< Eksodo 1 >

1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
Og disse ere Navnene paa Israels Sønner, som kom til Ægypten, med Jakob kom de, hver med sit Hus:
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Ruben, Simeon, Levi og Juda,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Isaskar, Sebulon og Benjamin,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Dan og Nafthali, Gad og Aser.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
Og alle Personer, som vare udkomne af Jakobs Lænd, de vare halvfjerdsindstyve Personer; men Josef var i Ægypten.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
Og Josef døde, og alle hans Brødre og al denne Slægt.
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
Og Israels Børn bleve frugtbare og vrimlede og bleve mangfoldige og vare saare talrige, og Landet blev fuldt af dem.
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Og der kom en ny Konge over Ægypten, som ikke kendte Josef.
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
Og han sagde til sit Folk: Se, Israels Børns Folk ere flere og talrigere end vi.
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
Velan, vi ville handle klogeligen imod det, at det ikke skal blive mangfoldigt; og det kunde ske, om der blev Lejlighed til en Krig, kunde det ogsaa slaa sig til vore Fjender og føre Krig imod os og drage ud af Landet.
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
Saa satte de Skattebetjente over det, at de skulde plage det med deres Byrder; og man byggede Farao Forraadsstæder, nemlig Pithom og Raamses.
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
Og jo mere de plagede det, desto mere blev det mangfoldigt, og udbredte sig, og de væmmedes ved Israels Børn.
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
Og Ægypterne tvang Israels Børn til at trælle strengt.
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
Og de gjorde dem deres Liv besk med haard Trældom i Ler og i Tegl og med alle Haande Trældom paa Marken; i al deres Trældom, i hvilken de tjente dem, maatte de trælle strengt.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
Og Kongen af Ægypten talede til de hebraiske Jordemødre, af hvilke den enes Navn var Sifra og den andens Navn Pua,
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
og han sagde: Naar I hjælpe de hebraiske Kvinder ved Fødselen, saa ser paa Stolene: Dersom det er en Søn, saa dræber ham, og dersom det er en Datter, da maa hun leve.
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
Men Jordemødrene frygtede Gud og gjorde ikke saa, som Kongen af Ægypten havde talet til dem, men lode Drengene leve.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
Da kaldte Kongen af Ægypten Jordemødrene og sagde til dem: Hvi gjorde I denne Gerning, at I lode Drengene leve?
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
Og Jordemødrene svarede Farao: De hebraiske ere ikke som de ægyptiske Kvinder, men de ere stærke; førend Jordemoderen kommer til dem, da have de født.
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
Derfor gjorde Gud vel imod Jordemødrene, og Folket blev mangfoldigt, og de bleve saare talrige.
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
Og det skete, efterdi Jordemødrene frygtede Gud, da lod han dem faa Huse.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
Saa bød Farao alt sit Folk og sagde: Hver en Søn, som fødes, kaster ham i Floden, og lader alle Døtre leve.

< Eksodo 1 >