< Eksodo 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Taona ine ndakuyika kuti ukhale ngati Mulungu kwa Farao, ndipo mʼbale wako Aaroni adzakhala mneneri wako.
and to say LORD to(wards) Moses to see: behold! to give: make you God to/for Pharaoh and Aaron brother: male-sibling your to be prophet your
2 Iwe ukanene zonse zimene ndakulamulirazi, ndipo Aaroni mʼbale wako ndiye akaziyankhule kwa Farao kuti atulutse ana a Israeli mʼdziko la Igupto.
you(m. s.) to speak: speak [obj] all which to command you and Aaron brother: male-sibling your to speak: speak to(wards) Pharaoh and to send: let go [obj] son: descendant/people Israel from land: country/planet his
3 Koma ndidzawumitsa mtima wa Farao, ndipo ngakhale nditachulukitsa zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa mu Igupto,
and I to harden [obj] heart Pharaoh and to multiply [obj] sign: miraculous my and [obj] wonder my in/on/with land: country/planet Egypt
4 iyeyo sadzakumverani. Choncho ndidzakantha Igupto, ndipo ndi ntchito zachiweruzo ndidzatulutsa magulu anga, anthu anga Aisraeli kuwachotsa mʼdziko la Igupto.
and not to hear: hear to(wards) you Pharaoh and to give: put [obj] hand my in/on/with Egypt and to come out: send [obj] army my [obj] people my son: descendant/people Israel from land: country/planet Egypt in/on/with judgment great: large
5 Ndipo Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzatambasula dzanja langa kukantha Igupto ndi kutulutsa Aisraeli mʼdzikomo.”
and to know Egyptian for I LORD in/on/with to stretch I [obj] hand my upon Egypt and to come out: send [obj] son: descendant/people Israel from midst their
6 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova anawalamulira.
and to make: do Moses and Aaron like/as as which to command LORD [obj] them so to make: do
7 Mose anali ndi zaka 80, ndipo Aaroni anali ndi zaka 83 pamene anakayankhula kwa Farao.
and Moses son: aged eighty year and Aaron son: aged three and eighty year in/on/with to speak: speak they to(wards) Pharaoh
8 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
and to say LORD to(wards) Moses and to(wards) Aaron to/for to say
9 “Ngati Farao adzati kwa inu, ‘Chitani chozizwitsa,’ iwe Mose udzati kwa Aaroni, ‘Tenga ndodo yako ndipo uyiponye pamaso pa Farao,’ ndipo idzasanduka njoka.”
for to speak: speak to(wards) you Pharaoh to/for to say to give: make to/for you wonder and to say to(wards) Aaron to take: take [obj] tribe: rod your and to throw to/for face: before Pharaoh to be to/for serpent: snake
10 Kotero Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kuchita monga momwe Yehova anawalamulira. Aaroni anaponya ndodo yake pansi patsogolo pa Farao ndi nduna zake ndipo inasanduka njoka.
and to come (in): come Moses and Aaron to(wards) Pharaoh and to make: do so like/as as which to command LORD and to throw Aaron [obj] tribe: rod his to/for face: before Pharaoh and to/for face: before servant/slave his and to be to/for serpent: snake
11 Naye Farao anayitanitsa anthu ake anzeru ndi amatsenga, ndipo nawonso amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo.
and to call: call to also Pharaoh to/for wise and to/for to practice sorcery and to make: do also they(masc.) magician Egypt in/on/with secret their so
12 Aliyense wa iwo anaponya ndodo yake pansi ndipo inasanduka njoka. Koma ndodo ya Aaroni inameza ndodo zawo.
and to throw man: anyone tribe: rod his and to be to/for serpent: snake and to swallow up tribe: rod Aaron [obj] tribe: rod their
13 Koma mtima wa Farao unawuma ndipo sanawamvere monga momwe Yehova ananenera.
and to strengthen: strengthen heart Pharaoh and not to hear: hear to(wards) them like/as as which to speak: speak LORD
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Farao ndi wowuma mtima. Akukana kulola anthu anga kuti apite.
