< Ezekieli 11 >

1 Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya.
Moreover the spirit lifted me up, and brought me unto the east gate of the LORD’S house, which looketh eastward: and behold, at the door of the gate five and twenty men; and I saw in the midst of them Jaazaniah the son of Azzur, and Pelatiah the son of Benaiah, princes of the people.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo.
And he said unto me, Son of man, these are the men that devise iniquity, and that give wicked counsel in this city.
3 Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo.
which say, [The time] is not near to build houses: this [city] is the caldron, and we be the flesh.
4 Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’”
Therefore prophesy against them, prophesy, O son of man.
5 Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’
And the spirit of the LORD fell upon me, and he said unto me, Speak, Thus saith the LORD: Thus have ye said, O house of Israel; for I know the things that come into your mind.
6 Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.
Ye have multiplied your slain in this city, and ye have filled the streets thereof with the slain.
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo.
Therefore thus saith the Lord GOD: Your slain whom ye have laid in the midst of it, they are the flesh, and this [city] is the caldron: but ye shall be brought forth out of the midst of it.
8 Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye.
Ye have feared the sword; and I will bring the sword upon you, saith the Lord GOD.
9 Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni.
And I will bring you forth out of the midst thereof, and deliver you into the hands of strangers, and will execute judgments among you.
10 Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Ye shall fall by the sword; I will judge you in the border of Israel; and ye shall know that I am the LORD.
11 Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli.
This [city] shall not be your caldron, neither shall ye be the flesh in the midst thereof; I will judge you in the border of Israel;
12 Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’”
and ye shall know that I am the LORD: for ye have not walked in my statutes, neither have ye executed my judgments, but have done after the ordinances of the nations that are round about you.
13 Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”
And it came to pass, when I prophesied, that Pelatiah the son of Benaiah died. Then fell I down upon my face, and cried with a loud voice, and said, Ah Lord GOD! wilt thou make a full end of the remnant of Israel?
14 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of the LORD came unto me, saying,
15 “Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’”
Son of man, thy brethren, even thy brethren, the men of thy kindred, and all the house of Israel, all of them, [are they] unto whom the inhabitants of Jerusalem have said, Get you far from the LORD; unto us is this land given for a possession:
16 “Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’
Therefore say, Thus saith the Lord GOD: Whereas I have removed them far off among the nations, and whereas I have scattered them among the countries, yet will I be to them a sanctuary for a little while in the countries where they are come.
17 “Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.
Therefore say, Thus saith the Lord GOD: I will gather you from the peoples, and assemble you out of the countries where ye have been scattered, and I will give you the land of Israel.
18 “Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa.
And they shall come thither, and they shall take away all the detestable things thereof and all the abominations thereof from thence.
19 Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu.
And I will give them one heart, and I will put a new spirit within you; and I will take the stony heart out of their flesh, and will give them an heart of flesh:
20 Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
that they may walk in my statutes, and keep mine ordinances, and do them: and they shall be my people, and I will be their God.
21 Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
But as for them whose heart walketh after the heart of their detestable things and their abominations, I will bring their way upon their own heads, saith the Lord GOD.
22 Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
Then did the cherubim lift up their wings, and the wheels were beside them; and the glory of the God of Israel was over them above.
23 Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo.
And the glory of the LORD went up from the midst of the city, and stood upon the mountain which is on the east side of the city.
24 Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera. Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira.
And the spirit lifted me up, and brought me in the vision by the spirit of God into Chaldea, to them of the captivity. So the vision that I had seen went up from me.
25 Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.
Then I spake unto them of the captivity all the things that the LORD had shewed me.

< Ezekieli 11 >