< Ezekieli 14 >
1 Tsiku lina ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kwa ine ndipo anakhala pansi pamaso panga.
Potem przyszedłszy do mnie mężowie z starszych Izraelskich, usiedli przedemną.
2 Ndipo Yehova anandipatsa uthenga uwu nati,
I stało sie słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
3 “Iwe mwana wa munthu, anthu awa ayika mtima pa mafano awo. Ayikanso maso awo pa zinthu zina zoyipa zopunthwitsa. Kodi ayembekezera kuti ndiwayankhe chimene atandifunse?
Synu człowieczy! ci mężowie złożyli plugawe bałwany swoje do serca swego, a nieprawość, która im jest ku obrażeniu. położyli przed twarzą swoją; mniemaszże, iż mię uprzejmie pytają o radę?
4 Tsono yankhula nawo ndi kuwawuza kuti zimene akunena Ambuye Yehova: ‘Ngati Mwisraeli aliyense ayika mtima wake pa mafano ndi kuyika maso ake pa zinthu zoyipa zopunthwitsa, kenaka nʼkupita kwa mneneri, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha molingana ndi kuchuluka kwa mafano ake.
Dlategoż powiedz im, i mów do nich: Tak mówi panujący Pan: Ktokolwiek z domu Izraelsiego położył plugawe bałwany swoje w sercu swojem, a nieprawość, która mu jest ku obrażeniu, położył przed twarzą swoją, a przyszedłby do proroka, Ja Pan odpowiem temu, który przyjdzie, o mnóstwie plugawych bałwanów jego.
5 Ine ndidzachita zimenezi kuti mwina nʼkukopa mitima ya anthu a Israeli, amene andisiya chifukwa cha mafano awo.’
Abym ułapał dom Izraelski w sercu ich, że się odwrócili odemnie od plugawych bałwanów swoich wszyscy zgoła.
6 “Nʼchifukwa chake uwawuze Aisraeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Lapani! Siyani mafano anu ndi ntchito zanu zonse zonyansa!
Przetoż rzecz do domu Izraelskiego: Tak mówi panujący Pan: Nawróćcie się, a cofnijcie się od plugawych bałwanów waszych, i od wszystkich obrzydliwości waszych odwróćcie twarz swoję.
7 “‘Ngati Mwisraeli wina aliyense kapena mlendo wina aliyense wokhala pakati pa Israeli adzichotsa yekha kwa Ine ndi kuyika mtima pa mafano ake ndi kuyikanso maso ake pa zinthu zopunthwitsa ndipo kenaka nʼkupita kwa mneneri kukafunsa nzeru, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha.
Bo ktobykolwiek z domu Izraelskiego i z przychodniów, którzy mieszkają w Izraelu, odwrócił się od naśladowania mnie, a położyłby plugawe bałwany swoje w sercu swem, i nieprawość, która mu jest ku obrażeniu, położyłby przed twarz swoją, i przyszedł by do proroka, aby mię przezeń pytał, Ja Pan odpowiem mu sam przez się,
8 Ine ndidzalimbana naye munthu ameneyo ndipo ndidzamusandutsa chitsanzo ndi chisudzo. Ndidzamuchotsa pakati pa anthu anga. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I postawię oblicze moje przeciw temu mężowi, i dam go na znak, i na przysłowie, a wytracę go z pośrodku ludu mojego; i dowiecie się, żem Ja Pan.
9 “‘Ndipo ngati mneneri anyengedwa nanenera, Ine Yehova ndiye ndamunyenga mneneri ameneyo, ndipo ndidzatambasula dzanja langa kumukantha ndi kumuwononga pakati pa anthu anga Aisraeli.
A gdyby się prorok dał zwieść, aby mówił słowo, Ja Pan zwiodłem proroka onego, i wyciągnę nań rękę swoję, i wygładzę go z pośrodku ludu mego Izraelskiego.
10 Iwo adzalangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Chilango cha wodzafunsira nzeru kwa mneneri chidzafanana ndi chilango cha mneneriyo.
I tak poniosą nieprawość swoję; jaka jest kaźń na tego, któryby się pytał, taka też kaźń na proroka będzie,
11 Ndidzachita zimenezi kuti Aisraeli asasocherenso kundisiya Ine ndi kuti asadziyipitsenso ndi machimo awo. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, akutero Ambuye Yehova.’”
Aby więcej nie błądził dom Izraelski odemnie, a nie mazali się więcej żadnemi przestępstwami swojemi, aby byli ludem moim, a Ja abym był Bogiem ich, mówi panujący Pan.
