< Eksodo 5 >
1 Zitachitika izi, Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndipo anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Aloleni anthu anga apite, kuti akachite chikondwerero cha Ine mʼchipululu.’”
And after that Moses and Aaron went in, and said unto Pharaoh, Thus hath said the Everlasting One, the God of Israel, Let my people go, that they may hold a feast unto me in the wilderness.
2 Koma Farao anati, “Yehova ndani kuti ine ndimumvere ndi kulola Aisraeli kuti apite? Ine Yehova sindikumudziwa ndipo sindilola kuti Aisraeli apite.”
And Pharaoh said, Who is the Everlasting, whose voice I am to obey, to let Israel go? I know not the Everlasting, nor will I let Israel go.
3 Ndipo iwo anati, “Mulungu wa Ahebri anakumana nafe. Chonde tiloleni tipite ulendo wa masiku atatu ku chipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu, ngati sititero iye adzatipweteka ndi miliri kapena lupanga.”
And they said, The God of the Hebrews hath met with us: let us go, we pray thee, a three days' journey into the desert, and sacrifice unto the Lord our God; lest he fall upon us with the pestilence, or with the sword.
4 Koma mfumu ya Igupto inati, “Mose ndi Aaroni, chifukwa chiyani mukuchititsa anthuwa kuti asagwire ntchito zawo? Bwererani ku ntchito zanu!”
And the king of Egypt said unto them, Wherefore do ye, Moses and Aaron, hinder the people from their works? get you unto your own affairs.
5 Ndiponso Farao anati, “Taonani, anthuwa mʼdziko muno alipo ochuluka, ndipo inu mukuwaletsa kugwira ntchito.”
And Pharaoh said, Behold, the people of the land now are many, and ye disturb them in the pursuit of their labors.
6 Pa tsiku lomwelo Farao analamulira akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu kuti
And Pharaoh commanded on the same day the taskmasters of the people, and its officers, saying,
7 “Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo.
Ye shall no more give the people straw to make the bricks, as yesterday and the day before; they themselves shall go and gather themselves straw.
8 Koma musawachepetsere chiwerengero cha njerwa chomwe munawalamulira kale kuti aziwumba. Iwowa ndi aulesi. Nʼchifukwa chake akulira kuti, ‘Tiloleni tipite tikapereke nsembe kwa Mulungu wathu.’
And the number of the bricks, which they did make heretofore, ye shall impose upon them, ye shall not diminish aught thereof; for they are idle: therefore they cry, saying, Let us go and sacrifice to our God.
9 Muwakhawulitse ndi ntchito anthu amenewa kuti azitanganidwa, asakhale ndi mpata omvera zabodza.”
Let the work be made to lie heavily upon the men, that they may have enough to do therein; and that they may not pay attention to false words.
10 Choncho akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu anapita kwa anthu aja nati, “‘Farao akuti sadzakupatsaninso udzu.
And the taskmasters of the people and its officers went out, and they said to the people, saying, Thus saith Pharaoh, I will not give you any straw.
11 Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’”
Go ye, get yourselves straw from wherever ye can find it; yet not the least shall be taken off from your work.
12 Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu.
And the people scattered themselves abroad throughout all the land of Egypt to gather stubble instead of straw.
13 Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.”
And the taskmasters were urgent, saying, Fulfill your works, every day its due portion, just as when there was straw.
14 Akapitawo a thangata a Farao ankawamenya oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja nawapanikiza kuti, “Chifukwa chiyani lero simunawumbe chiwerengero chovomerezeka cha njerwa monga chakale chija?”
And the officers of the children of Israel, whom the taskmasters of Pharaoh had set over them, were beaten, as these said, Wherefore have ye not fulfilled your task in making brick as heretofore, both yesterday and today?
15 Pamenepo oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja anapita kukadandaula kwa Farao kuti, “Chifukwa chiyani mwachitira antchito anu zotere?
And the officers of the children of Israel came and cried unto Pharaoh, saying, Wherefore dealest thou thus with thy servants?
16 Antchito anu sakupatsidwa udzu, komabe akutiwuza kuti, ‘Umbani njerwa!’ Antchito anu akumenyedwa, koma cholakwa sichili ndi anthu anu.”
Straw is not given unto thy servants, and, Make bricks, say they to us: and, behold, thy servants are beaten, and thy people are treated as sinners.
17 Farao anati, “Ulesi, inu ndinu alesi! Nʼchifukwa chake mukumanena kuti, ‘Mutilole tipite kukapereka nsembe kwa Yehova.’
But he said, Idle are ye, idle; therefore say ye, Let us go and sacrifice to the Lord.
18 Pitani tsopano kuntchito. Simudzapatsidwanso udzu komabe muyenera kuwumba muyeso wanu wovomerezeka wa njerwa.”
And now go, work, and straw shall not be given you; yet the required number of bricks shall ye deliver.
19 Oyangʼanira anzawo a Chiisraeli anazindikira kuti ali pa mavuto pamene anawuzidwa kuti, “Musachepetse chiwerengero cha njerwa chimene muyenera kuwumba tsiku lililonse.”
And the officers of the children of Israel saw themselves in the evil necessity to say, Ye shall not diminish aught from your bricks, every day of its task.
20 Atachoka pamaso pa Farao, anakumana ndi Mose ndi Aaroni akuwadikira,
And they met Moses and Aaron, standing in their way, as they came forth from Pharaoh.
21 ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.”
And they said unto them, May the Lord look upon you, and judge; because ye have made our savor to be abhorred in the eyes of Pharaoh, and the eyes of his servants, to put a sword in their hand to slay us.
22 Mose anabwerera kwa Yehova ndipo anati, “Chonde Ambuye, chifukwa chiyani mukuzunza anthu anu? Kodi munanditumira zimenezi?
And Moses returned unto the Lord, and said, Lord, wherefore hast thou let so much evil come upon this people? why is it that thou hast sent me?
23 Chipitireni changa kwa Farao kukamuyankhula mʼdzina lanu, iye wakhala akuzunza anthuwa, ndipo inu simunawapulumutse konse anthu anu.”
For, since I came unto Pharaoh to speak in thy name, he hath done more evil to this people; but thou hast in nowise delivered thy people.