< Eksodo 6 >
1 Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
And YHWH says to Moses, “Now you see that which I do to Pharaoh, for with a strong hand he sends them away, indeed, with a strong hand he casts them out of his land.”
2 Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
And God speaks to Moses and says to him, “I [am] YHWH,
3 Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
and I appear to Abraham, to Isaac, and to Jacob, as God Almighty; as for My Name YHWH, I have not been known to them;
4 Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
and I have also established My covenant with them, to give the land of Canaan to them, the land of their sojournings, wherein they have sojourned;
5 Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
and I have also heard the groaning of the sons of Israel, whom the Egyptians are causing to serve, and I remember My covenant.
6 “Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
Therefore say to the sons of Israel: I [am] YHWH, and I have brought you out from under the burdens of the Egyptians, and have delivered you from their service, and have redeemed you by an outstretched arm, and by great judgments,
7 Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
and have taken you to Myself for a people, and I have been to you for God, and you have known that I [am] your God YHWH, who is bringing you out from under the burdens of the Egyptians;
8 Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
and I have brought you to the land which I have lifted up My hand to give it to Abraham, to Isaac, and to Jacob, and have given it to you—a possession; I [am] YHWH.”
9 Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
And Moses speaks so to the sons of Israel, and they did not listen to Moses, for anguish of spirit, and for harsh service.
10 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
And YHWH speaks to Moses, saying,
11 “Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
“Go in, speak to Pharaoh king of Egypt, and he sends the sons of Israel out of his land”;
12 Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
and Moses speaks before YHWH, saying, “Behold, the sons of Israel have not listened to me, and how does Pharaoh hear me, and I of uncircumcised lips?”
13 Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
And YHWH speaks to Moses and to Aaron, and charges them for the sons of Israel, and for Pharaoh king of Egypt, to bring out the sons of Israel from the land of Egypt.
14 Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
These [are] heads of the house of their fathers. Sons of Reuben firstborn of Israel: Enoch, and Phallu, Hezron, and Carmi; these [are] families of Reuben.
15 Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
And sons of Simeon: Jemuel, and Jamin, and Ohad, and Jachin, and Zohar, and Shaul, son of the Canaanite; these [are] families of Simeon.
16 Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
And these [are] the names of the sons of Levi, as to their births: Gershon, and Kohath, and Merari; and the years of the life of Levi [are] one hundred and thirty-seven years.
17 Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
The sons of Gershon: Libni and Shimi, as to their families.
18 Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
And the sons of Kohath: Amram, and Izhar, and Hebron, and Uzziel; and the years of the life of Kohath [are] one hundred and thirty-three years.
19 Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
And the sons of Merari: Mahli and Mushi; these [are] families of Levi, as to their births.
20 Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
And Amram takes his aunt Jochebed to himself for a wife, and she bears Aaron and Moses to him; and the years of the life of Amram [are] one hundred and thirty-seven years.
21 Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
And sons of Izhar: Korah, and Nepheg, and Zichri.
22 Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
And sons of Uzziel: Mishael, and Elzaphan, and Sithri.
23 Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
And Aaron takes Elisheba daughter of Amminadab, sister of Naashon, to himself for a wife, and she bears to him Nadab, and Abihu, Eleazar, and Ithamar.
24 Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
And sons of Korah: Assir, and Elkanah, and Abiasaph; these [are] families of the Korahite.
25 Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
And Eleazar, Aaron’s son, has taken to himself [one] of the daughters of Putiel for a wife for himself, and she bears Phinehas to him; these [are] heads of the fathers of the Levites, as to their families.
26 Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
This [is] Aaron—and Moses—to whom YHWH said, “Bring out the sons of Israel from the land of Egypt, by their hosts”;
27 Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
these are they who are speaking to Pharaoh king of Egypt, to bring out the sons of Israel from Egypt, this [is] Moses—and Aaron.
28 Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
And it comes to pass in the day of YHWH’s speaking to Moses in the land of Egypt,
29 anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
that YHWH speaks to Moses, saying, “I [am] YHWH, speak to Pharaoh king of Egypt all that I am speaking to you.”
30 Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”
And Moses says before YHWH, “Behold, I [am] of uncircumcised lips, and how does Pharaoh listen to me?”