< Eksodo 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
Men HERREN svarede Moses: »Nu skal du faa at se, hvad jeg vil gøre ved Farao! Med Magt skal han blive tvunget til at lade dem rejse, og med Magt skal han blive tvunget til at drive dem ud af sit Land!«
2 Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
Gud talede til Moses og sagde til ham: »Jeg er HERREN!
3 Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
For Abraham, Isak og Jakob aabenbarede jeg mig som Gud den Almægtige, men under mit Navn HERREN gav jeg mig ikke til Kende for dem.
4 Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
Eftersom jeg har oprettet min Pagt med dem om at skænke dem Kana'ans Land, deres Udlændigheds Land, hvor de levede som fremmede,
5 Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
har jeg nu hørt Israeliternes Klageraab over, at Ægypterne holder dem i Trældom, og jeg er kommet min Pagt i Hu.
6 “Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
Derfor skal du sige til Israeliterne: Jeg er HERREN, og jeg vil udfri eder fra det Trællearbejde, Ægypterne har paalagt eder, og frelse eder fra deres Trældom og udløse eder med udrakt Arm og med vældige Straffedomme;
7 Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
og saa vil jeg antage eder som mit Folk og være eders Gud, og I skal kende, at jeg er HERREN eders Gud, som udfrier eder fra Ægypternes Trællearbejde;
8 Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
og jeg vil føre eder til det Land, jeg har svoret at ville skænke Abraham, Isak og Jakob, og give eder det i Eje. Jeg er HERREN!«
9 Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
Moses kundgjorde nu dette for Israeliterne; men de hørte ikke paa Moses, dertil var deres Modløshed for stor og deres Trællearbejde for haardt.
10 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
Da talede HERREN til Moses og sagde:
11 “Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
»Gaa hen og sig til Farao, Ægyptens Konge, at han skal lade Israeliterne drage ud af, sit Land!«
12 Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
Men Moses sagde for HERRENS Aasyn: »Israeliterne har ikke hørt paa mig, hvor skulde da Farao gøre det, tilmed da jeg er uomskaaren paa Læberne?«
13 Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
Da talede HERREN til Moses og Aron og sendte dem til Farao, Ægyptens Konge, for at føre Israeliterne ud af Ægypten.
14 Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
Følgende var Overhovederne for deres Fædrenehuse: Rubens, Israels førstefødtes, Sønner var: Hanok, Pallu, Hezron og Harmi; det er Rubens Slægter.
15 Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
Simeons. Sønner var Jemuel, Jamin, Ohad, Jakin, Zohar og Kana'anæerkvindens Søn Sja'ul; det er Simeons Slægter.
16 Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
Følgende er Navnene paa Levis Sønner efter deres Nedstamning: Gerson, Kehat og Merari. Levis Levetid var 137 Aar.
17 Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
Gersons Sønner var Libni og Sjim'i efter deres Slægter.
18 Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
Kehats Sønner var Amram, Jizhar, Hebron og Uzziel. Kehats Levetid var 133 Aar.
19 Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
Meraris Sønner var Mali og Musji. Det er Levis Slægter efter deres Nedstamning.
20 Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
Amram tog sin Faster Jokebed til Ægte; og hun fødte ham Aron og Moses. Amrams Levetid var 137 Aar.
21 Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
Jizhars Sønner var Kora, Nefeg og Zikri.
22 Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
Uzziels Sønner var Misjael, Elzafan og Sitri.
23 Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Aron tog Amminadabs Datter, Nahasjons Søster Elisjeba til Ægte; og hun fødte ham Nadab, Abihu, Eleazar og Itamar.
24 Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
Koras Sønner var Assir, Elkana og Abi'asaf; det er Koraiternes Slægter.
25 Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
Arons Søn Eleazar tog en at Putiels Døtre til Ægte; og hun fødte ham Pinehas. Det er Overhovederne for Leviternes Fædrenehuse efter deres Slægter.
26 Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
Det var Aron og Moses, som HERREN sagde til: »Før Israeliterne ud af Ægypten, Hærafdeling for Hærafdeling!«
27 Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
Det var dem, der talte til Farao, Ægyptens Konge, om at føre Israeliterne ud af Ægypten, Moses og Aron.
28 Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
Dengang HERREN talede til Moses i Ægypten,
29 anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
talede HERREN til Moses saaledes: »Jeg er HERREN! Forkynd Farao, Ægyptens Konge, alt, hvad jeg siger dig!«
30 Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”
Men Moses sagde for HERRENS Aasyn: »Se, jeg er uomskaaren paa Læberne, hvorledes skulde da Farao ville høre paa mig?«

< Eksodo 6 >