< Eksodo 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Taona ine ndakuyika kuti ukhale ngati Mulungu kwa Farao, ndipo mʼbale wako Aaroni adzakhala mneneri wako.
上主向梅瑟說:「看,我使你在法朗前像神一樣,你的哥哥亞郎將作你的代言人。
2 Iwe ukanene zonse zimene ndakulamulirazi, ndipo Aaroni mʼbale wako ndiye akaziyankhule kwa Farao kuti atulutse ana a Israeli mʼdziko la Igupto.
凡我吩咐你的一切,你要告訴你的哥哥亞郎,要他對法朗講話,叫他放以色列子民離開他的國境。
3 Koma ndidzawumitsa mtima wa Farao, ndipo ngakhale nditachulukitsa zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa mu Igupto,
我卻要使法朗心硬,為此在埃及國要增多我的奇蹟和異事。
4 iyeyo sadzakumverani. Choncho ndidzakantha Igupto, ndipo ndi ntchito zachiweruzo ndidzatulutsa magulu anga, anthu anga Aisraeli kuwachotsa mʼdziko la Igupto.
因法朗布聽從你們,我要向埃及伸手,藉嚴厲的懲罰,將我的軍隊,我的百姓以色列子民,從埃及國領出來。
5 Ndipo Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzatambasula dzanja langa kukantha Igupto ndi kutulutsa Aisraeli mʼdzikomo.”
當我向埃及人伸手,將以色列子民從埃及人中間領出來的時候,他們要承認我是上主。」
6 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova anawalamulira.
梅瑟和亞郎就受命行事;上主怎樣吩咐他們,他們就怎樣行了。
7 Mose anali ndi zaka 80, ndipo Aaroni anali ndi zaka 83 pamene anakayankhula kwa Farao.
當他們去與法朗會談的時候,梅瑟八十歲,亞郎八十三歲。
8 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
上主對梅瑟和亞郎說:「
9 “Ngati Farao adzati kwa inu, ‘Chitani chozizwitsa,’ iwe Mose udzati kwa Aaroni, ‘Tenga ndodo yako ndipo uyiponye pamaso pa Farao,’ ndipo idzasanduka njoka.”
如果法朗要求你們說:你們顯個奇蹟,給你們作證罷! 你就吩咐亞郎說:將你的棍杖扔在法朗的面前,棍杖就會變成一條蛇。」
10 Kotero Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kuchita monga momwe Yehova anawalamulira. Aaroni anaponya ndodo yake pansi patsogolo pa Farao ndi nduna zake ndipo inasanduka njoka.
梅瑟和亞郎就去見法朗,照上主的吩咐做了:亞郎將棍杖扔在法朗和他的臣僕面前,棍杖就變成了一條蛇。
11 Naye Farao anayitanitsa anthu ake anzeru ndi amatsenga, ndipo nawonso amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo.
法朗將他的智者和術士召來,這些埃及的巫士也用他們的巫術作了同樣的事:
12 Aliyense wa iwo anaponya ndodo yake pansi ndipo inasanduka njoka. Koma ndodo ya Aaroni inameza ndodo zawo.
他們每人扔下自己的棍杖,也都變成了蛇,但亞郎的棍杖卻吞了他們的棍杖。
13 Koma mtima wa Farao unawuma ndipo sanawamvere monga momwe Yehova ananenera.
法朗仍然心硬,不肯聽他們的話,正如上主所說。第一災、水變血
14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Farao ndi wowuma mtima. Akukana kulola anthu anga kuti apite.
上主對梅瑟說:「法朗硬了心,拒絕釋放百姓。
15 Upite kwa Farao mmawa pamene azidzapita ku madzi. Ukamudikire mʼmbali mwa Nailo kuti ukakumane naye ndipo unyamule ndodo imene inasanduka njoka ija mʼdzanja lako.
明天早晨你去見法朗。他去水邊時候,你要站在尼羅河邊迎住他;手中拿著那根變過蛇的棍杖。
16 Ndipo ukamuwuze Farao kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri wandituma kuti ndikuwuzeni kuti: Lolani anthu anga apite kuti akandipembedze mʼchipululu. Koma mpaka tsopano inu simunandimvere.
你對他說:上主,希伯來人的天主打發我來見你說:你應放我的百姓到曠野中去崇拜我;彈道現在你仍沒有聽從。
17 Izi ndi zimene Yehova akunena: Ndi ndodo imene ili mʼdzanja langa ndidzamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi adzasanduka magazi. Ndikadzachita ichi udzadziwa kuti Ine ndine Yehova:
上主這樣說:看,我要用我手中拿的棍杖擊打河水,水就變成血,如此你必承認,我是上主。
18 Nsomba za mu Nailo zidzafa, mtsinje udzanunkha ndipo Aigupto sadzatha kumwa madzi ake.’”
河中的魚都要死,河水都要腥臭,埃及人不能再喝河中的水。」
19 Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Tenga ndodo yako uyilozetse ku madzi a mu Igupto pa mitsinje, pa ngalande, pa zithaphwi ndi pa madambo, ndipo onse adzasanduka magazi.’ Mʼdziko lonse la Igupto mudzakhala magazi, ngakhale mʼzotungira madzi zopangidwa ndi mitengo ndi miyala.”
上主對梅瑟說:「你向亞郎說:拿起你的棍杖,將手伸在埃及的水上,即伸在河、溝渠、池沼和一切水塘之上,水都要變成血;如此埃及全國,連木器石器中的水野都要變成血。」
20 Mose ndi Aaroni anachita monga momwe Yehova analamulira. Anakweza ndodo yake pamaso pa Farao ndi akuluakulu ake ndipo anamenya madzi a mu Nailo, ndipo madzi onse anasanduka magazi.
梅瑟和亞郎就照了上主的吩咐作了:亞郎在法朗和他臣僕的面前,舉起棍杖一打河水,所有的河水變成了血;
21 Nsomba za mu Nailo zinafa ndipo mtsinje unanunkha kwambiri kotero kuti Aigupto sanathe kumwa madzi ake. Magazi anali ponseponse mu Igupto.
河中的魚都死了,河水都腥臭不堪,埃及人不能再喝河中的水;埃及遍地是血。
22 Koma amatsenga a Chiigupto anachita zinthu zomwezo mwa matsenga awo. Choncho Farao anawumabe mtima, ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananeneratu.
埃及的巫士用他們的巫術也行了同樣的事,因此法朗仍舊心硬,不肯聽信梅瑟和亞郎,正像上主所說的。
23 Mʼmalo mwake iye anatembenuka ndi kupita ku nyumba yake yaufumu ndipo zimenezi sanazilabadire.
法朗轉身回到宮中,沒有把事放在心上。
24 Anthu onse a ku Igupto anayamba kukumba mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo kuti apeze madzi akumwa, chifukwa sanathe kumwa madzi a mu mtsinjemo.
因為全埃及的人不能喝河中的水,便在河的附近掘水喝。第二災、蝦蟆
25 Panapita masiku asanu ndi awiri Yehova atamenya madzi a mu mtsinje wa Nailo.
上主擊打河水後,滿了七天,

< Eksodo 7 >