and to say LORD to(wards) Moses heavy heart Pharaoh to refuse to/for to send: let go [the] people
15 Upite kwa Farao mmawa pamene azidzapita ku madzi. Ukamudikire mʼmbali mwa Nailo kuti ukakumane naye ndipo unyamule ndodo imene inasanduka njoka ija mʼdzanja lako.
to go: went to(wards) Pharaoh in/on/with morning behold to come out: come [the] water [to] and to stand to/for to encounter: meet him upon lip: shore [the] Nile and [the] tribe: rod which to overturn to/for serpent to take: take in/on/with hand your
16 Ndipo ukamuwuze Farao kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri wandituma kuti ndikuwuzeni kuti: Lolani anthu anga apite kuti akandipembedze mʼchipululu. Koma mpaka tsopano inu simunandimvere.
and to say to(wards) him LORD God [the] Hebrew to send: depart me to(wards) you to/for to say to send: let go [obj] people my and to serve: minister me in/on/with wilderness and behold not to hear: obey till thus
17 Izi ndi zimene Yehova akunena: Ndi ndodo imene ili mʼdzanja langa ndidzamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi adzasanduka magazi. Ndikadzachita ichi udzadziwa kuti Ine ndine Yehova:
thus to say LORD in/on/with this to know for I LORD behold I to smite in/on/with tribe: rod which in/on/with hand my upon [the] water which in/on/with Nile and to overturn to/for blood
18 Nsomba za mu Nailo zidzafa, mtsinje udzanunkha ndipo Aigupto sadzatha kumwa madzi ake.’”
and [the] fish which in/on/with Nile to die and to stink [the] Nile and be weary Egyptian to/for to drink water from [the] Nile
19 Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Tenga ndodo yako uyilozetse ku madzi a mu Igupto pa mitsinje, pa ngalande, pa zithaphwi ndi pa madambo, ndipo onse adzasanduka magazi.’ Mʼdziko lonse la Igupto mudzakhala magazi, ngakhale mʼzotungira madzi zopangidwa ndi mitengo ndi miyala.”
and to say LORD to(wards) Moses to say to(wards) Aaron to take: take tribe: rod your and to stretch hand your upon water Egypt upon river their upon Nile their and upon pool their and upon all collection water their and to be blood and to be blood in/on/with all land: country/planet Egypt and in/on/with tree: wood and in/on/with stone
20 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova analamulira. Anakweza ndodo yake pamaso pa Farao ndi akuluakulu ake ndipo anamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi onse anasanduka magazi.
and to make: do so Moses and Aaron like/as as which to command LORD and to exalt in/on/with tribe: rod and to smite [obj] [the] water which in/on/with Nile to/for eye: seeing Pharaoh and to/for eye: seeing servant/slave his and to overturn all [the] water which in/on/with Nile to/for blood
21 Nsomba za mu Nailo zinafa ndipo mtsinje unanunkha kwambiri kotero kuti Aigupto sanathe kumwa madzi ake. Magazi anali ponseponse mu Igupto.
and [the] fish which in/on/with Nile to die and to stink [the] Nile and not be able Egyptian to/for to drink water from [the] Nile and to be [the] blood in/on/with all land: country/planet Egypt
22 Koma amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo. Choncho Farao anawumabe mtima, ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananeneratu.
and to make: do so magician Egypt in/on/with secrecy their and to strengthen: strengthen heart Pharaoh and not to hear: hear to(wards) them like/as as which to speak: speak LORD
23 Mʼmalo mwake iye anatembenuka ndi kupita ku nyumba yake yaufumu ndipo zimenezi sanazilabadire.
and to turn Pharaoh and to come (in): come to(wards) house: home his and not to set: consider heart his also to/for this
24 Anthu onse a ku Igupto anayamba kukumba mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo kuti apeze madzi akumwa, chifukwa sanathe kumwa madzi a mu mtsinjemo.
and to search all Egyptian around: side [the] Nile water to/for to drink for not be able to/for to drink from water [the] Nile
25 Panapita masiku asanu ndi awiri Yehova atamenya madzi a mu mtsinje wa Nailo.
and to fill seven day after to smite LORD [obj] [the] Nile

< Eksodo 7 >