< Ezekieli 14 >
1 Tsiku lina ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kwa ine ndipo anakhala pansi pamaso panga.
Og der kom Mænd af Israels Ældste til mig og sade for mit Ansigt.
2 Ndipo Yehova anandipatsa uthenga uwu nati,
Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
3 “Iwe mwana wa munthu, anthu awa ayika mtima pa mafano awo. Ayikanso maso awo pa zinthu zina zoyipa zopunthwitsa. Kodi ayembekezera kuti ndiwayankhe chimene atandifunse?
Du Menneskesøn! disse Mænd have givet deres Afguder Plads i deres Hjerte, og hvad der var dem Anstød til at synde, have de stillet for deres Ansigt; skulde jeg vel lade mig adspørge for dem?
4 Tsono yankhula nawo ndi kuwawuza kuti zimene akunena Ambuye Yehova: ‘Ngati Mwisraeli aliyense ayika mtima wake pa mafano ndi kuyika maso ake pa zinthu zoyipa zopunthwitsa, kenaka nʼkupita kwa mneneri, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha molingana ndi kuchuluka kwa mafano ake.
Derfor tal med dem, og sig til dem: Saa siger den Herre, Herre: Enhver Mand af Israels Hus, som giver sine Afguder Plads i sit Hjerte og stiller, hvad der var ham Anstød til at synde, for sit Ansigt og saa kommer til Profeten: For ham vil jeg, Herren, lade mig bringe til at svare desangaaende, nemlig angaaende hans Afguders Mangfoldighed,
5 Ine ndidzachita zimenezi kuti mwina nʼkukopa mitima ya anthu a Israeli, amene andisiya chifukwa cha mafano awo.’
for at jeg kan gribe Israels Hus ved deres Hjerte, fordi de vege fra mig alle sammen ved deres Afguder.
6 “Nʼchifukwa chake uwawuze Aisraeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Lapani! Siyani mafano anu ndi ntchito zanu zonse zonyansa!
Derfor sig til Israels Hus: Saa siger den Herre, Herre: Omvender eder, og vender eder bort fra eders Afguder, ja, vender eders Ansigter bort fra alle eders Vederstyggeligheder!
7 “‘Ngati Mwisraeli wina aliyense kapena mlendo wina aliyense wokhala pakati pa Israeli adzichotsa yekha kwa Ine ndi kuyika mtima pa mafano ake ndi kuyikanso maso ake pa zinthu zopunthwitsa ndipo kenaka nʼkupita kwa mneneri kukafunsa nzeru, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha.
Thi naar en Mand af Israels Hus eller af de fremmede, som opholde sig i Israel, skiller sig fra mig og giver sine Afguder Plads i sit Hjerte og stiller, hvad der var ham Anstød til at synde, for sit Ansigt og saa kommer til Profeten for at adspørge mig for sig: Ham vil jeg, Herren, lade mig bringe til at give et Svar fra mig selv.
8 Ine ndidzalimbana naye munthu ameneyo ndipo ndidzamusandutsa chitsanzo ndi chisudzo. Ndidzamuchotsa pakati pa anthu anga. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Og jeg vil rette mit Ansigt imod denne Mand og ødelægge ham, at han bliver til et Tegn og til et Ordsprog, og jeg vil udrydde ham af mit Folks Midte; og I skulle fornemme, at jeg er Herren.
9 “‘Ndipo ngati mneneri anyengedwa nanenera, Ine Yehova ndiye ndamunyenga mneneri ameneyo, ndipo ndidzatambasula dzanja langa kumukantha ndi kumuwononga pakati pa anthu anga Aisraeli.
Men naar Profeten lader sig overtale og taler noget, da har jeg, Herren, ladet denne Profet overtales; og jeg vil udrække min Haand over ham og ødelægge ham ud af mit Folk Israels Midte.
10 Iwo adzalangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Chilango cha wodzafunsira nzeru kwa mneneri chidzafanana ndi chilango cha mneneriyo.
Og de skulle bære deres Misgerning; som hans Misgerning er, der adspørger, saa skal Profetens Misgerning være,
11 Ndidzachita zimenezi kuti Aisraeli asasocherenso kundisiya Ine ndi kuti asadziyipitsenso ndi machimo awo. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, akutero Ambuye Yehova.’”
for at de af Israels Hus ikke mere skulle fare vild fra mig ej heller besmitte sig mere med nogen af deres Overtrædelser; men de skulle være mit Folk, og jeg skal være deres Gud, siger den Herre, Herre.
