< Eksodo 39 >
1 Anapanga zovala za ansembe, zovala potumikira ku malo wopatulika pogwiritsa ntchito nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira. Anapanganso zovala zopatulika za Aaroni monga momwe Yehova analamulira Mose.
Y de la costura de azul, púrpura y rojo hicieron las vestiduras para la obra del lugar santo, y las vestiduras sagradas para Aarón, como el Señor le había dado órdenes a Moisés.
2 Popanga efodi, iwo anagwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yosalala yofewa.
El efod hizo de oro, tela azul, púrpura, rojo y el mejor lino;
3 Anasula golide wopyapyala ndi kumulezaleza kuti alumikize kumodzi ndi nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yosalala yofewa yolukidwa mwaluso.
Martillando el oro en láminas delgadas y cortándolo en alambres para trabajar en la tela azul y el púrpura y el rojo y el lino por el diseñador.
4 Iwo anapanga efodi imene inali ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa, tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
E hicieron dos hombreras para unir sus bordes en la parte superior de los brazos.
5 Lamba womangira efodi anali wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Anali nsalu imodzi ndi efodiyo, wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Y él cinto bellamente trabajado que estaba sobre él, era del mismo diseño y del mismo material, trabajado en oro y tela azul, púrpura y rojo y lino torcido, como el Señor le dio órdenes a Moisés.
6 Iwo anakonza miyala ya onikisi ndi kuyiika mu zoyikamo zake zagolide ndipo anazokota mayina a ana a Israeli monga amachitira pa chidindo.
Luego hicieron las piedras de ónice, fijadas en marcos de oro y cortados como un sello, con los nombres de los hijos de Israel.
7 Kenaka anayimangirira pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli monga momwe Yehova analamulira Mose.
Estos se pusieron sobre las hombreras del efod, para ser piedras de memoria para los hijos de Israel, como el Señor le había dicho a Moisés.
8 Iwo anapanga chovala chapachifuwa mwaluso kwambiri. Anachipanga ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
El pectoral del sacerdote fue diseñada como el efod, del mejor lino trabajado con oro y tela azul, púrpura y rojo.
9 Kutalika kwake kunali kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, chinali chopinda pawiri.
Era cuadrado y doblado en dos, tan largo y ancho como la mano de un hombre;
10 Kenaka anayikapo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba anayika miyala ya rubi, topazi ndi berili;
Y sobre ella pusieron cuatro líneas de piedras: en la primera línea había una cornalina, una crisólito y una esmeralda;
11 mzere wachiwiri anayikapo miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
En el segundo, un rubí, un zafiro y un ónice;
12 mzere wachitatu anayikapo miyala ya opera, agate ndi ametisiti;
En el tercero, un jacinto, un ágata y una amatista;
13 mzere wachinayi anayikapo miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi anayiyika mu zoyikamo zagolide.
En el cuarto, un topacio, un berilo y un jaspe; fueron arreglados en marcos retorcidos de oro.
14 Miyalayo inalipo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse unazokotedwa ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
Había doce piedras para las doce tribus de Israel; en cada uno se cortó el nombre de una de las tribus de Israel, como el corte de un sello.
15 Anapanga timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
Y en él pectoral pusieron cadenas de oro, retorcidas como cuerdas.
16 Anapanganso zoyikamo zake zagolide ndi mphete ziwiri zagolide, ndipo anamangirira mphetezo pa ngodya ziwiri za chovala chapachifuwa.
E hicieron dos marcos de oro y dos anillos de oro, y los anillos se fijaron en los extremos del pectoral del sacerdote;
17 Anamangirira timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
Y pusieron las dos cadenas retorcidas en los dos anillos en los extremos del pectoral del sacerdote;
18 Ndipo mbali ina ya timaunyoloto anamangirira pa zoyikapo zake ziwiri zija, ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
Y los otros dos extremos de las cadenas se unieron a los dos marcos y se fijaron en la parte delantera del efod sobre las hombreras.
19 Anapanganso mphete ziwiri zagolide ndipo analumikiza ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
Hicieron además dos anillos de oro, y los pusieron en los dos extremos inferiores del pectoral, en el lado interno más cercano al efod.
20 Kenaka anapanga mphete zina ziwiri zagolide ndi kuzilumikiza kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
Y se pusieron otros dos anillos de oro en la parte delantera del efod, sobre las hombreras, en la unión y sobre él cinto labrado.
21 Anamangirira mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi ija monga Yehova analamulira Mose.
Y los anillos en el pectoral se fijaron a los anillos del efod con una cuerda azul, manteniéndolo en su lugar sobre el cinto del mismo efod, para que él pectoral no se soltara, como el Señor le dio órdenes a Moisés.