12 Yehova anayankhula nane kuti,
Znowu stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
13 “Iwe mwana wa munthu, ngati dziko lindichimwira posandikhulupirira, Ine ndidzatambasula dzanja langa kulikantha pochepetsa chakudya chake. Ndidzatumiza njala pa dzikolo ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Synu człowieczy! gdyby ziemia zgrzeszyła przeciwko mnie, dopuszczając się przestępstwa, tedy jeźlibym wyciągnął rękę moję na nią, a złamałbym jej łaskę chleba, i posłałbym na nią głód, i wytraciłbym z niej ludzi i zwierzęta;
14 Ngakhale anthu atatu awa, Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, akanangopulumutsa moyo wawo chifukwa cha chilungamo chawo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Choćby byli w pośrodku niej ci trzej mężowie, Noe, Danijel i Ijob, oni w sprawiedliwości swojej wybawiliby dusze swe, mówi panujący Pan.
15 “Kapena ndikanatumiza zirombo mʼdziko monse ndi kulisiya lopanda anthu, ndipo dzikolo nʼkukhala chipululu chakuti munthu sangadutse chifukwa cha zirombo.
Także jeźlibym zły zwierz przepuścił na ziemię, a osierociłby ją, i byłaby spustoszona, żeby jej nikt przechodzić nie mógł dla zwierza,
16 Apanso, ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo okha akanapulumuka, koma dziko likanasanduka chipululu.’
Jako żyję Ja, mówi panujący Pan, że choćby ci trzej mężowie byli w pośrodku jej, żadną miarąby nie wybawili synów ani córek: oniby tylko sami wybawieni byli, leczby ziemia spustoszona była.
17 “Kapena ndikanatumiza lupanga mʼdzikolo ndi kunena kuti, ‘Lupanga lipite mʼdziko monse,’ ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Albo jeźlibym przywiódł miecz na tę ziemię, a rzekłbym mieczowi: Przejdź przez tę ziemię, abym wytracił z niej ludzi i zwierzęta,
18 Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna kapena ana aakazi. Iwo okha akanapulumuka.’
Jako żyję Ja, mówi panujący Pan, że choćby ci trzej mężowie byli w pośrodku jej, żadną miarąby nie wybawili synów ani córek, aleby oni tylko sami byli wybawieni.
19 “Kapena ndikanatumiza mliri mʼdzikomo ndi kuonetsa ukali wanga pokhetsa magazi, kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Albo posłałlibym mór na tę ziemię, i wylałbym popędliwość swoję na nią ku wytraceniu, aby z niej ludzie i zwierzęta byli wytraceni.
20 Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti ngakhale Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, sakanatha ngakhale kupulumutsa mwana wamwamuna kapena wamkazi. Akanangodzipulumutsa okha chifukwa cha chilungamo chawo.
Że choćby Noe, Danijel i Ijob byli w pośrodku jej, jako żyję Ja, mówi panujący Pan, żadną miarąby ani syna ani córki nie wybawili, oniby tylko w sprawiedliwości swojej wybawili dusze swe.
21 “Pakuti Ambuye Yehova akuti: Kudzakhala zoopsa kwambiri pamene ndidzatumiza pa Yerusalemu zilango zanga zinayi izi: lupanga, njala, zirombo ndi mliri kuti ziwononge anthu ake ndi nyama zomwe!
Owszem, tak mówi panujący Pan: Choćbym cztery kaźni moje ciężkie, miecz, i głód, i zły zwierz, i mór posłał na Jeruzalem, abym wytracił z niego ludzi i zwierzęta,
22 Komabe padzakhala ena opulumuka, ana aamuna ndi ana aakazi amene adzatulutsidwa mʼdzikomo. Iwo adzabwera kwa inu, ndipo mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo, mitima yanu idzakhala pansi mukadzakumbukira chilango chimene ndinachita pa Yerusalemu.
A oto jeźliby zostali w nim, którzyby tego uszli, a wywiedzeni byli synowie albo córki, oto i oni muszą iść do was; i oglądacie drogę ich, i sprawy ich, i ucieszycie się nad tem złem, które przywiodę na Jeruzalem, nad wszystkiem, co przywiodę na nie.
23 Mitima yanu idzakhala pansi mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo. Tsono mudzadziwa kuti Yerusalemu sindinamuchite zimenezi popanda chifukwa, akutero Ambuye Yehova.”
A tak ucieszą was, gdy ujrzycie drogę ich i sprawy ich; i zrozumiecie, żem to wszystko nie darmo uczynił, com uczynił w nim, mówi panujący Pan.