< Eksodo 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
A Gospod reèe Mojsiju: sad æeš vidjeti šta æu uèiniti Faraonu; jer pod rukom krjepkom pustiæe ih, i istjeraæe ih iz zemlje svoje pod rukom krjepkom.
2 Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
Još govori Bog Mojsiju i reèe mu: ja sam Gospod.
3 Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
I javio sam se Avramu, Isaku i Jakovu imenom Bog svemoguæi, a imenom svojim Gospod ne bih im poznat.
4 Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
I uèinih zavjet svoj s njima da æu im dati zemlju Hanansku, zemlju u kojoj bijahu došljaci, u kojoj življahu kao stranci.
5 Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
I èuh uzdisanje sinova Izrailjevijeh, koje Misirci drže u ropstvu, i opomenuh se zavjeta svojega.
6 “Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
Zato kaži sinovima Izrailjevijem: ja sam Gospod, i izvešæu vas ispod bremena Misirskih, i oprostiæu vas ropstva njihova, i izbaviæu vas mišicom podignutom i sudovima velikim.
7 Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
I uzeæu vas da mi budete narod, i ja æu vam biti Bog, te æete poznati da sam ja Gospod Bog vaš, koji vas izvodim ispod bremena Misirskih.
8 Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
Pak æu vas odvesti u svoju zemlju, za koju podigoh ruku svoju zaklinjuæi se da æu je dati Avramu, Isaku i Jakovu; i daæu vam je u našljedstvo, ja Gospod.
9 Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
I Mojsije kaza tako sinovima Izrailjevijem; ali ne poslušaše Mojsija od slabosti duha svojega i od ljutoga ropstva.
10 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
I Gospod reèe Mojsiju govoreæi:
11 “Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
Idi, kaži Faraonu caru Misirskom neka pusti sinove Izrailjeve iz zemlje svoje.
12 Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
A Mojsije progovori pred Gospodom i reèe: eto, sinovi Izrailjevi ne poslušaše me, a kako æe me poslušati Faraon, kad sam neobrezanijeh usana?
13 Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
Ali Gospod govori Mojsiju i Aronu, i zapovjedi im da idu k sinovima Izrailjevijem i k Faraonu, da izvedu sinove Izrailjeve iz zemlje Misirske.
14 Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
Ovo su poglavice u domovima otaca svojih: sinovi Ruvima prvenca Izrailjeva: Enoh i Faluj, Asron i Harmija; to su porodice Ruvimove.
15 Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
A sinovi Simeunovi: Jemuilo i Jamin i Aod i Ahin i Sar i Saul, sin neke Hananejke; to su porodice Simeunove.
16 Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
A ovo su imena sinova Levijevih po porodicama njihovijem: Girson i Kat i Merarije; a Levije poživje sto i trideset i sedam godina.
17 Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
A ovo su sinovi Girsonovi: Lovenije i Semej po porodicama svojim.
18 Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
A sinovi Katovi: Amram i Isar i Hevron i Ozilo; a Kat poživje sto i trideset i tri godine.
19 Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
A sinovi Merarijevi: Molija i Musija. To su porodice Levijeve po lozama svojim.
20 Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
A Amram se oženi Johavedom bratuèedom svojom, i ona mu rodi Arona i Mojsija. A poživje Amram sto i trideset i sedam godina.
21 Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
A sinovi Isarovi bjehu: Korej i Nafek i Zehrija.
22 Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
A sinovi Ozilovi: Misailo i Elisafan i Segrija.
23 Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
A Aron se oženi Jelisavetom kæerju Aminadavovom, sestrom Nasonovom; i ona mu rodi Nadava i Avijuda i Eleazara i Itamara.
24 Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
A sinovi Korejevi bjehu: Asir i Elkana i Avijasar. To su porodice Korejeve.
25 Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
I Eleazar sin Aronov oženi se jednom od kæeri Futilovijeh, i ona mu rodi Finesa. To su poglavice izmeðu otaca Levitskih po svojim porodicama.
26 Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
To je Aron i Mojsije, kojima reèe Gospod: izvedite sinove Izrailjeve iz zemlje Misirske u èetama njihovijem.
27 Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
To su koji govoriše Faraonu caru Misirskom da izvedu sinove Izrailjeve iz Misira; to je Mojsije i to je Aron.
28 Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
I kad Gospod govoraše Mojsiju u zemlji Misirskoj,
29 anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
Reèe Gospod Mojsiju govoreæi: ja sam Gospod; kaži Faraonu caru Misirskom sve što sam ti kazao.
30 Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”
I Mojsije reèe pred Gospodom: evo sam neobrezanijeh usana, pa kako æe me poslušati Faraon?

< Eksodo 6 >