< Eksodo 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Taona ine ndakuyika kuti ukhale ngati Mulungu kwa Farao, ndipo mʼbale wako Aaroni adzakhala mneneri wako.
Da sagde HERREN til Moses: "Se, jeg gør dig til Gud for Farao, men din Broder Aron skal være din Profet.
2 Iwe ukanene zonse zimene ndakulamulirazi, ndipo Aaroni mʼbale wako ndiye akaziyankhule kwa Farao kuti atulutse ana a Israeli mʼdziko la Igupto.
Du skal sige til ham alt, hvad jeg pålægger dig, men din Broder Aron skal sige det til Farao, for at han skal lade Israeliterne rejse ud af sit Land.
3 Koma ndidzawumitsa mtima wa Farao, ndipo ngakhale nditachulukitsa zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa mu Igupto,
Men jeg vil forhærde Faraos Hjerte og derefter gøre mange Tegn og Undere i Ægypten.
4 iyeyo sadzakumverani. Choncho ndidzakantha Igupto, ndipo ndi ntchito zachiweruzo ndidzatulutsa magulu anga, anthu anga Aisraeli kuwachotsa mʼdziko la Igupto.
Farao skal ikke høre på eder, men jeg vil lægge min Hånd på Ægypten og føre mine Hærskarer, mit Folk Israeliterne, ud af Ægypten med vældige Straffedomme;
5 Ndipo Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzatambasula dzanja langa kukantha Igupto ndi kutulutsa Aisraeli mʼdzikomo.”
og når jeg udrækker min Hånd mod Ægypten og fører Israeliterne ud derfra, skal Ægypterne kende, at jeg er HERREN."
6 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova anawalamulira.
Da gjorde Moses og Aron, som HERREN pålagde dem.
7 Mose anali ndi zaka 80, ndipo Aaroni anali ndi zaka 83 pamene anakayankhula kwa Farao.
Moses var firsindstyve og Aron tre og firsindstyve År gammel, da de talte til Farao.
8 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
Og HERREN talede til Moses og Aron og sagde:
9 “Ngati Farao adzati kwa inu, ‘Chitani chozizwitsa,’ iwe Mose udzati kwa Aaroni, ‘Tenga ndodo yako ndipo uyiponye pamaso pa Farao,’ ndipo idzasanduka njoka.”
"Når Farao kræver et Under af eder, sig så til Aron: Tag din Stav og kast den ned foran Farao, så skal den blive til en Slange!"
10 Kotero Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kuchita monga momwe Yehova anawalamulira. Aaroni anaponya ndodo yake pansi patsogolo pa Farao ndi nduna zake ndipo inasanduka njoka.
Da gik Moses og Aron til Farao og gjorde, som HERREN bød; og da Aron kastede sin Stav foran Farao og hans Tjenere, blev den til en Slange.
11 Naye Farao anayitanitsa anthu ake anzeru ndi amatsenga, ndipo nawonso amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo.
Men Farao lod som Modtræk Vismændene og Besværgerne kalde, og de, Ægyptens Koglere, gjorde også det samme ved Hjælp af deres hemmelige Kunster;
12 Aliyense wa iwo anaponya ndodo yake pansi ndipo inasanduka njoka. Koma ndodo ya Aaroni inameza ndodo zawo.
de kastede hver sin Stav, og Stavene blev til Slanger, men Arons Stav opslugte deres Stave.
13 Koma mtima wa Farao unawuma ndipo sanawamvere monga momwe Yehova ananenera.
Men Faraos Hjerte blev forhærdet, og han hørte ikke på dem, således som HERREN havde sagt.
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Farao ndi wowuma mtima. Akukana kulola anthu anga kuti apite.
HERREN sagde nu til Moses: "Faraos Hjerte er forstokket, han vægrer sig ved at lade Folket rejse.
