< Ezekieli 13 >

1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
و کلام خداوند بر من نازل شده، گفت:۱
2 “Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
«ای پسر انسان به ضد انبیای اسرائیل که نبوت می‌نمایند، نبوت نما. و به آنانی که ازافکار خود نبوت می‌کنند، بگو کلام خداوند رابشنوید!۲
3 Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
خداوند یهوه چنین می‌گوید: وای برانبیاء احمق که تابع روح خویش می‌باشند و هیچ ندیده‌اند.۳
4 Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
‌ای اسرائیل انبیای تو مانند روباهان درخرابه‌ها بوده‌اند.۴
5 Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
شما به رخنه‌ها برنیامدید ودیوار را برای خاندان اسرائیل تعمیر نکردید تاایشان در روز خداوند به جنگ بتوانند ایستاد.۵
6 Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
رویای باطل و غیب گویی کاذب می‌بینند ومی گویند: خداوند می‌فرماید، با آنکه خداوندایشان را نفرستاده است و مردمان را امیدوارمی سازند به اینکه کلام ثابت خواهد شد.۶
7 Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
آیارویای باطل ندیدید و غیب گویی کاذب را ذکرنکردید چونکه گفتید خداوند می‌فرماید با آنکه من تکلم ننمودم؟»۷
8 “Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
بنابراین خداوند یهوه چنین می‌فرماید: «چونکه سخن باطل گفتید و رویای کاذب دیدید، اینک خداوند یهوه می‌فرماید من به ضد شماخواهم بود.۸
9 Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
پس دست من بر انبیایی که رویای باطل دیدند و غیب گویی کاذب کردند درازخواهد شد و ایشان در مجلس قوم من داخل نخواهند شد و در دفتر خاندان اسرائیل ثبت نخواهند گردید و به زمین اسرائیل وارد نخواهندگشت و شما خواهید دانست که من خداوند یهوه می باشم.۹
10 “Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
و از این جهت که قوم مرا گمراه کرده، گفتند که سلامتی است در حینی که سلامتی نبودو یکی از ایشان دیوار را بنا نمود و سایرین آن رابه گل ملاط مالیدند.۱۰
11 choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
پس به آنانی که گل ملاطرا مالیدند بگو که آن خواهد افتاد. باران سیال خواهد بارید و شما‌ای تگرگهای سخت خواهیدآمد و باد شدید آن را خواهد شکافت.۱۱
12 Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
و هان چون دیوار بیفتد، آیا شما را نخواهند گفت: کجااست آن اندودی که به آن اندود گردید؟»۱۲
13 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
لهذا خداوند یهوه چنین می‌گوید: «من آن را به باد شدید در غضب خود خواهم شکافت وباران سیال در خشم من خواهد بارید و تگرگهای سخت برای فانی ساختن آن در غیظ من خواهدآمد.۱۳
14 Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
و آن دیوار را که شما به گل ملاط اندودکردید منهدم نموده، به زمین یکسان خواهم ساخت و پی آن منکشف خواهد شد. و چون آن بیفتد شما در میانش هلاک خواهید شد و خواهیددانست که من یهوه هستم.۱۴
15 Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
پس چون خشم خود را بر دیوار و بر آنانی که آن را به گل ملاطاندود کردند به اتمام رسانیده باشم، آنگاه به شماخواهم گفت: دیوار نیست شده و آنانی که آن رااندود کردند نابود گشته‌اند.۱۵
16 Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
یعنی انبیای اسرائیل که درباره اورشلیم نبوت می‌نمایند وبرایش رویای سلامتی را می‌بینند با آنکه خداوندیهوه می‌گوید که سلامتی نیست.۱۶
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
و تو‌ای پسرانسان نظر خود را بر دختران قوم خویش که ازافکار خود نبوت می‌نمایند بدار و بر ایشان نبوت نما،۱۷
18 Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
و بگو خداوند یهوه چنین می‌فرماید: وای بر آنانی که بالشها برای مفصل هر بازویی می‌دوزند و مندیلها برای سر هر قامتی می‌سازند تا جانها را صید کنند! آیا جانهای قوم مرا صیدخواهید کرد و جانهای خود را زنده نگاه خواهیدداشت؟۱۸
19 Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
و مرا در میان قوم من برای مشت جویی و لقمه نانی بی‌حرمت می‌کنید چونکه به قوم من که به دروغ شما گوش می‌گیرند دروغ گفته، جانهایی را که مستوجب موت نیستندمی کشید و جانهایی را که مستحق حیات نمی باشند زنده نگاه می‌دارید.۱۹
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
لهذا خداوندیهوه چنین می‌گوید: اینک من به ضد بالشهای شما هستم که به واسطه آنها جانها را مثل مرغان صید می‌کنید. و آنها را از بازوهای شما خواهم درید و کسانی را که جانهای ایشان را مثل مرغان صید می‌کنید، رهایی خواهم داد.۲۰
21 Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
و مندیلهای شما را خواهم درید و قوم خود را از دست شماخواهم رهانید و دیگر در دست شما نخواهند بودتا ایشان را صید کنید پس خواهید دانست که من یهوه هستم.۲۱
22 Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
چونکه شما به دروغ خود، دل مرد عادل را که من محزون نساختم، محزون ساخته‌اید و دستهای مرد شریر را تقویت داده ایدتا از رفتار قبیح خود بازگشت ننماید و زنده نشود.۲۲
23 choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
لهذا بار دیگر رویای باطل نخواهید دید وغیب گویی نخواهید نمود. و چون قوم خود را ازدست شما رهایی دهم، آنگاه خواهید دانست که من یهوه می‌باشم.»۲۳

< Ezekieli 13 >