< Ezekieli 13 >

1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And the word of the Lord came vnto me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
Sonne of man, prophecie against the prophets of Israel, that prophecie, and say thou vnto them, that prophecie out of their owne hearts, Heare the worde of the Lord.
3 Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
Thus sayth the Lord God, Woe vnto the foolish Prophets that follow their owne spirit, and haue seene nothing.
4 Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
O Israel, thy Prophets are like the foxes in the waste places.
5 Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
Ye haue not risen vp in the gappes, neither made vp the hedge for ye house of Israel, to stand in the battel in the daye of the Lord.
6 Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
They haue seene vanitie, and lying diuination, saying, The Lord sayth it, and the Lord hath not sent them: and they haue made others to hope that they would cofirme the word of their prophecie.
7 Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
Haue ye not seene a vaine vision? and haue yee not spoken a lying diuination? ye say, The Lord sayth it, albeit I haue not spoken.
8 “Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
Therefore thus sayth the Lord God, Because ye haue spoken vanytie and haue seene lyes, therefore beholde, I am agaynst you, sayth the Lord God,
9 Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
And mine hande shalbe vpon the Prophets that see vanity, and diuine lies: they shall not be in the assemblie of my people, neither shall they be written in the writing of the house of Israel, neither shall they enter into the land of Israel: and yee shall know that I am the Lord God.
10 “Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
And therefore, because they haue deceiued my people, saying, Peace, and there was no peace: and one buylt vp a wall, and behold, the others daubed it with vntempered morter,
11 choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
Say vnto them which daube it with vntempered morter, that it shall fall: for there shall come a great showre, and I wil sende haylestones, which shall cause it to fall, and a stormie winde shall breake it.
12 Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
Lo, when the wall is fallen, shall it not bee sayd vnto you, Where is the daubing wherewith ye haue daubed it?
13 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
Therefore thus sayth the Lord God, I will cause a stormie winde to breake foorth in my wrath, and a great showre shall bee in mine anger, and hailestones in mine indignation to consume it.
14 Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
So I wil destroy the wall that ye haue daubed with vntempered morter, and bring it downe to the ground, so that the fundation thereof shalbe discouered, and it shall fal, and ye shalbe consumed in the middes thereof, and ye shall know, that I am the Lord.
15 Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
Thus will I accomplish my wrath vpon the wall, and vpon them that haue daubed it with vntempered morter, and will say vnto you, The wall is no more, neither the daubers thereof,
16 Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
To wit, the Prophets of Israel, which prophesie vpon Ierusalem, and see visions of peace for it, and there is no peace, sayth the Lord God.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
Likewise thou sonne of man, set thy face against the daughters of thy people, which prophesie out of their owne heart: and prophesie thou against them, and say,
18 Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
Thus sayth the Lord God, Woe vnto the women that sowe pillowes vnder al arme holes, and make vailes vpon the head of euery one that standeth vp, to hunt soules: will yee hunt ye soules of my people, and will yee giue life to the soules that come vnto you?
19 Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
And will ye pollute me among my people for handfuls of barly, and for pieces of bread to slay the soules of them that shoulde not dye, and to giue life to the soules that should not liue in lying to my people, that heare your lies?
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
Wherefore thus saith the Lord God, Behold, I will haue to do with your pillowes, wherewith yee hunt the soules to make them to flie, and I will teare them from your armes, and will let the soules goe, euen the soules, that ye hunt to make them to flie.
21 Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Your vailes also will I teare, and deliuer my people out of your hande, and they shalbe no more in your hands to be hunted, and ye shall knowe that I am the Lord.
22 Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
Because with your lyes yee haue made the heart of the righteous sadde, whome I haue not made sad, and strengthened the hands of the wicked, that he should not returne from his wicked way, by promising him life,
23 choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
Therefore ye shall see no more vanitie, nor diuine diuinatios: for I wil deliuer my people out of your hand, and ye shall know that I am ye Lord.

< Ezekieli 13 >