it is cast into the fire for fuel: the fire hath consumed both ends thereof, and the midst thereof is reduced to ashes: shall it be useful for any work?
5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
Even when it was whole it was not fit for work: how much less, when the fire hath devoured and consumed it, shall any work be made of it?
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
Therefore thus saith the Lord God: As the vine tree among the trees of the forests which I have given to the fire to be consumed, so will I deliver up the inhabitants of Jerusalem.
7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And I will set my face against them: they shall go out from fire, and fire shall consume them: and you shall know that I am the Lord, when I shall have set my face against them.
8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”
And I shall have made their land a wilderness, and desolate, because they have been transgressors, saith the Lord God.

< Ezekieli 15 >