15 Upite kwa Farao mmawa pamene azidzapita ku madzi. Ukamudikire mʼmbali mwa Nailo kuti ukakumane naye ndipo unyamule ndodo imene inasanduka njoka ija mʼdzanja lako.
Gå derfor i Morgen tidlig til Farao, når han begiver sig ned til Vandet, og træd frem for ham ved Nilens Bred og tag Staven, der forvandledes til en Slange, i Hånden
16 Ndipo ukamuwuze Farao kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri wandituma kuti ndikuwuzeni kuti: Lolani anthu anga apite kuti akandipembedze mʼchipululu. Koma mpaka tsopano inu simunandimvere.
og sig til ham: HERREN, Hebræernes Gud, sendte mig til dig med det Bud: Lad mit Folk rejse, at det kan dyrke mig i Ørkenen! Men hidtil har du ikke adlydt.
17 Izi ndi zimene Yehova akunena: Ndi ndodo imene ili mʼdzanja langa ndidzamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi adzasanduka magazi. Ndikadzachita ichi udzadziwa kuti Ine ndine Yehova:
Så siger HERREN: Deraf skal du kende, at jeg er HERREN: Se, jeg slår Vandet i Nilen med Staven, som jeg holder i min Hånd, og det skal forvandles til Blod,
18 Nsomba za mu Nailo zidzafa, mtsinje udzanunkha ndipo Aigupto sadzatha kumwa madzi ake.’”
Fiskene i Nilen skal dø, og Nilen skal stinke, og Ægypterne skal væmmes ved at drikke Vand fra Nilen."
19 Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Tenga ndodo yako uyilozetse ku madzi a mu Igupto pa mitsinje, pa ngalande, pa zithaphwi ndi pa madambo, ndipo onse adzasanduka magazi.’ Mʼdziko lonse la Igupto mudzakhala magazi, ngakhale mʼzotungira madzi zopangidwa ndi mitengo ndi miyala.”
Og HERREN sagde til Moses: "Sig til Aron: Tag din Stav og ræk din Hånd ud over Ægypternes Vande, deres Floder, Kanaler, Damme og alle Vandsamlinger, så skal Vandet blive til Blod, og der skal være Blod i hele Ægypten, både i Trækar og Stenkar."
20 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova analamulira. Anakweza ndodo yake pamaso pa Farao ndi akuluakulu ake ndipo anamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi onse anasanduka magazi.
Og Moses og Aron gjorde, som HERREN bød; Moses løftede Staven og slog Vandet i Nilen for Øjnene af Farao og hans Tjenere, og alt Vandet i Nilen forvandledes til Blod;
21 Nsomba za mu Nailo zinafa ndipo mtsinje unanunkha kwambiri kotero kuti Aigupto sanathe kumwa madzi ake. Magazi anali ponseponse mu Igupto.
Fiskene i Nilen døde, og Nilen stank, så Ægypterne ikke kunde drikke Vand fra Nilen, og der var Blod i hele Ægypten.
22 Koma amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo. Choncho Farao anawumabe mtima, ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananeneratu.
Men de Ægyptiske Koglere gjorde det samme ved Hjælp af deres hemmelige Kunster, og Faraos Hjerte blev forhærdet, så han ikke hørte på dem, således som HERREN havde sagt.
23 Mʼmalo mwake iye anatembenuka ndi kupita ku nyumba yake yaufumu ndipo zimenezi sanazilabadire.
Da vendte Farao sig bort og gik hjem, og heller ikke dette lagde han sig på Sinde.
24 Anthu onse a ku Igupto anayamba kukumba mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo kuti apeze madzi akumwa, chifukwa sanathe kumwa madzi a mu mtsinjemo.
Men alle Ægypterne gravede i Omegnen af Nilen efter Drikkevand, thi de kunde ikke drikke Nilvandet.
25 Panapita masiku asanu ndi awiri Yehova atamenya madzi a mu mtsinje wa Nailo.
Og således gik der syv Dage, efter at HERREN havde slået Nilen.

< Eksodo 7 >