12 Yehova anayankhula nane kuti,
Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
13 “Iwe mwana wa munthu, ngati dziko lindichimwira posandikhulupirira, Ine ndidzatambasula dzanja langa kulikantha pochepetsa chakudya chake. Ndidzatumiza njala pa dzikolo ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Du Menneskesøn! naar et Land synder imod mig, saa at det bliver troløst imod mig, og jeg udrækker min Haand over det og formindsker Brøds Forraad for det, og jeg sender Hunger i det og udrydder Menneske og Fæ deraf,
14 Ngakhale anthu atatu awa, Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, akanangopulumutsa moyo wawo chifukwa cha chilungamo chawo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
men der var disse tre Mænd, Noa, Daniel Og Job derudi: Da skulde disse alene redde deres Sjæl ved deres Retfærdighed, siger den Herre, Herre.
15 “Kapena ndikanatumiza zirombo mʼdziko monse ndi kulisiya lopanda anthu, ndipo dzikolo nʼkukhala chipululu chakuti munthu sangadutse chifukwa cha zirombo.
Naatr jeg lader vilde Dyr gaa igennem Landet, og de berøve Folk deres Børn, og det blev øde, saa at ingen gaar der igennem for Dyrenes Skyld,
16 Apanso, ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo okha akanapulumuka, koma dziko likanasanduka chipululu.’
men hine tre Mænd vare derudi, saa sandt jeg lever, siger den Herre, Herre: De skulde hverken redde Sønner eller Døtre; de selv alene skulde reddes, men Landet vorde øde.
17 “Kapena ndikanatumiza lupanga mʼdzikolo ndi kunena kuti, ‘Lupanga lipite mʼdziko monse,’ ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Eller naar jeg lader Sværdet komme over det samme Land, og jeg siger: Sværd! du skal fare igennem Landet, og jeg udrydder Menneske og Fæ deraf,
18 Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna kapena ana aakazi. Iwo okha akanapulumuka.’
men hine tre Mænd vare derudi, saa sandt jeg lever, siger den Herre, Herre: De skulde ikke redde Sønner eller Døtre; men de alene skulde reddes.
19 “Kapena ndikanatumiza mliri mʼdzikomo ndi kuonetsa ukali wanga pokhetsa magazi, kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe.
Eller naar jeg sender Pest i det samme Land og udøser min Harme over det med Blod, saa at jeg udrydder Menneske og Fæ deraf,
20 Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti ngakhale Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, sakanatha ngakhale kupulumutsa mwana wamwamuna kapena wamkazi. Akanangodzipulumutsa okha chifukwa cha chilungamo chawo.
men Noa, Daniel og Job vare derudi, saa sandt jeg lever, siger den Herre, Herre: De skulde hverken redde Søn eller Datter; men de skulde redde deres egen Sjæl ved deres Retfærdighed.
21 “Pakuti Ambuye Yehova akuti: Kudzakhala zoopsa kwambiri pamene ndidzatumiza pa Yerusalemu zilango zanga zinayi izi: lupanga, njala, zirombo ndi mliri kuti ziwononge anthu ake ndi nyama zomwe!
Thi saa siger den Herre, Herre: Meget mere, naar jeg sender mine fire grumme Straffedomme over Jerusalem, nemlig: Sværd og Hunger og vilde Dyr og Pest for at udrydde Menneske og Fæ deraf,
22 Komabe padzakhala ena opulumuka, ana aamuna ndi ana aakazi amene adzatulutsidwa mʼdzikomo. Iwo adzabwera kwa inu, ndipo mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo, mitima yanu idzakhala pansi mukadzakumbukira chilango chimene ndinachita pa Yerusalemu.
og se, der bliver nogle undkomne tilovers, som bortføres, Sønner og Døtre: Se, de skulle gaa ud til eder, og I skulle se deres Vej og deres Gerninger; og I skulle trøste eder over den Ulykke, som jeg lod komme over Jerusalem, ja, alt det, som jeg lod komme over den.
23 Mitima yanu idzakhala pansi mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo. Tsono mudzadziwa kuti Yerusalemu sindinamuchite zimenezi popanda chifukwa, akutero Ambuye Yehova.”
Og de skulle trøste eder, naar I se deres Vej og deres Gerninger; og I skulle erkende, at jeg intet har gjort uden Grund af alt det, som jeg gjorde derudi, siger den Herre, Herre.