< Ezekieli 15 >
1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
HERRENs Ord kom til mig således:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
Menneskesøn! Hvad har Vinstokken forud for alle andre Træer, Ranken, som står iblandt Skovens Træer?
3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
Tager man Gavntræ deraf? Eller tager man deraf en Knag til at hænge alskens Redskaber på?
4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
Når den så oven i købet har været givet Ilden til Føde, så at Ilden har fortæret begge dens Ender, og Midten er svedet, duer den så til noget?
5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
Se, da den endnu var uskadt, brugtes den ikke til noget, endsige at den skulde kunne bruges til noget nu, da Ilden har fortæret den og den er svedet.
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
Derfor, så siger den Herre HERREN: Som det går Vinstokken blandt Skovens Træer, hvilke jeg giver Ilden til Føde, således giver jeg Jerusalems Indbyggere hen;
7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
jeg vender mit Åsyn imod dem; af Ilden slap de ud, men Ild skal dog fortære dem; og I skal kende, at jeg er HERREN, når jeg vender mit Åsyn imod dem.
8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”
Og jeg gør Landet øde, fordi de var troløse, lyder det fra den Herre HERREN.