< Eksodo 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Taona ine ndakuyika kuti ukhale ngati Mulungu kwa Farao, ndipo mʼbale wako Aaroni adzakhala mneneri wako.
And Jehovah said to Moses, See, I have made thee God to Pharaoh; and Aaron thy brother shall be thy prophet.
2 Iwe ukanene zonse zimene ndakulamulirazi, ndipo Aaroni mʼbale wako ndiye akaziyankhule kwa Farao kuti atulutse ana a Israeli mʼdziko la Igupto.
Thou shalt speak all that I command thee; and Aaron thy brother shall speak unto Pharaoh, that he let the children of Israel go out of his land.
3 Koma ndidzawumitsa mtima wa Farao, ndipo ngakhale nditachulukitsa zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa mu Igupto,
And I will render Pharaoh's heart obdurate, and multiply my signs and my wonders in the land of Egypt.
4 iyeyo sadzakumverani. Choncho ndidzakantha Igupto, ndipo ndi ntchito zachiweruzo ndidzatulutsa magulu anga, anthu anga Aisraeli kuwachotsa mʼdziko la Igupto.
And Pharaoh will not hearken unto you; and I will lay my hand upon Egypt, and bring forth my hosts, my people, the children of Israel, out of the land of Egypt by great judgments.
5 Ndipo Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzatambasula dzanja langa kukantha Igupto ndi kutulutsa Aisraeli mʼdzikomo.”
And the Egyptians shall know that I am Jehovah, when I stretch forth my hand on Egypt, and bring out the children of Israel from among them.
6 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova anawalamulira.
And Moses and Aaron did as Jehovah had commanded them: so did they.
7 Mose anali ndi zaka 80, ndipo Aaroni anali ndi zaka 83 pamene anakayankhula kwa Farao.
And Moses was eighty years old, and Aaron was eighty-three years old, when they spoke to Pharaoh.
8 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
And Jehovah spoke to Moses and to Aaron, saying,
9 “Ngati Farao adzati kwa inu, ‘Chitani chozizwitsa,’ iwe Mose udzati kwa Aaroni, ‘Tenga ndodo yako ndipo uyiponye pamaso pa Farao,’ ndipo idzasanduka njoka.”
When Pharaoh shall speak to you, saying, Do a miracle for yourselves, — then thou shalt say unto Aaron, Take thy staff and cast [it] before Pharaoh — it will become a serpent.
10 Kotero Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kuchita monga momwe Yehova anawalamulira. Aaroni anaponya ndodo yake pansi patsogolo pa Farao ndi nduna zake ndipo inasanduka njoka.
And Moses and Aaron went in to Pharaoh, and did so, as Jehovah had commanded; and Aaron cast down his staff before Pharaoh, and before his bondmen, and it became a serpent.
11 Naye Farao anayitanitsa anthu ake anzeru ndi amatsenga, ndipo nawonso amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo.
And Pharaoh also called the sages and the sorcerers; and they too, the scribes of Egypt, did so with their enchantments:
12 Aliyense wa iwo anaponya ndodo yake pansi ndipo inasanduka njoka. Koma ndodo ya Aaroni inameza ndodo zawo.
they cast down every man his staff, and they became serpents; but Aaron's staff swallowed up their staves.
13 Koma mtima wa Farao unawuma ndipo sanawamvere monga momwe Yehova ananenera.
And Pharaoh's heart was stubborn, and he hearkened not to them, as Jehovah had said.
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Farao ndi wowuma mtima. Akukana kulola anthu anga kuti apite.
And Jehovah said to Moses, Pharaoh's heart is hardened: he refuseth to let the people go.
15 Upite kwa Farao mmawa pamene azidzapita ku madzi. Ukamudikire mʼmbali mwa Nailo kuti ukakumane naye ndipo unyamule ndodo imene inasanduka njoka ija mʼdzanja lako.
Go unto Pharaoh in the morning — behold, he will go out unto the water — and take thy stand by the bank of the river in front of him; and take in thy hand the staff that was turned into a serpent.
16 Ndipo ukamuwuze Farao kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri wandituma kuti ndikuwuzeni kuti: Lolani anthu anga apite kuti akandipembedze mʼchipululu. Koma mpaka tsopano inu simunandimvere.
And say unto him, Jehovah the God of the Hebrews has sent me to thee, saying, Let my people go, that they may serve me in the wilderness; but behold, hitherto thou hast not hearkened.
17 Izi ndi zimene Yehova akunena: Ndi ndodo imene ili mʼdzanja langa ndidzamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi adzasanduka magazi. Ndikadzachita ichi udzadziwa kuti Ine ndine Yehova:
Thus saith Jehovah: In this shalt thou know that I am Jehovah — behold, I will smite with the staff that is in my hand upon the water which is in the river, and it shall be turned into blood.
18 Nsomba za mu Nailo zidzafa, mtsinje udzanunkha ndipo Aigupto sadzatha kumwa madzi ake.’”
And the fish that is in the river shall die; and the river shall stink; and the Egyptians shall loathe to drink the water out of the river.
19 Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Tenga ndodo yako uyilozetse ku madzi a mu Igupto pa mitsinje, pa ngalande, pa zithaphwi ndi pa madambo, ndipo onse adzasanduka magazi.’ Mʼdziko lonse la Igupto mudzakhala magazi, ngakhale mʼzotungira madzi zopangidwa ndi mitengo ndi miyala.”
And Jehovah said to Moses, Say unto Aaron, Take thy staff, and stretch out thy hand upon the waters of the Egyptians — upon their streams, upon their rivers, and upon their ponds, and upon all their reservoirs of water, that they may become blood; and there shall be blood throughout the land of Egypt, both in [vessels of] wood and in [vessels of] stone.
20 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova analamulira. Anakweza ndodo yake pamaso pa Farao ndi akuluakulu ake ndipo anamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi onse anasanduka magazi.
And Moses and Aaron did so, as Jehovah had commanded; and he lifted up the staff, and smote the waters that were in the river before the eyes of Pharaoh, and before the eyes of his bondmen; and all the waters that were in the river were turned into blood.
21 Nsomba za mu Nailo zinafa ndipo mtsinje unanunkha kwambiri kotero kuti Aigupto sanathe kumwa madzi ake. Magazi anali ponseponse mu Igupto.
And the fish that was in the river died; and the river stank, and the Egyptians could not drink the water of the river; and the blood was throughout the land of Egypt.
22 Koma amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo. Choncho Farao anawumabe mtima, ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananeneratu.
And the scribes of Egypt did so with their sorceries; and Pharaoh's heart was stubborn, neither did he hearken to them, as Jehovah had said.
23 Mʼmalo mwake iye anatembenuka ndi kupita ku nyumba yake yaufumu ndipo zimenezi sanazilabadire.
And Pharaoh turned and went into his house, and took not this to heart either.
24 Anthu onse a ku Igupto anayamba kukumba mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo kuti apeze madzi akumwa, chifukwa sanathe kumwa madzi a mu mtsinjemo.
And all the Egyptians dug round about the river for water to drink; for they could not drink of the water of the river.
25 Panapita masiku asanu ndi awiri Yehova atamenya madzi a mu mtsinje wa Nailo.
And seven days were fulfilled, after Jehovah had smitten the river.

< Eksodo 7 >