< Eksodo 8 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: ej pie Faraona un saki tam: tā saka Tas Kungs: atlaid Manus ļaudis, ka tie Man kalpo;
2 Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
Un ja tu liegsies, tos atlaist, redzi, tad Es visas tavas robežas sitīšu ar vardēm,
3 Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
Ka upe kustin kustēs ar vardēm, un tās celsies un nāks tavā namā un tavā guļamā kambarī un uz tavu gultu un tavu kalpu namos un pār taviem ļaudīm un tavos cepļos un tavās abrās.
4 Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
Un vardes nāks uz tevi un uz taviem ļaudīm un uz taviem kalpiem.
5 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: saki Āronam: izstiep savu roku ar savu zizli pār strautiem, pār upēm un pār ezeriem, un liec vardēm nākt pār Ēģiptes zemi.
6 Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
Un Ārons izstiepa savu roku pār Ēģiptes ūdeņiem, tad nāca vardes un apklāja Ēģiptes zemi
7 Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
Un tie burvji darīja arīdzan tā ar savu buršanu un lika vardēm nākt pār Ēģiptes zemi.
8 Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
Tad Faraons aicināja Mozu un Āronu un sacīja: lūdziet To Kungu, ka Viņš tās vardes atņemtu no manis un no maniem ļaudīm; tad es tos ļaudis atlaidīšu, upurēt Tam Kungam.
9 Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
Bet Mozus sacīja uz Faraonu: saki man jel, kad man būs lūgt tevis dēļ un tavu kalpu un tavu ļaužu labad, lai tās vardes tiek izdeldētas, ka vairs nav pie tevis nedz tavā namā, bet paliek upē vien?
10 Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
Un viņš sacīja: rītu. Un tas sacīja: lai ir pēc tava vārda; lai tu atzīsti, ka neviens nav kā Tas Kungs, mūsu Dievs.
11 Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
Tām vardēm būs atstāties no tevis un no tava nama un no taviem kalpiem un no taviem ļaudīm; upē vien tām būs palikt.
12 Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
Tad Mozus un Ārons aizgāja no Faraona, un Mozus sauca uz To Kungu to varžu dēļ, kā viņš Faraonam bija apsolījis.
13 Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
Un Tas Kungs darīja pēc Mozus vārda, un tās vardes nomira namos, sētās un uz laukiem.
14 Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
Un tie tās meta kopās, un zeme smirdēja.
15 Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
Kad nu Faraons redzēja, ka bija dabūjis atvieglināšanu, tad viņš apcietināja savu sirdi un tiem neklausīja, kā Tas Kungs bija sacījis.
16 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: saki Āronam: izstiep savu zizli un sit zemes pīšļus, lai top par utīm pa visu Ēģiptes zemi, un tie tā darīja.
17 Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
Jo Ārons izstiepa savu roku ar savu zizli un sita zemes pīšļus, un utis radās pie cilvēkiem un pie lopiem; - visi zemes pīšļi palika par utīm pa visu Ēģiptes zemi.
18 Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
Tad tie burvji darbojās arī tā ar savu buršanu, likt utīm nākt; bet tie nevarēja. Tā bija utis pie cilvēkiem un pie lopiem.
19 Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
Tad tie burvji sacīja uz Faraonu: šis ir Dieva pirksts. Tomēr Faraona sirds apcietinājās, un viņš tiem neklausīja, tā kā Tas Kungs bija sacījis.
20 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
Tad Tas Kungs sacīja uz Mozu: celies rīt agri un stājies Faraona priekšā: redzi, viņš izies pie ūdens, - un runā uz to: tā saka Tas Kungs: atlaid Manus ļaudis, lai tie Man kalpo.
21 Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
Bet ja tu Manus ļaudis neatlaidīsi, tad Es sūtīšu visādus kukaiņus pār tevi un pār taviem kalpiem un pār taviem ļaudīm un tavos namos, un visādiem kukaiņiem būs piepildīt ēģiptiešu namus un to zemi, kur tie ir.
22 “Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
Un tanī dienā Es izšķiršu Gošenes zemi, kur Mani ļaudis dzīvo, ka tur nebūs kukaiņiem būt, lai tu atzīsti, ka Es Tas Kungs esmu pa visu zemi.
23 Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
Un Es darīšu starpību starp Maniem ļaudīm un taviem ļaudīm; rīt šai zīmei būs notikt.
24 Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
Un Tas Kungs darīja tā, un kukaiņi nāca bariem Faraona namā un viņa kalpu namos un pa visu Ēģiptes zemi, un zeme tapa maitāta no kukaiņiem.
25 Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
Tad Faraons aicināja Mozu un Āronu un sacīja: ejat un upurējat savam Dievam šinī zemē.
26 Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
Bet Mozus sacīja: tā nevar darīt; jo, kas ēģiptiešiem negantība, to mēs upurētu Tam Kungam, savam Dievam. Redzi, ja tad mēs, kas ēģiptiešiem negantība, upurētu viņu priekšā, vai tie mūs ar akmeņiem nenomētātu?
27 Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
Mēs iesim kādu treju dienu gājumu tuksnesī un upurēsim Tam Kungam, savam Dievam, kā Viņš mums ir sacījis.
28 Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
Tad Faraons sacīja: es jūs atlaidīšu, upurēt Tam Kungam, savam Dievam; tikai neaizejiet visai tālu, - lūdziet par mani.
29 Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
Tad Mozus sacīja: redzi, es aizeju no tevis un lūgšu To Kungu, ka šiem kukaiņiem rītu būs atstāties no Faraona un no viņa kalpiem un no viņa ļaudīm; tikai Faraonam nebūs vairs mani pievilt, neatlaižot tos ļaudis, upurēt Tam Kungam.
30 Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
Tad Mozus aizgāja no Faraona un lūdza To Kungu.
31 Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
Un Tas Kungs darīja pēc Mozus vārda, un tie kukaiņi atstājās no Faraona, no viņa kalpiem un no viņa tautas, ka tur neviens nepalika.
32 Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.
Tomēr Faraons arī šo reiz apcietināja savu sirdi un neatlaida tos ļaudis.

< Eksodo 8 >