< Eksodo 37 >

1 Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
And Bezaleel made the ark [of] shittim wood: two cubits and a half [was] the length of it, and a cubit and a half the breadth of it, and a cubit and a half the height of it:
2 Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
And he overlaid it with pure gold within and without, and made a crown of gold to it round about.
3 Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
And he cast for it four rings of gold, [to be set] by the four corners of it; even two rings upon the one side of it, and two rings upon the other side of it.
4 Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
And he made staves [of] shittim wood, and overlaid them with gold.
5 Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
And he put the staves into the rings by the sides of the ark, to bear the ark.
6 Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
And he made the mercy seat [of] pure gold: two cubits and a half [was] the length thereof, and one cubit and a half the breadth thereof.
7 Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho.
And he made two cherubims [of] gold, beaten out of one piece made he them, on the two ends of the mercy seat;
8 Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
One cherub on the end on this side, and another cherub on the [other] end on that side: out of the mercy seat made he the cherubims on the two ends thereof.
9 Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
And the cherubims spread out [their] wings on high, [and] covered with their wings over the mercy seat, with their faces one to another; [even] to the mercy seatward were the faces of the cherubims.
10 Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
And he made the table [of] shittim wood: two cubits [was] the length thereof, and a cubit the breadth thereof, and a cubit and a half the height thereof:
11 Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake.
And he overlaid it with pure gold, and made thereunto a crown of gold round about.
12 Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
Also he made thereunto a border of an handbreadth round about; and made a crown of gold for the border thereof round about.
13 Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi.
And he cast for it four rings of gold, and put the rings upon the four corners that [were] in the four feet thereof.
14 Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
Over against the border were the rings, the places for the staves to bear the table.
15 Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
And he made the staves [of] shittim wood, and overlaid them with gold, to bear the table.
16 Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.
And he made the vessels which [were] upon the table, his dishes, and his spoons, and his bowls, and his covers to cover withal, [of] pure gold.
17 Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi.
And he made the candlestick [of] pure gold: [of] beaten work made he the candlestick; his shaft, and his branch, his bowls, his knops, and his flowers, were of the same:
18 Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
And six branches going out of the sides thereof; three branches of the candlestick out of the one side thereof, and three branches of the candlestick out of the other side thereof:
19 Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho.
Three bowls made after the fashion of almonds in one branch, a knop and a flower; and three bowls made like almonds in another branch, a knop and a flower: so throughout the six branches going out of the candlestick.
20 Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake.
And in the candlestick [were] four bowls made like almonds, his knops, and his flowers:
21 Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi
And a knop under two branches of the same, and a knop under two branches of the same, and a knop under two branches of the same, according to the six branches going out of it.
22 Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
Their knops and their branches were of the same: all of it [was] one beaten work [of] pure gold.
23 Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri.
And he made his seven lamps, and his snuffers, and his snuffdishes, [of] pure gold.
24 Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
[Of] a talent of pure gold made he it, and all the vessels thereof.
25 Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo.
And he made the incense altar [of] shittim wood: the length of it [was] a cubit, and the breadth of it a cubit; [it was] foursquare; and two cubits [was] the height of it; the horns thereof were of the same.
26 Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
And he overlaid it with pure gold, [both] the top of it, and the sides thereof round about, and the horns of it: also he made unto it a crown of gold round about.
27 Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira.
And he made two rings of gold for it under the crown thereof, by the two corners of it, upon the two sides thereof, to be places for the staves to bear it withal.
28 Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.
And he made the staves [of] shittim wood, and overlaid them with gold.
29 Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.
And he made the holy anointing oil, and the pure incense of sweet spices, according to the work of the apothecary.

< Eksodo 37 >