< Eksodo 39 >

1 Anapanga zovala za ansembe, zovala potumikira ku malo wopatulika pogwiritsa ntchito nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira. Anapanganso zovala zopatulika za Aaroni monga momwe Yehova analamulira Mose.
And of the blue, and purple, and scarlet, they made cloths of service, to do service in the holy place, and made the holy garments for Aaron; as the LORD commanded Moses.
2 Popanga efodi, iwo anagwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yosalala yofewa.
And he made the ephod of gold, blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen.
3 Anasula golide wopyapyala ndi kumulezaleza kuti alumikize kumodzi ndi nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yosalala yofewa yolukidwa mwaluso.
And they beat the gold into thin plates, and cut it into wires, to work it in the blue, and in the purple, and in the scarlet, and in the fine linen, with skilful work.
4 Iwo anapanga efodi imene inali ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa, tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
They made shoulderpieces for it, to couple it together: by the two edges was it coupled together.
5 Lamba womangira efodi anali wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Anali nsalu imodzi ndi efodiyo, wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
And the beautifully woven band of his ephod, that was upon it, was of the same, according to its work; of gold, blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen; as the LORD commanded Moses.
6 Iwo anakonza miyala ya onikisi ndi kuyiika mu zoyikamo zake zagolide ndipo anazokota mayina a ana a Israeli monga amachitira pa chidindo.
And they wrought onyx stones inclosed in settings of gold, engraved, as signets are engraved, with the names of the children of Israel.
7 Kenaka anayimangirira pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli monga momwe Yehova analamulira Mose.
And he put them on the shoulders of the ephod, that they should be stones for a memorial to the children of Israel; as the LORD commanded Moses.
8 Iwo anapanga chovala chapachifuwa mwaluso kwambiri. Anachipanga ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
And he made the breastplate of skilful work, like the work of the ephod; of gold, blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen.
9 Kutalika kwake kunali kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, chinali chopinda pawiri.
It was foursquare; they made the breastplate double: a span was the length of it, and a span the breadth of it, being doubled.
10 Kenaka anayikapo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba anayika miyala ya rubi, topazi ndi berili;
And they set in it four rows of stones: the first row was a sardius, a topaz, and a carbuncle: this was the first row.
11 mzere wachiwiri anayikapo miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
And the second row, an emerald, a sapphire, and a diamond.
12 mzere wachitatu anayikapo miyala ya opera, agate ndi ametisiti;
And the third row, a ligure, an agate, and an amethyst.
13 mzere wachinayi anayikapo miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi anayiyika mu zoyikamo zagolide.
And the fourth row, a beryl, an onyx, and a jasper: they were inclosed in settings of gold in their inclosings.
14 Miyalayo inalipo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse unazokotedwa ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
And the stones were according to the names of the children of Israel, twelve, according to their names, like the engravings of a signet, every one with his name, according to the twelve tribes.
15 Anapanga timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
And they made upon the breastplate chains at the ends, of braided work of pure gold.
16 Anapanganso zoyikamo zake zagolide ndi mphete ziwiri zagolide, ndipo anamangirira mphetezo pa ngodya ziwiri za chovala chapachifuwa.
And they made two settings of gold, and two gold rings; and put the two rings in the two ends of the breastplate.
17 Anamangirira timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
And they put the two braided chains of gold in the two rings on the ends of the breastplate.
18 Ndipo mbali ina ya timaunyoloto anamangirira pa zoyikapo zake ziwiri zija, ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
And the two ends of the two braided chains they fastened in the two settings, and put them on the shoulderpieces of the ephod, before it.
19 Anapanganso mphete ziwiri zagolide ndipo analumikiza ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
And they made two rings of gold, and put them on the two ends of the breastplate, upon the border of it, which was on the side of the ephod inward.
20 Kenaka anapanga mphete zina ziwiri zagolide ndi kuzilumikiza kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
And they made two other golden rings, and put them on the two sides of the ephod underneath, toward the forepart of it, opposite its other coupling, above the beautifully woven band of the ephod.
21 Anamangirira mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi ija monga Yehova analamulira Mose.
And they bound the breastplate by its rings to the rings of the ephod with a lace of blue, that it might be above the beautifully woven band of the ephod, and that the breastplate might not be loosed from the ephod; as the LORD commanded Moses.
22 Anayipangira efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo, wolukidwa ndi mmisiri waluso.
And he made the robe of the ephod of woven work, all of blue.
23 Mkanjowo unali ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo panali chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
And there was an hole in the midst of the robe, as the hole of a coat of mail, with a band around the hole, that it should not rend.
