< Eksodo 37 >

1 Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
And Bezaleel made the ark of shittim wood: two cubits and a half was the length of it, and a cubit and a half the breadth of it, and a cubit and a half the height of it:
2 Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
And he overlaid it with pure gold within and without, and made a crown of gold for it all around.
3 Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
And he cast for it four rings of gold, to be set by its four corners; even two rings upon its one side, and two rings upon its other side
4 Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
And he made staffs of shittim wood, and overlaid them with gold.
5 Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
And he put the staffs into the rings by the sides of the ark, to bear the ark.
6 Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
And he made the mercy seat of pure gold: two cubits and a half was the length of it, and one cubit and a half the breadth of it.
7 Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho.
And he made two cherubim of gold, beaten out of one piece he made them, on the two ends of the mercy seat;
8 Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
One cherub on the end on this side, and another cherub on the other end on that side: out of the mercy seat made he the cherubim on its two ends.
9 Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
And the cherubim spread out their wings on high, and covered with their wings over the mercy seat, with their faces one to another; even toward the mercy seat were the faces of the cherubim.
10 Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
And he made the table of shittim wood: two cubits was its length, and a cubit its breadth, and a cubit and a half its height:
11 Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake.
And he overlaid it with pure gold, and made for it a crown of gold all around.
12 Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
Also he made for it a border of an handbreadth all around; and made a crown of gold for its border all around.
13 Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi.
And he cast for it four rings of gold, and put the rings upon the four corners that were in its four feet.
14 Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
Close to the border were the rings, the places for the staffs to bear the table.
15 Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
And he made the staffs of shittim wood, and overlaid them with gold, to bear the table.
16 Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.
And he made the vessels which were upon the table, its dishes, and its spoons, and its bowls, and its covers to cover with, of pure gold.
17 Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi.
And he made the lampstand of pure gold: of beaten work he made the lampstand; its shaft, and its branch, its bowls, its knobs, and its flowers, were of the same:
18 Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
And six branches proceeding from its sides; three branches of the lampstand from the one side of it, and three branches of the lampstand from its other side:
19 Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho.
Three bowls made after the fashion of almonds in one branch, a knob and a flower; and three bowls made like almonds in another branch, a knob and a flower: so throughout the six branches going out of the lampstand.
20 Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake.
And in the lampstand were four bowls made like almonds, its knobs, and its flowers:
21 Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi
And a knob under two branches of the same, and a knob under two branches of the same, and a knob under two branches of the same, according to the six branches going out of it.
22 Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
Their knobs and their branches were of the same: all of it was one beaten work of pure gold.
23 Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri.
And he made its seven lamps, and its snuffers, and its snuffdishes, of pure gold.
24 Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
Of a talent of pure gold he made it, and all its vessels.
25 Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo.
And he made the incense altar of shittim wood: the length of it was a cubit, and the breadth of it a cubit; it was foursquare; and two cubits was the height of it; the horns of it were of the same.
26 Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
And he overlaid it with pure gold, both the top of it, and its sides all around, and its horns: also he made for it a crown of gold all around.
27 Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira.
And he made two rings of gold for it under its crown, by its two corners, upon its two sides, to be places for the staffs to bear it with.
28 Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.
And he made the staffs of shittim wood, and overlaid them with gold.
29 Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.
And he made the holy anointing oil, and the pure incense of sweet spices, according to the work of the perfumer.

< Eksodo 37 >