< Ezekieli 13 >
1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And the word of Yahweh came unto me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
Son of man. prophesy against the prophets of Israel, who are prophesying, —and say unto them who prophesy out of their own heart, Hear ye the word of Yahweh,
3 Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
Thus, saith My Lord, Yahweh, Alas for the base prophets, —who follow their own spirit and have seen, nothing.
4 Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
As jackals, among ruins, thy prophets O Israel have been.
5 Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
Ye have not gone up into the breaches, Nor built a wall about the house of Israel, - to stand in the battle in the day of Yahweh.
6 Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
They have had Visions of falsehood, and Divinations of lies, Who say. Declareth Yahweh, when, Yahweh, hath not sent them, — Yet have they waited for a fulfilling of the word.
7 Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
Is it not a Vision of falsehood, ye have seen, and a Divination of lies, ye have spoken, Since ye are saying. Declareth Yahweh! when I have not spoken?
8 “Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
Therefore Thus saith My Lord Yahweh, Because ye have spoken falsehood, And have had visions of lies, Therefore behold me! against you, Declareth My Lord Yahweh.
9 Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
So then my hand shall be against the prophets who have Visions of falsehood and who divine Divinations of lies— In the council of my people, shall they not be found. And in the register of the house of Israel, shall they not be written, And Upon the so of Israel, shall they not enter, — So shall ye know that, I, am The Lord Yahweh,
10 “Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
Because, yea, even because, they have led astray my people saying. Prosperity! when there was no prosperity, —and one man, was building a partition wall, when there they were! eating it with whitewash
11 choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
Say thou unto them who are coating with whitewash It shall fall, - There hath come an overflowing rain And I will make hail-stones fall, And a tempestuous wind shall break it down.
12 Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
Lo! when the wall hath fallen, shall it not be said unto you, Where is the coating, wherewith ye coated it?
13 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
Therefore Thus saith my Lord, Yahweh, So will I break down with a tempestuous wind. in mine indignation, — And an overflowing rain in mine anger, shall there be, With hailstones in wrath to make an end;
14 Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And I will pull down the wall which ye have coated with whitewash And will bring it unto the ground So shall be discovered its foundation, Yea it shall fall And ye shall come to an end in the midst thereof, So shall ye know that, I, am Yahweh.
15 Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
Thus will I bring to an end mine indignation against the wall, and against them who were coating it with whitewash, And will say to you No more is the wall, And no more are they who were coating it:
16 Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
to wit the prophets of Israel who are prophesying unto Jerusalem, and are seeing, on her behalf, visions of prosperity, — when there is no prosperity, Declareth My Lord Yahweh.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
And thou, Son of man Set thy face against the daughters of thy people, Those who are prophesying out of their own heart, — And prophesy thou against them;
18 Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
and say, Thus, saith My Lord Yahweh, Alas! for the women Who sew oracle, cases on all elbows And prepare wraps upon the head of every stature to hunt souls, — the souls ye hunt, are those of my people, Whereas your own souls: , ye keep alive.
19 Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
Thus have ye profaned me unto my people for handfuls of barley and for pieces of bread, Putting to death the souls that should not die, and Keeping alive the souls that should not live, — By your lying to my people, who hearken to lies
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
Therefore, Thus saith my Lord Yahweh, Behold me! against your oracle-cases wherewith ye are hunting the souls to make them fly, And I will tear them off your arms, And let go the souls of them whose souls ye are hunting as birds;
21 Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And will tear off your wraps, And deliver my people out of your hand, And they shall be no longer in your hand to be hunted; - So shall ye know that, I, am Yahweh.
22 Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
Because of the paining of the heart of the righteous man with falsehood, whom, I, have not pained, — And strengthening the hands of the lawless man, that he should not turn from his wicked way. by letting him live
23 choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Therefore—of falsehood: , shall ye have no vision, And a divination: , shall ye not divine any more, — So will I deliver my people out of your hand, And ye shall know that, I, am Yahweh.