22 Anayipangira efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo, wolukidwa ndi mmisiri waluso.
El manto que iba con el efod estaba hecho de azul;
23 Mkanjowo unali ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo panali chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
Con un agujero en la parte superior en el medio, como el agujero en el saco de un hombre luchador, bordeado con una banda para hacerlo fuerte.
24 Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, analumikiza mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yofewa yosalala ndi yopetedwa bwino yomwe inazungulira mkanjo.
Las faldas del manto se trabajaban en las orillas con granadas en azul y púrpura y rojo hechas de lino torcido.
25 Ndipo anapanga maberu agolide wabwino kwambiri ndipo analumikiza mozungulira mpendero pakati pa makangadzawo.
Y entre las granadas alrededor de la falda pusieron campanillas de oro, como el Señor le dio órdenes a Moisés.
26 Kotero panali mphonje imodzi ndi belu limodzi kuzungulira mpendero wa mkanjo wovala potumikira monga momwe Yehova analamulira Mose.
Alrededor de la falda de la túnica había campanas y granadas a su vez.
27 Kwa Aaroni ndi ana ake anawapangira minjiro ya nsalu yofewa yosalala, yolukidwa bwino ndi munthu waluso,
Los abrigos para Aarón y sus hijos hicieron del mejor lino;
28 nduwira ya nsalu yofewa yosalala, lamba wa nsalu yofewa yosalala, womanga mʼmutu, ndi makabudula amʼkati a nsalu yofewa yosalala olukidwa bwino.
Y la mitra para Aarón, y hermosos tocados de lino, y pantalones de lino,
29 Anapanga lamba wolukidwa bwino wa nsalu yofewa ndi yosalala ya mtundu wa mtambo yapepo ndi yofiira. Ili linaliluso la munthu wopanga zokometsera monga Yehova analamulira Mose.
Y una cinta de lino bordado con un diseño de azul, púrpura y rojo, como el Señor le había dicho a Moisés.
30 Iwo anapanga duwa lagolide wabwino kwambiri ngati chidindo ndipo anazokotapo mawu akuti, Wopatulikira Yehova.
La placa para la corona sagrada estaba hecha del mejor oro, y sobre ella se cortaron estas palabras: SANTIDAD AL SEÑOR.
31 Kenaka analimangira ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Fue fijado al tocado con una cuerda azul, como el Señor le había dado órdenes a Moisés.
32 Tsopano ntchito yonse ya tenti ya msonkhano inatha. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
Así que todo el trabajo del santuario, el santuario de reunión estaba hecho; como el Señor le había dado órdenes a Moisés, así lo hicieron los hijos de Israel.
33 Kenaka anabweretsa chihema kwa Mose. Tenti ndi zipangizo zake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
Entonces llevaron la tienda a Moisés, la tienda con todo lo necesario para ella; sus ganchos, sus tablas, sus varillas, sus columnas y sus basas;
34 chophimba cha chikopa cha nkhosa yayimuna chonyikidwa mu utoto ofiira, chophimba cha chikopa cha akatumbu ndi nsalu zophimba;
La cubierta exterior de piel de oveja de color rojo, y la cubierta de cuero, y el velo de la entrada;
35 bokosi la umboni pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake;
El cofre del pacto, con sus varas y él propiciatorio;
36 tebulo pamodzi ndi zipangizo zake ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
La mesa, con todos sus vasos y el pan santo;
37 choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri pamodzi ndi nyale zake ndi zipangizo zake zonse, ndiponso mafuta anyalezo;
El candelabro, con los recipientes para colocar las luces en sus lugares sobre él, y todos sus recipientes, y el aceite para las luces;
38 guwa lagolide, mafuta odzozera, lubani onunkhira ndi nsalu yotchinga pa khomo lolowera mu tenti;
Y el altar de oro, y el aceite sagrado, y él incienso aromático, y la cortina para la entrada de la tienda;
39 guwa lamkuwa ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse; beseni ndi miyendo yake;
Y el altar de bronce, con su parrilla de bronce, y sus varas, y todos sus utensilios, y el recipiente para lavatorio y su base;
40 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo; zingwe zake ndi zikhomo za tenti; zipangizo zonse za chihema, tenti ya msonkhano;
Las cortinas para el espacio abierto, con los pilares y sus basas, y la cortina para la entrada, y los cordones y estacas, y todos los instrumentos necesarios para el trabajo del santuario de la Tienda de reunión;
41 ndiponso zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.
Las túnicas para usar en el lugar santo, y las túnicas sagradas para Aarón y sus hijos cuando actúan como sacerdotes.
42 Aisraeli anagwira ntchito yonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
Los hijos de Israel hicieron todo lo que el Señor le había dado a Moisés.
43 Mose anayendera ntchitoyo ndipo anaona kuti anayichita monga momwe Yehova analamulira. Kotero Mose anawadalitsa.
Entonces Moisés, viendo todas sus obras, vio que habían hecho todo lo que el Señor había dicho, y les bendijo.