< Eksodo 39 >

1 Anapanga zovala za ansembe, zovala potumikira ku malo wopatulika pogwiritsa ntchito nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira. Anapanganso zovala zopatulika za Aaroni monga momwe Yehova analamulira Mose.
And of the blue, and purple, and scarlet yarn, they made the cloths of service, to do the service in the holy place; and they made the holy garments which were for Aaron, as the Lord had commanded Moses.
2 Popanga efodi, iwo anagwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yosalala yofewa.
And he made the ephod, of gold, blue, and purple, and scarlet yarn, and twisted linen;
3 Anasula golide wopyapyala ndi kumulezaleza kuti alumikize kumodzi ndi nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yosalala yofewa yolukidwa mwaluso.
And they did heat the gold into thin plates, and cut it into wires, to work it in the blue, and in the purple, and in the scarlet yarn, and in the linen, with weaver's work.
4 Iwo anapanga efodi imene inali ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa, tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
They made shoulder-pieces for it, joined on; on both its edges was it thus joined together.
5 Lamba womangira efodi anali wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Anali nsalu imodzi ndi efodiyo, wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
And the belt for girding it on, that was upon it, was of the same piece with itself, of the same make: of gold, blue, and purple, and scarlet yarn, and twisted linen; as the Lord had commanded Moses.
6 Iwo anakonza miyala ya onikisi ndi kuyiika mu zoyikamo zake zagolide ndipo anazokota mayina a ana a Israeli monga amachitira pa chidindo.
And they wrought the onyx stones enclosed in casings of gold, engraved with the engraving of a signet, after the names of the children of Israel.
7 Kenaka anayimangirira pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli monga momwe Yehova analamulira Mose.
And he put them on the shoulder-pieces of the ephod, as stones of memorial to the children of Israel; as the Lord had commanded Moses.
8 Iwo anapanga chovala chapachifuwa mwaluso kwambiri. Anachipanga ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
And he made the breastplate with weaver's work, like the work of the ephod: of gold, blue, and purple, and scarlet yarn, and twisted linen.
9 Kutalika kwake kunali kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, chinali chopinda pawiri.
It was foursquare, double did they make the breastplate: it was a span in length, and a span in breadth, double.
10 Kenaka anayikapo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba anayika miyala ya rubi, topazi ndi berili;
And they set in it four rows of stones: the first row, a sardius, a topaz, and an emerald; this was the first row.
11 mzere wachiwiri anayikapo miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
And the second row, a carbuncle, a sapphire, and a diamond.
12 mzere wachitatu anayikapo miyala ya opera, agate ndi ametisiti;
And the third row, an opal, a turquoise, and an amethyst.
13 mzere wachinayi anayikapo miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi anayiyika mu zoyikamo zagolide.
And the fourth row, a chrysolite, an onyx, and a jasper: they were fitted in golden casings when they were set in.
14 Miyalayo inalipo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse unazokotedwa ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
And the stones were according to the names of the children of Israel, twelve, according to their names, [engraved] with the engraving of a signet, every one according to his name, for the twelve tribes.
15 Anapanga timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
And they made upon the breastplate chains with knots at the ends, of wreathed work, of pure gold.
16 Anapanganso zoyikamo zake zagolide ndi mphete ziwiri zagolide, ndipo anamangirira mphetezo pa ngodya ziwiri za chovala chapachifuwa.
And they made two casings of gold, and two golden rings; and they put the two rings on the two ends of the breastplate.
17 Anamangirira timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
And they put the two wreathed chains of gold in the two rings on the ends of the breastplate.
18 Ndipo mbali ina ya timaunyoloto anamangirira pa zoyikapo zake ziwiri zija, ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
And the two ends of the two wreathed chains they fastened on the two casings, and they put them on the shoulder-pieces of the ephod, on the outside thereof.
19 Anapanganso mphete ziwiri zagolide ndipo analumikiza ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
And they made two golden rings, and put them on the two ends of the breastplate, on its border, which was on the opposite side of the ephod, inward.
20 Kenaka anapanga mphete zina ziwiri zagolide ndi kuzilumikiza kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
And they made two more golden rings, and put them on the two shoulder-pieces of the ephod underneath, toward its front part, close by its seam, above the girdle of the ephod.
21 Anamangirira mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi ija monga Yehova analamulira Mose.
And they fastened the breastplate by its rings unto the rings of the ephod with a lace of blue, that it might remain on the girdle of the ephod, and that the breastplate might not be loosed from the ephod; as the Lord had commanded Moses.
22 Anayipangira efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo, wolukidwa ndi mmisiri waluso.
And he made the robe of the ephod of woven work, altogether of blue woolen yarn.
