< Ezekieli 13 >
1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
HERRENS Ord kom til mig saaledes:
2 “Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
Menneskesøn, profetér mod Israels Profeter, profetér og sig til dem, som profeterer efter deres eget Hjertes Tilskyndelse: Hør HERRENS Ord!
3 Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
Saa siger den Herre HERREN: Ve Profeterne, de Daarer, som følger deres egen Aand uden at have skuet noget!
4 Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
Dine Profeter, Israel, er som Sjakaler i Ruiner.
5 Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
De stillede sig ikke i Murbruddet og byggede ikke en Mur om Israels Hus, saa det kunde staa sig i Striden paa HERRENS Dag.
6 Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
De skuede Tomhed og spaaede Løgn, idet de sagde: »Saa lyder det fra HERREN!« uden at HERREN havde sendt dem, og dog ventede de Ordet stadfæstet,
7 Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
Var det ikke tomme Syner, I skuede, og Løgnespaadomme, I fremsatte? Og I siger: »Saa lyder det fra HERREN!« uden at jeg har talet.
8 “Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
Derfor, saa siger den Herre HERREN: Fordi I forkynder Tomhed og skuer Løgn, se, derfor kommer jeg over eder, lyder det fra den Herre HERREN.
9 Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
Jeg udrækker min Haand mod Profeterne, der skuer Tomhed og spaar Løgn; i mit Folks Samfund skal de ikke være, de skal ikke optages i Israels Hus's Mandtalsbog og ikke komme til Israels Land; og I skal kende, at jeg er den Herre HERREN.
10 “Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
Fordi, ja fordi de vildleder mit Folk ved af forkynde Fred, hvor ingen Fred er, og naar det bygger en Væg, stryger den over med Kalk,
11 choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
saa sig til dem, der stryger over med kalk: Skylregn skal komme, Isstykker skal falde og Stormvejr bryde løs,
12 Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
og naar saa Væggen styrter sammen, vil man da ikke spørge eder: »Hvor er Kalken, I strøg paa?«
13 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
Derfor, saa siger den Herre HERREN: Og jeg lader et Stormvejr bryde løs i min Harme, og Skylregn skal komme i min Vrede og Isstykker i min Harme til Undergang;
14 Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
og Væggen, som I strøg over med Kalk, river jeg ned og lader den styrte til Jorden, saa dens Grundvold blottes, og ved dens Fald skal I gaa til Grunde derinde; og I skal kende, at jeg er HERREN.
15 Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
Jeg vil udtømme min Vrede over Væggen og dem, der strøg den over med Kalk, saa man skal sige til eder: »Hvor er Væggen, og hvor er de, som strøg den over,
16 Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
Israels Profeter, som profeterede om Jerusalem og skuede Fredssyner for det, hvor ingen Fred var« — lyder det fra den Herre HERREN.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
Og du, Menneskesøn, vend dit Ansigt mod dit Folks Døtre, som profeterer efter deres eget Hjertes Tilskyndelse; profeter imod dem
18 Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
og sig: Saa siger den Herre HERREN: Ve dem, der syr Bind til alle Haandled og laver Slør til alle Hoveder efter hver Legemshøjde for at fange Sjæle! Dræber I Sjæle, der hører til mit Folk, og holder Sjæle i Live af Egennytte?
19 Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
I, som vanhelliger mig for mit Folk for nogle Haandfulde Bygkorn og nogle Bidder Brød og saaledes dræber Sjæle, der ikke skulde dø, og holder Sjæle i Live, som ikke skulde leve, idet I lyver for mit Folk, som gerne hører paa Løgn!
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
Derfor, saa siger den Herre HERREN: Se, jeg kommer over eders Bind, med hvilke I fanger Sjæle, og river dem af eders Arme, og de Sjæle, I fanger, lader jeg slippe fri som Fugle;
21 Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
og jeg sønderriver eders Slør og frier mit Folk af eders Haand, saa de ikke mere er Bytte i eders Haand; og I skal kende, at jeg er HERREN.
22 Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
Fordi I ved Svig volder den retfærdiges Hjerte Smerte, skønt jeg ikke vilde volde ham Smerte, og styrker den gudløses Hænder, saa han ikke omvender sig fra sin onde Vej, at jeg kan holde ham i Live,
23 choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
derfor skal I ikke mere skue Tomhed eller drive eders Spaadomskunst; jeg frier mit Folk af eders Haand; og I skal kende, at jeg er HERREN.