24 Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, analumikiza mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yofewa yosalala ndi yopetedwa bwino yomwe inazungulira mkanjo.
And they made upon the hems of the robe pomegranates of blue, and purple, and scarlet, and twined linen.
25 Ndipo anapanga maberu agolide wabwino kwambiri ndipo analumikiza mozungulira mpendero pakati pa makangadzawo.
And they made bells of pure gold, and put the bells between the pomegranates upon the hem of the robe, around between the pomegranates;
26 Kotero panali mphonje imodzi ndi belu limodzi kuzungulira mpendero wa mkanjo wovala potumikira monga momwe Yehova analamulira Mose.
A bell and a pomegranate, a bell and a pomegranate, around the hem of the robe to minister in; as the LORD commanded Moses.
27 Kwa Aaroni ndi ana ake anawapangira minjiro ya nsalu yofewa yosalala, yolukidwa bwino ndi munthu waluso,
And they made coats of fine linen of woven work for Aaron, and for his sons,
28 nduwira ya nsalu yofewa yosalala, lamba wa nsalu yofewa yosalala, womanga mʼmutu, ndi makabudula amʼkati a nsalu yofewa yosalala olukidwa bwino.
And a mitre of fine linen, and goodly headdresses of fine linen, and linen breeches of fine twined linen,
29 Anapanga lamba wolukidwa bwino wa nsalu yofewa ndi yosalala ya mtundu wa mtambo yapepo ndi yofiira. Ili linaliluso la munthu wopanga zokometsera monga Yehova analamulira Mose.
And a waistband of fine twined linen, and blue, and purple, and scarlet, of needlework; as the LORD commanded Moses.
30 Iwo anapanga duwa lagolide wabwino kwambiri ngati chidindo ndipo anazokotapo mawu akuti, Wopatulikira Yehova.
And they made the plate of the holy crown of pure gold, and wrote upon it a writing, like the engravings of a signet, HOLINESS TO THE LORD.
31 Kenaka analimangira ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira, monga momwe Yehova analamulira Mose.
And they tied to it a lace of blue, to fasten it on high upon the mitre; as the LORD commanded Moses.
32 Tsopano ntchito yonse ya tenti ya msonkhano inatha. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
Thus was all the work of the tabernacle of the tent of the congregation finished: and the children of Israel did according to all that the LORD commanded Moses, so did they.
33 Kenaka anabweretsa chihema kwa Mose. Tenti ndi zipangizo zake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
And they brought the tabernacle to Moses, the tent, and all its furniture, its clasps, its boards, its bars, and its pillars, and its sockets,
34 chophimba cha chikopa cha nkhosa yayimuna chonyikidwa mu utoto ofiira, chophimba cha chikopa cha akatumbu ndi nsalu zophimba;
And the covering of rams’ skins dyed red, and the covering of badgers’ skins, and the veil of the covering,
35 bokosi la umboni pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake;
The ark of the testimony, and its staffs, and the mercy seat,
36 tebulo pamodzi ndi zipangizo zake ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
The table, and all its vessels, and the showbread,
37 choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri pamodzi ndi nyale zake ndi zipangizo zake zonse, ndiponso mafuta anyalezo;
The pure lampstand, with its lamps, even with the lamps to be set in order, and all its vessels, and the oil for light,
38 guwa lagolide, mafuta odzozera, lubani onunkhira ndi nsalu yotchinga pa khomo lolowera mu tenti;
And the golden altar, and the anointing oil, and the sweet incense, and the hanging for the tabernacle door,
39 guwa lamkuwa ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse; beseni ndi miyendo yake;
The brasen altar, and its grate of brass, its staffs, and all its vessels, the laver and its foot,
40 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo; zingwe zake ndi zikhomo za tenti; zipangizo zonse za chihema, tenti ya msonkhano;
The hangings of the court, its pillars, and its sockets, and the hanging for the court gate, its cords, and its pins, and all the vessels of the service of the tabernacle, for the tent of the congregation,
41 ndiponso zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.
The cloths of service to do service in the holy place, and the holy garments for Aaron the priest, and his sons’ garments, to minister in the priest’s office.
42 Aisraeli anagwira ntchito yonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
According to all that the LORD commanded Moses, so the children of Israel made all the work.
43 Mose anayendera ntchitoyo ndipo anaona kuti anayichita monga momwe Yehova analamulira. Kotero Mose anawadalitsa.
And Moses looked upon all the work, and, behold, they had done it as the LORD had commanded, even so had they done it: and Moses blessed them.

< Eksodo 39 >