< Ezekieli 13 >

1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
2 “Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
Ndodana yomuntu, profetha umelene labaprofethi bakoIsrayeli abaprofethayo, utsho kubo abaprofetha okwenhliziyo yabo: Zwanini ilizwi leNkosi.
3 Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
Itsho njalo iNkosi uJehova: Maye kubaprofethi abayizithutha, abalandela umoya wabo, abangabonanga lutho!
4 Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
Israyeli, abaprofethi bakho banjengamakhanka emanxiweni.
5 Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
Kalenyukelanga ezikhexeni, kumbe libiyele indlu kaIsrayeli uthango ukuze ime empini ngosuku lweNkosi.
6 Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
Babone okuyize, lokuvumisa kwamanga, abathi: INkosi ithi; kanti iNkosi ingabathumanga; bathemba ekuqinisweni kwelizwi.
7 Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
Kalibonanga yini umbono oyize njalo likhulume ukuvumisa okungamanga yini? Kanti lithi: INkosi ithi; kodwa mina ngingakhulumanga.
8 “Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
Ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Ngoba likhulume okuyize, labona amanga, ngakho, khangelani, ngimelene lani, itsho iNkosi uJehova.
9 Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
Njalo isandla sami sizakuba phezu kwabaprofethi ababona okuyize, labavumisa amanga; kabayikuba senhlanganweni yabantu bami, futhi kabayikubhalwa embhalweni wendlu yakoIsrayeli, futhi kabayikungena elizweni lakoIsrayeli; njalo lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi uJehova.
10 “Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
Ngoba, yebo ngoba beduhise abantu bami, besithi: Ukuthula; khona kungelakuthula; kwathi omunye wakha umduli ongaqinanga, khangela-ke, abanye bawubhada ngodaka olungalunganga.
11 choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
Tshono kulabo abawubhada ngekalaga ukuthi uzakuwa. Kuzakuba khona izulu elikhukhulayo; lawe, matshe amakhulu esiqhotho, uzakuwa, lomoya wesiphepho uwuqhekeze.
12 Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
Khangela-ke, nxa umduli usuwile, kakuyikutshiwo yini kini ukuthi: Lungaphi udaka elalibhade ngalo?
13 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
Ngakho itsho njalo iNkosi uJehova: Ngizawuqhekeza ngomoya wesiphepho ekuthukutheleni kwami, kube khona izulu elikhukhulayo ngolaka lwami, lamatshe esiqhotho ngentukuthelo yami ukuwuqeda.
14 Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Ngokunjalo ngizadiliza umduli eliwubhade ngekalaga, ngiwuwisele emhlabathini, ukuze kwembuleke isisekelo sawo, uwe; njalo lizaqedwa phakathi kwawo; njalo lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
15 Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
Ngokunjalo ngizaphelelisa ulaka lwami emdulini laphezu kwalabo abawubhade ngekalaga, besengisithi kini: Umduli kawusekho, lalabo abawubhadayo kabakho;
16 Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
okutsho abaprofethi bakoIsrayeli abaprofetha ngeJerusalema, labayibonela umbono wokuthula, kanti kungelakuthula, itsho iNkosi uJehova.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
Wena-ke ndodana yomuntu, misa ubuso bakho bumelene lamadodakazi abantu bakho, abaprofetha okuvela enhliziyweni yabo, uprofethe umelene labo.
18 Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
Ubususithi: Itsho njalo iNkosi uJehova: Maye kwabesifazana abathungela izigqizo kuzo zonke izihlakala, abenza izimbombozo ezinde phezu kwekhanda labo bonke ubude, ukuze bazingele imiphefumulo! Lizazingela imiphefumulo yabantu bami yini, njalo lizazigcinela imiphefumulo iphila yini?
19 Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
Futhi lizangingcolisa yini phakathi kwabantu bami ngenxa yezandla ezigcwele ibhali, langenxa yezincezu zezinkwa, ukuthi libulale imiphefumulo ebingayikufa, lokuthi ligcine iphila imiphefumulo ebingayikuphila, ngokuqamba amanga kwenu ebantwini bami abalalela amanga?
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
Ngalokho itsho njalo iNkosi uJehova: Khangelani, ngimelene lezigqizo zenu, elizingela ngazo lapho imiphefumulo liyenza iphaphe; ngizaziqamula engalweni zenu, ngiyekele imiphefumulo ihambe, ngitsho imiphefumulo eliyizingelayo liyenza iphaphe.
21 Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Lezimbombozo zenu ezinde ngizazidabula, ngophule abantu bami esandleni senu, ukuthi bengasayikuba sesandleni senu ukuba yimpango; njalo lizakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
22 Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
Ngoba lidanisile inhliziyo yolungileyo ngamanga, engingamdabukisanga mina, langoba laqinisa izandla zomubi ukuze angaphenduki endleleni yakhe embi, ukumgcina ephila.
23 choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Ngakho kalisayikubona okuyize njalo kaliyikuvumisa okuvunyiswayo; ngoba ngizakophula abantu bami esandleni senu; beselisazi ukuthi ngiyiNkosi.

< Ezekieli 13 >