23 Mkanjowo unali ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo panali chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
And there was an opening in the midst of the robe, as the opening of a habergeon, with a binding round about the opening, that it should not be rent.
24 Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, analumikiza mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yofewa yosalala ndi yopetedwa bwino yomwe inazungulira mkanjo.
And they made upon the lower hem of the robe pomegranates of blue, and purple, and scarlet yarn, twisted.
25 Ndipo anapanga maberu agolide wabwino kwambiri ndipo analumikiza mozungulira mpendero pakati pa makangadzawo.
And they made bells of pure gold; and they put the bells between the pomegranates upon the lower hem of the robe, round about, between the pomegranates;
26 Kotero panali mphonje imodzi ndi belu limodzi kuzungulira mpendero wa mkanjo wovala potumikira monga momwe Yehova analamulira Mose.
A bell and a pomegranate, a bell and a pomegranate, round about the lower hem of the robe, to minister therein; as the Lord had commanded Moses.
27 Kwa Aaroni ndi ana ake anawapangira minjiro ya nsalu yofewa yosalala, yolukidwa bwino ndi munthu waluso,
And they made the coats of linen, of woven work, for Aaron and for his sons,
28 nduwira ya nsalu yofewa yosalala, lamba wa nsalu yofewa yosalala, womanga mʼmutu, ndi makabudula amʼkati a nsalu yofewa yosalala olukidwa bwino.
And the mitre of linen, and the goodly bonnets of linen, and linen breeches of twisted linen thread.
29 Anapanga lamba wolukidwa bwino wa nsalu yofewa ndi yosalala ya mtundu wa mtambo yapepo ndi yofiira. Ili linaliluso la munthu wopanga zokometsera monga Yehova analamulira Mose.
And the girdle of twisted linen, and blue, and purple, and scarlet yarn, the work of the embroiderer; as the Lord had commanded Moses.
30 Iwo anapanga duwa lagolide wabwino kwambiri ngati chidindo ndipo anazokotapo mawu akuti, Wopatulikira Yehova.
And they made the plate of the holy crown of pure gold, and wrote upon it a writing, like the engrafting of a signet, Holy to the Lord.
31 Kenaka analimangira ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira, monga momwe Yehova analamulira Mose.
And they put on it a lace of blue, to place it upon the mitre above; as the Lord had commanded Moses.
32 Tsopano ntchito yonse ya tenti ya msonkhano inatha. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
Thus was finished all the work of the tabernacle of the tent of the congregation; and the children of Israel had made it in accordance with all that the Lord had commanded Moses, so had they made it.
33 Kenaka anabweretsa chihema kwa Mose. Tenti ndi zipangizo zake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
And they brought the tabernacle unto Moses, the tent, and all its vessels, its hooks, its boards, its bars, and its pillars, and its sockets,
34 chophimba cha chikopa cha nkhosa yayimuna chonyikidwa mu utoto ofiira, chophimba cha chikopa cha akatumbu ndi nsalu zophimba;
And the covering of rams' skins dyed red, and the covering of badgers' skins, and the vail of the separation:
35 bokosi la umboni pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake;
The ark of the testimony, and its staves, and the mercy-seat;
36 tebulo pamodzi ndi zipangizo zake ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
The table, and all its vessels, and the showbread;
37 choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri pamodzi ndi nyale zake ndi zipangizo zake zonse, ndiponso mafuta anyalezo;
The pure candlestick, with its lamps, the lamps to be set in order thereupon, and all its vessels, and the oil for the lighting,
38 guwa lagolide, mafuta odzozera, lubani onunkhira ndi nsalu yotchinga pa khomo lolowera mu tenti;
And the golden altar, and the anointing oil, and the incense of spices, and the hanging for the door of the tabernacle;
39 guwa lamkuwa ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse; beseni ndi miyendo yake;
The copper altar, and the grating of copper which belonged to it, its staves, and all its vessels, the laver and its foot;
40 nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo; zingwe zake ndi zikhomo za tenti; zipangizo zonse za chihema, tenti ya msonkhano;
The hangings of the court, its pillars and its sockets, and the hanging for the court-gate, its cords, and its pins, and all the vessels of the service of the tabernacle, for the tent of the congregation;
41 ndiponso zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.
The cloths of service to do the service in the holy place, and the holy garments for Aaron the priest, and the garments of his sons, to minister therein.
42 Aisraeli anagwira ntchito yonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
All, just as the Lord had commanded Moses, so had the children of Israel done all the work.
43 Mose anayendera ntchitoyo ndipo anaona kuti anayichita monga momwe Yehova analamulira. Kotero Mose anawadalitsa.
And Moses did look over all the work, and, behold, they had done it as the Lord had commanded, even so had they done it: and Moses blessed them.

< Eksodo 39 >