< Eksodo 8 >
1 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
Yahweh dit à Moïse: « Va vers Pharaon, et tu lui diras: Ainsi dit Yahweh: Laisse aller mon peuple, afin qu’il me serve.
2 Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
Si tu refuses de le laisser aller, voici que je vais frapper du fléau des grenouilles toute l’étendue de ton pays.
3 Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
Le fleuve fourmillera de grenouilles; elles monteront et entreront dans ta maison, dans ta chambre à coucher et sur ton lit, dans la maison de tes serviteurs, et au milieu de ton peuple, dans tes fours et dans tes pétrins;
4 Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
sur toi, sur ton peuple et sur tous tes serviteurs les grenouilles monteront. »
5 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
Yahweh dit à Moïse: « Dis à Aaron: étends ta main avec ton bâton sur les rivières, sur les canaux et sur les étangs, et fais monter les grenouilles sur le pays d’Égypte. »
6 Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
Aaron étendit sa main sur les eaux de l’Égypte, et les grenouilles montèrent et couvrirent le pays d’Égypte.
7 Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
Mais les magiciens firent la même chose par leurs enchantements; ils firent monter les grenouilles sur le pays d’Égypte.
8 Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
Pharaon appela Moïse et Aaron, et leur dit: « Priez Yahweh afin qu’il éloigne les grenouilles de moi et de mon peuple, et je laisserai aller le peuple, pour qu’il offre des sacrifices à Yahweh. »
9 Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
Moïse dit à Pharaon: « Donne-moi tes ordres! Pour quand dois-je faire des prières en ta faveur, en faveur de tes serviteurs et de ton peuple, afin que Yahweh éloigne les grenouilles de toi et de tes maisons, de manière à ce qu’il n’en reste plus que dans le fleuve? »
10 Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
Il répondit: « Pour demain ». Et Moïse dit: « Il en sera ainsi, afin que tu saches que nul n’est pareil à Yahweh, notre Dieu.
11 Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
Les grenouilles se retireront de toi et de tes maisons, de tes serviteurs et de ton peuple; il n’en restera que dans le fleuve. »
12 Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
Moïse et Aaron sortirent de chez Pharaon, et Moïse cria vers Yahweh au sujet des grenouilles dont il avait affligé Pharaon.
13 Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
Yahweh fit selon la parole de Moïse, et les grenouilles moururent dans les maisons, dans les cours et dans les champs.
14 Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
On les entassa en monceaux, et le pays en fut infecté.
15 Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
Mais Pharaon, voyant qu’on respirait, endurcit son cœur, et il n’écouta pas Moïse et Aaron, selon que Yahweh l’avait dit.
16 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
Yahweh dit à Moïse: « Dis à Aaron: Etends ton bâton et frappe la poussière de la terre, et elle se changera en moustiques dans tout le pays d’Égypte. »
17 Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
Ils firent ainsi; Aaron étendit sa main avec son bâton et frappa la poussière de la terre, et les moustiques furent sur les hommes et sur les animaux. Toute la poussière de la terre fut changée en moustiques, dans tout le pays d’Égypte.
18 Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
Les magiciens firent de même avec leurs enchantements, afin de produire des moustiques; mais ils ne le purent pas. Les moustiques étaient sur les hommes et sur les animaux.
19 Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
Et les magiciens dirent à Pharaon: « C’est le doigt d’un dieu! » Et le cœur de Pharaon s’endurcit, et il ne les écouta pas, selon que Yahweh l’avait dit.
20 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
Yahweh dit à Moïse: « Lève-toi de bon matin et présente-toi devant Pharaon, au moment où il sort pour aller au bord de l’eau. Tu lui diras: Ainsi parle Yahweh: Laisse aller mon peuple afin qu’il me serve.
21 Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
Si tu ne laisses pas aller mon peuple, je vais envoyer des scarabées contre toi, contre tes serviteurs, contre ton peuple et contre tes maisons; les maisons des Égyptiens seront remplies de scarabées, ainsi que la terre qu’ils habitent.
22 “Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
Mais je distinguerai, ce jour-là, le pays de Gessen, où mon peuple habite, et là il n’y aura pas de scarabées, afin que tu saches que moi, Yahweh, je suis au milieu de cette terre.
23 Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
J’établirai ainsi une différence entre mon peuple et ton peuple; c’est demain que ce signe aura lieu. »
24 Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
Yahweh fit ainsi; il vint une multitude de scarabées dans la maison de Pharaon et de ses serviteurs, et tout le pays d’Égypte fut ravagé par les scarabées.
25 Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
Pharaon appela Moïse et Aaron, et leur dit: « Allez, offrez des sacrifices à votre Dieu dans ce pays. »
26 Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
Moïse répondit: « Il ne convient pas de faire ainsi, car c’est une abomination pour les Égyptiens que les sacrifices que nous offrons à Yahweh, notre Dieu; et si nous offrons, sous les yeux des Égyptiens, des sacrifices qui sont pour eux des abominations, ne nous lapideront-ils pas?
27 Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
Nous irons à trois journées de marche dans le désert pour offrir des sacrifices à Yahweh, notre Dieu, selon qu’il nous le dira. »
28 Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
Pharaon dit: « Pour moi, je vous laisserai aller, pour offrir des sacrifices à Yahweh, votre Dieu, dans le désert; seulement ne vous éloignez pas trop dans votre marche. Faites des prières pour moi. »
29 Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
Moïse répondit: Voici, je vais sortir de chez toi, et je prierai Yahweh, et demain les scarabées se retireront de Pharaon, de ses serviteurs et de son peuple. Mais que Pharaon ne trompe plus, en ne permettant pas au peuple d’aller offrir des sacrifices à Yahweh! »
30 Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
Moïse sortit de chez Pharaon et pria Yahweh.
31 Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
Et Yahweh fit selon la parole de Moïse, et les scarabées s’éloignèrent de Pharaon, de ses serviteurs et de son peuple; il n’en resta pas un seul.
32 Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.
Mais Pharaon endurcit son cœur cette fois encore, et il ne laissa pas aller le peuple.