< Ezekieli 10 >
1 Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro.
And saw and behold in the firmament that was over the heads of the cherubims, there appeared over them as it were the sapphire stone, as the appearance of the likeness of a throne.
2 Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.
And he spoke to the man, that was clothed with linen, and said: Go in between the wheels that are under the cherubims and fill thy hand with the coals of fire that are between the cherubims, and pour them out upon the city. And he went in, in my sight:
3 Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati.
And the cherubims stood on the right side of the house, when the man went in, and a cloud filled the inner court.
4 Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo.
And the glory of the Lord was lifted up from above the cherub to the threshold of the house: and the house was filled with the cloud, and the court was filled with the brightness of the glory of the Lord.
5 Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.
And the sound of the wings of the cherubims was heard even to the outward court as the voice of God Almighty speaking.
6 Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi.
And when he had commanded the man that was clothed with linen, saying: Take fire from the midst of the wheels that are between the cherubims: he went in and stood beside the wheel,
7 Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka.
And one cherub stretched out his arm from the midst of the cherubims to the fire that was between the cherubims: and he took, and put it into the hands of him that was clothed with linen: who took it and went forth.
8 Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.
And there appeared in the cherubims the likeness of a man’s hand under their wings.
9 Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti.
And I saw, and behold there were four wheels by the cherubims: one wheel by one cherub, and another wheel by another cherub: and the appearance of the wheels was to the sight like the chrysolite stone:
10 Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake.
And as to their appearance, all four were alike: as if a wheel were in the midst of a wheel.
11 Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka.
And when they went, they went by four ways: and they turned not when they went: but to the place whither they first turned, the rest also followed, and did not turn back.
12 Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija.
And their whole body, and their necks, and their hands, and their wings, and the circles were full of eyes, round about the four wheels.
13 Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.”
And these wheels he called voluble, in my hearing.
14 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.
And every one had four faces: one face was the face of a cherub, and the second face, the face of a man: and in the third was the face of a lion: and in the fourth the face of an eagle.
15 Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara.
And the cherubims were lifted up: this is the living creature that I had seen by the river Chobar.
16 Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo.
And when the cherubims went, the wheels also went by them: and when the cherubims lifted up their wings, to mount up from the earth, the wheels stayed not behind, but were by them.
17 Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.
When they stood, these stood: and when they were lifted up, these were lifted up: for the spirit of life was in them.
18 Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi.
And the glory of the Lord went forth from the threshold of the temple: and stood over the cherubims.
19 Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
And the cherubims lifting up their wings, were raised from the earth before me: and as they went out, the wheels also followed: and it stood in the entry of the east gate of the house of the Lord: and the glory of the God of Israel was over them.
20 Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi.
This is the living creature, which I saw under the God of Israel by the river Chobar: and I understood that they were cherubims.
21 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu.
Each one had four faces, and each one had four wings: and the likeness of a man’s hand was under their wings.
22 Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.
And as to the likeness of their faces, they were the same faces which I had seen by the river Chobar, and their looks, and the impulse of every one to go straight forward.