< Ezekieli 12 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
And it came [the] word of Yahweh to me saying.
2 “Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
O son of humankind in [the] midst of [the] house of rebellion you [are] dwelling whom eyes [belong] to them to see and not they see ears [belong] to them to hear and not they hear for [are] a house of rebellion they.
3 “Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
And you O son of humankind prepare for yourself baggage of exile and go into exile by day to eyes their and you will go into exile from place your to a place another to eyes their perhaps they will see for [are] a house of rebellion they.
4 Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
And you will bring out baggage your like baggage of exile by day to eyes their and you you will go out in the evening to eyes their like goings out of exile.
5 Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
To eyes their dig yourself in the wall and you will bring out in it.
6 Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
To eyes their on a shoulder you will lift [it] up in the darkness you will bring [it] out face your you will cover and not you will see the land for a sign I have made you to [the] house of Israel.
7 Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
And I did so just as I was commanded baggage my I brought out like baggage of exile by day and in the evening I dug myself in the wall by hand in the darkness I brought [it] out on a shoulder I lifted [it] up to eyes their.
8 Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
And it came [the] word of Yahweh to me in the morning saying.
9 “Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
O son of humankind ¿ not have they said to you [the] house of Israel [the] house of rebellion what? [are] you doing.
10 “Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
Say to them thus he says [the] Lord Yahweh [is] the prince the oracle this in Jerusalem and all [the] house of Israel who they [are] in midst of them.
11 Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
Say I [am] sign your just as I have done so it will be done to them in exile in captivity they will go.
12 “Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
And the prince who [is] in midst of them to a shoulder he will lift up in the darkness so he may go out in the wall they will dig to bring out in it face his he will cover because that not he will see to the eye he the land.
13 Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
And I will spread net my over him and he will be caught in hunting net my and I will bring him Babylon towards [the] land of [the] Chaldeans and it not he will see and there he will die.
14 Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
And all [those] who [are] around him (help his *Q(K)*) and all troops his I will disperse to every wind and a sword I will draw after them.
15 “Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
And they will know that I [am] Yahweh when scatter I them among the nations and I will disperse them among the lands.
16 Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
And I will leave over some of them people of number from [the] sword from [the] famine and from [the] pestilence so that they may recount all abominations their among the nations where they have gone there and they will know that I [am] Yahweh.
17 Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
And it came [the] word of Yahweh to me saying.
18 “Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
O son of humankind food your in quaking you will eat and water your in trembling and in anxiety you will drink.
19 Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
And you will say to [the] people of the land thus he says [the] Lord Yahweh of [the] inhabitants of Jerusalem concerning [the] land of Israel food their in anxiety they will eat and water their in horror they will drink so that it may be desolate land its from fullness its from [the] violence of all the inhabitants in it.
20 Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
And the cities inhabited they will be waste and the land a desolation it will become and you will know that I [am] Yahweh.
21 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And it came [the] word of Yahweh to me saying.
22 “Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
O son of humankind what? [is] the proverb this to you on [the] land of Israel saying they are long the days and it perishes every vision.
23 Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
Therefore say to them thus he says [the] Lord Yahweh I will make to cease the proverb this and not people will use as a proverb it again in Israel that except speak to them they have drawn near the days and [the] matter of every vision.
24 Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
For not it will be again any vision of worthlessness and divination of flattery in [the] midst of [the] house of Israel.
25 Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
For - I Yahweh I will speak which I will speak a word so it may be done not it will be postponed again for in days your O house of rebellion I will speak a word and I will do it [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
26 Yehova anandiyankhula nati:
And it came [the] word of Yahweh to me saying.
27 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
O son of humankind there! [the] house of Israel [are] saying the vision which he [is] seeing [is] of days many and of times distant he [is] prophesying.
28 “Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”
Therefore say to them thus he says [the] Lord Yahweh not it will be postponed again all words my [that] which I will speak a word so it may be done [the] utterance of [the] Lord Yahweh.

< Ezekieli 12 >