< Ezekieli 15 >
1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
Du Menneskesøn! hvad har Træet af Vinstokken forud for alt andet Træ? den Vinkvist, som har været iblandt Skovens Træer?
3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
Mon man tager Træet deraf til at gøre et Arbejde deraf? eller mon man tager en Knag deraf til at hænge noget Redskab derpaa?
4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
Se, det gives til Ilden til at fortæres; naar da Ilden har fortæret begge Ender deraf, og det midterste deraf er forbrændt, mon det saa duer til noget Arbejde?
5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
Se, den Tid det var helt, da kunde intet Arbejde gøres deraf; hvor meget mindre kan noget Arbejde herefter gøres deraf, naar Ilden har fortæret det, og det er forbrændt?
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
Derfor, saa siger den Herre, Herre: Ligesom Vinstokkens Træ er iblandt Skovens Træer, hvilket jeg har givet Ilden at fortære: Saaledes har jeg hengivet Jerusalems Indbyggere.
7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Og jeg vil rette mit Ansigt imod dem, de ere udgangne af Uden, men Ilden skal dog fortære dem; og I skulle fornemme, at jeg er Herren, naar jeg retter mit Ansigt imod dem.
8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”
Og jeg vil gøre Landet øde, fordi de have været saare troløse, siger den Herre, Herre.