< Ezekieli 15 >

1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And the word of the Lord came to me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
“Son of man, what can be made from the stalk of a vine, compared to all the plants of the woods that are among the trees of the forests?
3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
Can any wood be taken from it, so that it may be made into a work, or formed into a peg so as to hang some kind of vessel upon it?
4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
Behold, it is used in the fire as fuel. The fire consumes both its ends; and its middle is reduced to ashes. So how can it be useful for any work?
5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
Even when it was whole, it was unsuitable for a work. How much more so, when fire has devoured it and burned it up, will nothing of it be useful?
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
Therefore, thus says the Lord God: Like the stalk of the vine among the trees of the forests, which I have given to be devoured by fire, so will I deliver the inhabitants of Jerusalem.
7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And I will set my face against them. They will go away from fire, and yet fire will consume them. And you shall know that I am the Lord, when I will have set my face against them,
8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”
and when I will have made their land impassable and desolate. For they have stood forth as transgressors, says the Lord God.”

< Ezekieli 15 >