< Eksodo 9 >
1 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
Alors l'Éternel dit à Moïse: Va vers Pharaon, et dis-lui: Ainsi a dit l'Éternel, le Dieu des Hébreux: Laisse aller mon peuple, afin qu'il me serve;
2 Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
Car si tu refuses de les laisser aller, et si tu les retiens encore,
3 dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
Voici, la main de l'Éternel sera sur ton bétail qui est aux champs, sur les chevaux, sur les ânes, sur les chameaux, sur les bœufs et sur les brebis: il y aura une très grande mortalité.
4 Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
Et l'Éternel distinguera entre le bétail d'Israël et le bétail des Égyptiens, et rien de tout ce qui est aux enfants d'Israël ne mourra.
5 Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
Et l'Éternel fixa le terme, en disant: Demain l'Éternel fera cela dans le pays.
6 Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
L'Éternel fit donc cela dès le lendemain, et tout le bétail des Égyptiens mourut; mais du bétail des enfants d'Israël il ne mourut pas une seule bête.
7 Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
Et Pharaon envoya voir, et voici, il n'était pas mort une seule bête du bétail d'Israël. Mais le cœur de Pharaon s'appesantit, et il ne laissa point aller le peuple.
8 Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
Alors l'Éternel dit à Moïse et à Aaron: Prenez plein vos mains de cendre de fournaise, et que Moïse la répande vers les cieux, sous les yeux de Pharaon.
9 Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
Et elle deviendra de la poussière sur tout le pays d'Égypte, et elle deviendra, sur les hommes et sur les bêtes, des ulcères bourgeonnant en pustules, dans tout le pays d'Égypte.
10 Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
Ils prirent donc de la cendre de fournaise, et se tinrent devant Pharaon; et Moïse la répandit vers les cieux, et elle devint, sur les hommes et sur les bêtes, des ulcères bourgeonnant en pustules.
11 Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
Et les magiciens ne purent se tenir devant Moïse, à cause des ulcères; car les ulcères étaient sur les magiciens comme sur tous les Égyptiens.
12 Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
Et l'Éternel endurcit le cœur de Pharaon, et il ne les écouta point, comme l'Éternel l'avait dit à Moïse.
13 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
Puis, l'Éternel dit à Moïse: Lève-toi de bon matin, présente-toi devant Pharaon, et dis-lui: Ainsi a dit l'Éternel, le Dieu des Hébreux: Laisse aller mon peuple, afin qu'il me serve;
14 Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
Car cette fois, je vais envoyer toutes mes plaies contre ton cœur, et sur tes serviteurs et sur ton peuple, afin que tu saches que nul n'est semblable à moi sur toute la terre.
15 Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
Car maintenant, si j'avais étendu ma main, et si je t'avais frappé par la mortalité, toi et ton peuple, tu serais effacé de la terre.
16 Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
Mais voici pourquoi je t'ai fait subsister: c'est afin que tu fasses voir ma puissance, et pour que mon nom soit célébré par toute la terre.
17 Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
Si tu t'élèves encore contre mon peuple, pour ne point le laisser aller,
18 Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
Voici je vais faire pleuvoir demain, à cette heure, une si forte grêle, qu'il n'y en a point eu de semblable en Égypte, depuis le jour où elle fut fondée jusqu'à présent.
19 Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
Maintenant donc, envoie mettre en sûreté ton bétail, et tout ce que tu as aux champs. La grêle tombera sur tous les hommes et les bêtes qui se trouveront aux champs, et qui ne se retireront pas dans les maisons, et ils mourront.
20 Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
Celui des serviteurs de Pharaon qui craignit la parole de l'Éternel, fit promptement retirer dans les maisons ses serviteurs et son bétail.
21 Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
Mais celui qui ne fit point attention à la parole de l'Éternel, laissa ses serviteurs et son bétail aux champs.
22 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
Alors l'Éternel dit à Moïse: Étends ta main vers les cieux, et qu'il y ait de la grêle sur tout le pays d'Égypte, sur les hommes, et sur les bêtes, et sur toute herbe des champs dans le pays d'Égypte.
23 Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
Moïse étendit donc sa verge vers les cieux, et l'Éternel fit tonner et grêler, et le feu se promenait sur la terre. Et l'Éternel fit pleuvoir de la grêle sur le pays d'Égypte.
24 Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
Et il y eut de la grêle, et un feu continu au milieu de la grêle, qui était si prodigieuse, qu'il n'y en avait point eu de semblable dans tout le pays d'Égypte, depuis qu'il était devenu une nation.
25 Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
Et la grêle frappa dans tout le pays d'Égypte tout ce qui était aux champs, depuis les hommes jusqu'aux bêtes. La grêle frappa aussi toutes les herbes des champs et brisa tous les arbres des champs.
26 Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
Le pays de Gossen, où étaient les enfants d'Israël, fut le seul où il n'y eut point de grêle.
27 Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
Alors Pharaon envoya appeler Moïse et Aaron, et leur dit: J'ai péché cette fois; l'Éternel est le juste, et moi et mon peuple nous sommes les coupables.
28 Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
Intercédez auprès de l'Éternel; et qu'il n'y ait plus de tonnerres ni de grêle; et je vous laisserai aller, et vous ne resterez pas plus longtemps.
29 Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
Alors Moïse lui dit: Dès que je serai sorti de la ville, j'étendrai mes mains vers l'Éternel, les tonnerres cesseront, et il n'y aura plus de grêle, afin que tu saches que la terre est à l'Éternel.
30 Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
Mais, pour toi et tes serviteurs, je sais que vous ne craindrez pas encore l'Éternel Dieu.
31 Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
Or, le lin et l'orge furent frappés; car l'orge était en épis, et le lin en fleur.
32 Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
Mais le blé et l'épeautre ne furent point frappés, parce qu'ils sont tardifs.
33 Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
Moïse quitta donc Pharaon, sortit de la ville, et étendit ses mains vers l'Éternel; et les tonnerres et la grêle cessèrent, et la pluie ne se répandit plus sur la terre.
34 Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
Et Pharaon, voyant que la pluie, la grêle et les tonnerres avaient cessé, continua encore de pécher; et il appesantit son cœur, lui et ses serviteurs.
35 Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
Le cœur de Pharaon s'endurcit donc, et il ne laissa point aller les enfants d'Israël, comme l'Éternel l'avait dit par l'organe de Moïse.