< Eksodo 6 >
1 Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
Manke Rəbbee Mısayk'le eyhen: – Həşde vak'le g'acesın, Zı hucooyiy fironuk ha'a. Yizde xənne gucune ögiyl, mang'vee manbı g'avkasınbıb, vuk'lele haa'as saccu cune ölkeençe hudooracenva.
2 Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
Qiyğa Allahee Mısayk'le eyhen: – Zı Rəbb vorna.
3 Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
Zı İbrahimıs, I'saq'ı's, Yaaq'ubus Gırgın Əxəna Allah xhinne gyagu, Zıcar Zı manbışis YAHVE xhinne qıvats'ı'ı deş.
4 Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
Zı manbışika mugaavileniy hav'u, co menne cigaynbı xhinne aaxvan Kana'anğançenbışin cigabı cos helesva.
5 Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
Zak'le İzrailybışe, Misirbışde xılençe ts'ıts'a'an uts'ur ats'an. Zasse şenbışika hav'una mugaavile yik'el hipxın deş.
6 “Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
Mançil-alla İzrailybışik'le eyhe: «Zı Rəbb vorna. Zı şole Misirbışda xamut g'avşesda. Zı Yizde xənne gucuka Misirbışis yı'q'na cazaa huvu, şu manbışde nukariyvalike g'attivxhan haa'asınbı.
7 Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
Zı şoke Zasın millet ha'as, Zı vuşda Allah ixhes. Manke şok'le ats'axhxhesın, Zı şu Misireene əq'übeençe g'attivxhan hav'una vuşda Rəbb Allah vor.
8 Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
Zı şu İbrahimıs, I'saq'ı's, Yaaq'ubus k'ın g'assır helesva uvhuyne cigabışeeqa quvkees. Man cıgabı vuşunbı ixhes. Zı Rəbb vorna».
9 Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
Mısee man uvhuynbı İzrailybışis yuşana'a. Manbı əq'übayn rı'hı'le g'av'uva, manbışe mang'ul k'ırı iliyxhe deş.
10 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
Manke Rəbbee Mısayk'le eyhen:
11 “Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
– Fironusqa, Misirne paççahısqa, hark'ın eyhe, İzrailybı cune ölkeençe g'avkecen.
12 Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
Mısee Rəbbik'le eyhen: – İzrailybışe zal k'ırı ilydiyxhe, fironee nəxüd zal k'ırı ilixheye? Zasse yugrar yuşana'as əxə deş.
13 Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
Rəbb Mısaykayiy Harunuka yuşan hı'ı, manbı fironusqa Misirne paççahısqa g'uxoole, İzrailybı cune ölkeençe g'avkecenva.
14 Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
İzrailybışde nasılbışin ç'ak'ınbı inbı vob: İzrailyne ts'erriyne duxayn Ruvenın dixbı: Xanok, Pallu, Xetsroniy Karmi. İn xizanbı Ruvenıke g'adıynbı vod.
15 Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
Şimonun dixbı: Yemuel, Yamin, Ohad, Yakin, Tsoxar. Sayir Kana'anğançene xhunaşşeykena dix Şaul. İn xizanbı Şimonıke g'adıynbı vod.
16 Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
Xərıng'ule otçu k'ıning'ulqamene Leviyne dixbışin dobı: G'erşon, Qohat, Merari. Levee vəşşe xhebts'ale yighılle sen ha'a.
17 Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
G'erşonun dixbı: Livniyiy Şimey. Manbışqad xizanbı ıxha.
18 Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
Qohatın dixbı: Amram, İtshar, Xevron, Uzziel. Qohatee vəşşe xhebts'ale xhebılle sen ha'a.
19 Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
Merariyn dixbı: Maxliyiy Muşi. İn xizanbı Leviyke g'adıynbı vod.
20 Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
Amramee cuna mamasiy Yoxeved hee'e. Məng'ee Amramıs Haruniy Mısa vuxu. Amramee vəşşe xhebts'ale yighılle sen ha'a.
21 Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
İtsharın dixbı: Qorax, Nefeg, Zixri.
22 Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
Uzzielin dixbı: Mişael, Eltsafan, Zıtri.
23 Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Harunee Amminadavna yiş Elişeeva hee'e. Mana Naxşonna yiçu yixha. Məng'ee Harunus Nadav, Avihu, Eliazar, İtamar vuxu.
24 Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
Qoraxın dixbı: Assir, Elqana, Aviasaf. İnbı Qoraxın xizanbı.
25 Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
Harunne duxee Eliazaree Putielyne yişbışda sa hee'e. Məng'ee Eleazarıs Pinxas uxu. Leviyne xizanbışin ç'ak'ınbı inbı vob.
26 Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
İne nasılenbıniy vob Haruniy Mısa. Rəbbe manbışik'leniy uvhu, İzrailybı Misirğançe g'oşunbı xhinne qığee'ecenva.
27 Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
Manbıniy fironuka Misirne paççahıka İzrailybı Misirğançe qığav'uyne hək'ee yuşan hav'u. İnəxbın insanar vuxha Mısayiy Harun.
28 Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
Rəbb Mısayka Misir yuşana'ang'a
29 anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
uvhuynniy: – Zı Rəbb vorna! Zı vak'le uvhuyn gırgın kar fironuk'le, Misirne paççahık'le eyhe.
30 Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”
Mısee Rəbbik'le eyhen: – Zasse yugrar yuşana'as əxə deş, nəxüdne fironee zal k'ırı alixhxhes?