< Ezekieli 12 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of the Lord came to me, saying:
2 “Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
“Son of man, you live in the midst of a provoking house. They have eyes to see, and they do not see; and ears to hear, and they do not hear. For they are a provoking house.
3 “Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
As for you, then, son of man, prepare for yourself the supplies for traveling far away, and travel away in the daytime in their sight. And you shall travel from your place to another place in their sight, so that perhaps they may consider it. For they are a provoking house.
4 Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
And you shall carry your supplies outside, like the supplies of one who is traveling far away, in the daytime in their sight. Then you shall go forth in the evening in their presence, just as one goes forth who is moving far away.
5 Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
Dig for yourself through the wall, before their eyes. And you shall go out through it.
6 Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
In their sight, you shall be carried on shoulders, you shall be carried in the dark. You shall cover your face, and you shall not see the ground. For I have appointed you as a portent for the house of Israel.”
7 Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
Therefore, I did just as he had instructed me. I brought out my supplies in the daytime, like the supplies of one who is moving far away. And in the evening, I dug myself through the wall by hand. And I went out in the dark, and I was carried on shoulders, in their sight.
8 Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
And the word of the Lord came to me, in the morning, saying:
9 “Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
“Son of man, has not the house of Israel, the provoking house, said to you: ‘What are you doing?’
10 “Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
Say to them: Thus says the Lord God: This is the burden concerning my leader who is in Jerusalem, and concerning the entire house of Israel, who are in their midst.
11 Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
Say: I am your portent. Just as I have done, so shall it be done to them. They will be taken captive and moved far away.
12 “Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
And the leader who is in their midst will be carried on shoulders; he will go forth in darkness. They will dig through the wall, so that they may lead him away. His face will be covered, so that he may not see the land with his eye.
13 Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
And I will extend my net over him, and he will be captured in my dragnet. And I will lead him to Babylon, into the land of the Chaldeans, but he himself will not see it. And there he shall die.
14 Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
And all who are around him, his guards and his companies, I will scatter into every wind. And I will unsheathe the sword after them.
15 “Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
And they shall know that I am the Lord, when I will have dispersed them among the Gentiles, and will have sowed them among the lands.
16 Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
And I will leave behind a few men of them, apart from the sword, and the famine, and the pestilence, so that they may declare all their wicked deeds among the Gentiles, to whom they will go. And they shall know that I am the Lord.”
17 Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
And the word of the Lord came to me, saying:
18 “Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
“Son of man, eat your bread in consternation. Moreover, drink your water hurriedly and in sorrow.
19 Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
And say to the people of the land: Thus says the Lord God, to those who are living in Jerusalem, in the land of Israel: They shall eat their bread in anxiety, and drink their water in desolation, so that the land may be desolate before its multitude, because of the iniquity of all who are living in it.
20 Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
And cities that are now inhabited will become desolate, and the land will be forsaken. And you shall know that I am the Lord.”
21 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And the word of the Lord came to me, saying:
22 “Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
“Son of man, what is this proverb that you have in the land of Israel? saying: ‘The days shall be extended in length, and every vision shall perish.’
23 Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
Therefore, say to them: Thus says the Lord God: I will cause this proverb to cease, and it shall no longer be a common saying in Israel. And tell them that the days are approaching, and the word of every vision.
24 Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
For there shall no longer be any empty visions, nor any ambiguous divination in the midst of the sons of Israel.
25 Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
For I, the Lord, will speak. And whatever word I will speak, it shall be done, and it shall not be delayed any more. Instead, in your days, O provoking house, I will speak a word and do it, says the Lord God.”
26 Yehova anandiyankhula nati:
And the word of the Lord came to me, saying:
27 “Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
“Son of man, behold the house of Israel, those who are saying: ‘The visions that this one sees is many days away,’ and, ‘This man prophesies about times that are far away.’
28 “Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”
Because of this, say to them: Thus says the Lord God: No word of mine will be delayed any longer. The word that I will speak will be fulfilled, says the Lord God.”

< Ezekieli 12 >