< Ezekieli 10 >

1 Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro.
Then I saw, and, behold, on the vault that was above the head of the cherubim, there appeared over them something like a sapphire stone, something similar in appearance to the likeness of a throne.
2 Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.
And he said unto the man clothed in linen, and said, Go in between the wheels, under the cherub, and fill thy hands with coals of fire from between the cherubim, and throw [them] over the city. And he went in before my eyes.
3 Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati.
Now the cherubim were standing on the right side of the house, when the man went in: and the cloud filled the inner court.
4 Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo.
Then the glory of the Lord rose upward from the cherub, toward the threshold of the house: and the house was filled with the cloud, and the court was full of the brightness of the Lord's glory.
5 Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.
And the sound of the wings of the cherubim was heard as far as the outer court, like the voice of the Almighty God when he speaketh.
6 Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi.
And it came to pass, when he commanded the man clothed in linen, saying, Take fire from between the wheels, from between the cherubim, that he went in, and stood beside the wheel.
7 Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka.
And the one cherub stretched forth his hand from between the cherubim unto the fire that was between the cherubim, and lifted it up, and placed it into the hands of the one clothed in linen; who took it, and went out.
8 Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.
And there became visible on the cherubim the form of a man's hand beneath their wings.
9 Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti.
And I saw, and, behold, there were four wheels by the cherubim, one wheel by the one cherub, and another wheel by the other cherub: and the appearance of the wheels was like the glitter of a chrysolite stone.
10 Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake.
And as for their appearances, the whole four had one likeness, as if a wheel were in the midst of another wheel.
11 Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka.
In their going, they went toward their four sides, they turned not round in their going; but to the place whither the head was turned they followed it, they turned not round in their going.
12 Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija.
And their whole body, and their back, and their hands, and their wings, as also the wheels, were full of eyes round about, [even] the wheels that belonged to all four of them.
13 Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.”
As for the wheels, they were called Galgal before my ears.
14 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.
And every one had four faces: the one face was the face of a cherub, and the second face was the face of a man, and the third face was the face of a lion, and the fourth the face of an eagle.
15 Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara.
And the cherubim lifted themselves up. This is the living creature that I saw by the river Kebar.
16 Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo.
And when the cherubim went forward, the wheels went close by them; and when the cherubim lifted up their wings to mount up from the earth, the wheels also did not turn away from beside them.
17 Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.
When those halted, these halted; and when those lifted themselves up, these lifted themselves up with them; for the spirit of the living creature was in them.
18 Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi.
And the glory of the Lord went forth from off the threshold of the house, and halted over the cherubim.
19 Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
And the cherubim lifted up their wings, and mounted up from the earth before my eyes as they went forth, and the wheels at the same time with them, and halted at the entrance of the east gate of the house of the Lord: and the glory of the God of Israel was over them above.
20 Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi.
This is the living creature that I saw under the God of Israel by the river Kebar; and I understood that they were cherubim.
21 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu.
Every one had four faces apiece, and every one had four wings; and the likeness of the hands of a man was under their wings.
22 Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.
And the likeness of their faces was the same as the faces which I had seen by the river Kebar, their appearances and themselves: they went every one in the direction of his face.

< Ezekieli 10 >