< Eksodo 1 >
1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
Dette er Navnene paa Israels Sønner, der sammen med Jakob kom til Ægypten med deres Familier:
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Ruben, Simeon, Levi og Juda,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Issakar, Zebulon og Benjamin,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Dan og Naftali, Gad og Aser.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
Jakobs Efterkommere udgjorde i alt halvfjerdsindstyve, men Josef var i Ægypten.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
Imidlertid døde Josef og alle hans Brødre og hele dette Slægtled.
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
Men Israeliterne var frugtbare og formerede sig, og de blev mange og overmaade talrige, saa at Landet blev fuldt af dem.
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Da kom der en ny Konge over Ægypten, som ikke vidste noget om Josef;
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
og han sagde til sit Folk: »Se, Israels Folk bliver talrigere og stærkere end vi.
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
Velan, lad os gaa klogt til Værks imod dem, for at de ikke skal blive for mange; ellers kan det hænde, naar vi kommer i Krig, at de gaar over til vore Modstandere og kæmper mod os og til sidst forlader Landet!«
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
Saa satte man Fogeder over dem til at plage dem med Trællearbejde, og de maatte bygge Forraadsbyer for Farao: Pitom og Ra'amses.
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
Men jo mere man plagede dem, des flere blev de, og des mere bredte de sig, saa Ægypterne fik Rædsel for Israeliterne.
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
Og Ægypterne tvang Israeliterne til Trællearbejde
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
og gjorde dem Livet bittert ved haardt Arbejde med Ler og Tegl og alle Haande Markarbejde, ved alt det Arbejde, de tvang dem til at udføre for sig.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
Ægypterkongen sagde da til Hebræerkvindernes Jordemødre, af hvilke den ene hed Sjifra, den anden Pua:
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
»Naar I forløser Hebræerkvinderne, skal I se godt efter ved Fødselen, og er det et Drengebarn, tag saa Livet af det, men er det et Pigebarn, lad det saa leve!«
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
Men Jordemødrene frygtede Gud og gjorde ikke, som Ægypterkongen havde befalet dem, men lod Drengebørnene leve.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
Da lod Ægypterkongen Jordemødrene kalde og sagde til dem: »Hvorfor har I baaret eder saaledes ad og ladet Drengebørnene leve?«
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
Men Jordemødrene svarede Farao: »Hebræerkvinderne er ikke som de Ægyptiske Kvinder, de har let ved at føde; inden Jordemoderen kommer til dem, har de allerede født!«
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
Og Gud gjorde vel imod Jordemødrene, og Folket blev stort og saare talrigt;
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
og Gud gav Jordemødrene Afkom, fordi de frygtede ham.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
Da udstedte Farao den Befaling til hele sit Folk: »Alle Drengebørn, der fødes, skal I kaste i Nilen, men Pigebørnene skal I lade leve!«